Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Asr   Versículo:

Suratu Al-Asr

وَٱلۡعَصۡرِ
Ndikuilumbilira nthawi.[480]
[480] Chinthu cha mtengo wapatali kwa munthu pa dziko lino ndi moyo wake. Choncho mphindi iliyonse imene akuigwiritsa ntchito pa zinthu zabwino ndiyo imene idzamuthandiza. Ndipo mphindi iliyonse imene akuigwiritsa ntchito mu zinthu zoipa kapena zopanda pake, kumeneko ndiko kutaika kwake; (kuluza).
Os Tafssir em língua árabe:
إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لَفِي خُسۡرٍ
Ndithu munthu aliyense ndi wotaika (chifukwa chakugonjetsedwa ndi zilakolako zake).
Os Tafssir em língua árabe:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلۡحَقِّ وَتَوَاصَوۡاْ بِٱلصَّبۡرِ
Kupatula amene akhulupirira (mwa Allah) ndi kumachita zabwino, ndikumalangizana kutsatira choona ndiponso ndi kumalangizana za kupirira (potsatira malamulo a Allah ndi zina za mdziko).[481]
[481] Mgulu la otaika mwapatulidwa anthu olungama amene zochita zawo zili zolungama, omwe amalamulira kutsatira njira yolungama ndi kupilira. Anthu otere saataika, chifukwa chakuti nthawi yawo amaigwiritsira ntchito pa zinthu zabwino, zowathandiza padziko ndi pambuyo pa imfa. Kupilira kulipo mitundu inayi:-
(a) Kupilira pochita zinthu zabwino zomwe zili zovuta kwa munthu kuzipitiriza, monga kupemphera Swala zisanu.
(b) Kupilira posiya kuchita zoipa zimene zili zovuta kwa munthu kuti azileke.
(c) Kuwapilira anthu anzako; kupilira ndi zoipa zawo posawabwezera choipa chilichonse.
(d) Kupilira ndi mazunzo a padziko, monga njala, matenda, kusauka ndi zina zotero.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Asr
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar