แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา * - สารบัญ​คำแปล


แปลความหมาย​ อายะฮ์: (236) สูเราะฮ์: Al-Baqarah
لَّا جُنَاحَ عَلَيۡكُمۡ إِن طَلَّقۡتُمُ ٱلنِّسَآءَ مَا لَمۡ تَمَسُّوهُنَّ أَوۡ تَفۡرِضُواْ لَهُنَّ فَرِيضَةٗۚ وَمَتِّعُوهُنَّ عَلَى ٱلۡمُوسِعِ قَدَرُهُۥ وَعَلَى ٱلۡمُقۡتِرِ قَدَرُهُۥ مَتَٰعَۢا بِٱلۡمَعۡرُوفِۖ حَقًّا عَلَى ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Palibe tchimo pa inu mutawapatsa akazi mawu achilekaniro pomwe simudakhudzane nawo; pomwenso simudawadziwitse gawo la chiwongo chawo; koma asangalatseni (powapatsa chilekaniro). Wopeza bwino apereke malinga ndikupeza bwino kwake; wochepekedwa apereke malingana ndikuchepekedwa kwake. Chilekaniro chosangalatsacho chikhale molingana ndi malamulo a Shariya, ndipo ndilamulo kwa ochita zabwino.[39]
[39] Kuthetsa ukwati nkololedwa m’Chisilamu. Koma ngakhale nkololedwa, Shariya ya Chisilamu imanyansidwa ndimachitidwe othetsa ukwati pokhapokha pakhale zifukwa zovomerezeka ndi Shariya.
Ngati patapezeka zifukwa zochititsa kuti ukwati uthe nkofunika kuti mkwati amchitire mkwatibwi zabwino monga izi:
a) ampatse chiwongo (mahar) chimene chinatsalira ngati sadamalize kupereka.
b) ampatse ndalama zina zapadera zomtulutsira mkaziyo m’nyumba.
c) ampatse chovala, malo okhala, chakudya patsiku lililonse kufikira edda yake itatha ngakhale eddayo itatenga nthawi yaitali.
d) amsiire zinthu zake kuti atenge pamodzi ndi zimene adampatsa. Nkosaloledwa kumlanda chilichonse mwa zimenezi.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
 
แปลความหมาย​ อายะฮ์: (236) สูเราะฮ์: Al-Baqarah
สารบัญสูเราะฮ์ หมายเลข​หน้า​
 
แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - สารบัญ​คำแปล

การแปลความหมายอัลกุรอานเป็นภาษาชิเชวา แปลโดย คอลิด อิบรอฮีม เบตาลา (ed. 2020)

ปิด