Check out the new design

Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ * - Lexique des traductions


Traduction des sens Sourate: Yûsuf   Verset:
قَالَ مَعَاذَ ٱللَّهِ أَن نَّأۡخُذَ إِلَّا مَن وَجَدۡنَا مَتَٰعَنَا عِندَهُۥٓ إِنَّآ إِذٗا لَّظَٰلِمُونَ
(Yûsuf) adati: “Ha! tikudzitchinjiriza mwa Allah, sitingagwire wina koma yemwe chuma chathu tachipeza ndi iye, kuopa kuti tingakhale ochita zoipa.”
Les exégèses en arabe:
فَلَمَّا ٱسۡتَيۡـَٔسُواْ مِنۡهُ خَلَصُواْ نَجِيّٗاۖ قَالَ كَبِيرُهُمۡ أَلَمۡ تَعۡلَمُوٓاْ أَنَّ أَبَاكُمۡ قَدۡ أَخَذَ عَلَيۡكُم مَّوۡثِقٗا مِّنَ ٱللَّهِ وَمِن قَبۡلُ مَا فَرَّطتُمۡ فِي يُوسُفَۖ فَلَنۡ أَبۡرَحَ ٱلۡأَرۡضَ حَتَّىٰ يَأۡذَنَ لِيٓ أَبِيٓ أَوۡ يَحۡكُمَ ٱللَّهُ لِيۖ وَهُوَ خَيۡرُ ٱلۡحَٰكِمِينَ
Choncho, pamene adataya mtima za iye, adapita pambali kukanong’onezana. Wamkulu wawo adati: “Kodi simudziwa kuti bambo wanu adatenga lonjezo kuchokera kwa inu m’dzina la Allah (kuti mudzam’bweza iyeyo?) ndiponso kale mudalakwa (pa mapangano anu) pa za Yûsuf. Choncho sindichoka dziko lino kufikira atandilola bambo (kutero) kapena Allah andilamule (zondichotsa kuno pomasulidwa m’bale wangayu); Iye Ngwabwino polamula kuposa olamula.”
Les exégèses en arabe:
ٱرۡجِعُوٓاْ إِلَىٰٓ أَبِيكُمۡ فَقُولُواْ يَٰٓأَبَانَآ إِنَّ ٱبۡنَكَ سَرَقَ وَمَا شَهِدۡنَآ إِلَّا بِمَا عَلِمۡنَا وَمَا كُنَّا لِلۡغَيۡبِ حَٰفِظِينَ
“Bwererani kwa bambo wanu ndipo mukawauze (kuti): “E bambo wathu! Ndithu mwana wanu waba. Ndipo ife sitidaikire umboni (wakuti wakuba achitidwe ukapolo) koma pa zomwe tidazidziwa (kuti mwa ife mulibe wakuba), ndipo sitidali kudziwa zamseri.”
Les exégèses en arabe:
وَسۡـَٔلِ ٱلۡقَرۡيَةَ ٱلَّتِي كُنَّا فِيهَا وَٱلۡعِيرَ ٱلَّتِيٓ أَقۡبَلۡنَا فِيهَاۖ وَإِنَّا لَصَٰدِقُونَ
“Ndipo afunseni anthu a m’mudzi momwe tidalimo ndi a pa ulendo omwe tadza nawo, ndipo ndithudi ife tikunena zoona.”
Les exégèses en arabe:
قَالَ بَلۡ سَوَّلَتۡ لَكُمۡ أَنفُسُكُمۡ أَمۡرٗاۖ فَصَبۡرٞ جَمِيلٌۖ عَسَى ٱللَّهُ أَن يَأۡتِيَنِي بِهِمۡ جَمِيعًاۚ إِنَّهُۥ هُوَ ٱلۡعَلِيمُ ٱلۡحَكِيمُ
(Ya’qub) adati: “Koma mitima yanu yakukometserani chinthu. (Kwanga ndi) kupirira kwabwino kokha basi. Mwina Allah adzandibweretsera onse pamodzi. Ndithudi, Iye Ngodziwa, Ngwanzeru zakuya.”
Les exégèses en arabe:
وَتَوَلَّىٰ عَنۡهُمۡ وَقَالَ يَٰٓأَسَفَىٰ عَلَىٰ يُوسُفَ وَٱبۡيَضَّتۡ عَيۡنَاهُ مِنَ ٱلۡحُزۡنِ فَهُوَ كَظِيمٞ
Ndipo adawachokera ndikunena (kuti): “Ha! kudandaula kwanga za Yûsuf!” Ndipo maso ake adayera chifukwa cha kudandaula ndipo iye adadzazidwa ndi chisoni.
Les exégèses en arabe:
قَالُواْ تَٱللَّهِ تَفۡتَؤُاْ تَذۡكُرُ يُوسُفَ حَتَّىٰ تَكُونَ حَرَضًا أَوۡ تَكُونَ مِنَ ٱلۡهَٰلِكِينَ
(Iwo) adati: “Tikulumbira Allah! Simusiya kumkumbukira Yûsuf (ndikulira) mpaka mufika podwala, kapena mukhala mwa owonongeka (ndi imfa).”
Les exégèses en arabe:
قَالَ إِنَّمَآ أَشۡكُواْ بَثِّي وَحُزۡنِيٓ إِلَى ٱللَّهِ وَأَعۡلَمُ مِنَ ٱللَّهِ مَا لَا تَعۡلَمُونَ
(Iye) adati: “Ndithu ine ndikusuma dandaulo langa ndi kukhumata kwanga kwa Allah, ndipo ndikudziwa kupyolera mwa Allah zomwe simukudziwa.”
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Sourate: Yûsuf
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ - Lexique des traductions

Traduit par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ.

Fermeture