د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه * - د ژباړو فهرست (لړلیک)


د معناګانو ژباړه آیت: (236) سورت: البقرة
لَّا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ إِن طَلَّقۡتُمُ ٱلنِّسَآءَ مَا لَمۡ تَمَسُّوهُنَّ أَوۡ تَفۡرِضُواْ لَهُنَّ فَرِيضَةٗۚ وَمَتِّعُوهُنَّ عَلَى ٱلۡمُوسِعِ قَدَرُهُۥ وَعَلَى ٱلۡمُقۡتِرِ قَدَرُهُۥ مَتَٰعَۢا بِٱلۡمَعۡرُوفِۖ حَقًّا عَلَى ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Palibe tchimo pa inu mutawapatsa akazi mawu achilekaniro pomwe simudakhudzane nawo; pomwenso simudawadziwitse gawo la chiwongo chawo; koma asangalatseni (powapatsa chilekaniro). Wopeza bwino apereke malinga ndikupeza bwino kwake; wochepekedwa apereke malingana ndikuchepekedwa kwake. Chilekaniro chosangalatsacho chikhale molingana ndi malamulo a Shariya, ndipo ndilamulo kwa ochita zabwino.[39]
[39] Kuthetsa ukwati nkololedwa m’Chisilamu. Koma ngakhale nkololedwa, Shariya ya Chisilamu imanyansidwa ndimachitidwe othetsa ukwati pokhapokha pakhale zifukwa zovomerezeka ndi Shariya.
Ngati patapezeka zifukwa zochititsa kuti ukwati uthe nkofunika kuti mkwati amchitire mkwatibwi zabwino monga izi:
a) ampatse chiwongo (mahar) chimene chinatsalira ngati sadamalize kupereka.
b) ampatse ndalama zina zapadera zomtulutsira mkaziyo m’nyumba.
c) ampatse chovala, malo okhala, chakudya patsiku lililonse kufikira edda yake itatha ngakhale eddayo itatenga nthawi yaitali.
d) amsiire zinthu zake kuti atenge pamodzi ndi zimene adampatsa. Nkosaloledwa kumlanda chilichonse mwa zimenezi.
عربي تفسیرونه:
 
د معناګانو ژباړه آیت: (236) سورت: البقرة
د سورتونو فهرست (لړلیک) د مخ نمبر
 
د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - د ژباړو فهرست (لړلیک)

چیچوایي ژبې ته د قرآن کریم د معناګانو ژباړه، خالد ابراهیم بیتالا ژباړلې ده، ۲۰۲۰ کال چاپ

بندول