Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Versículo: (260) Surah: Suratu Al-Baqarah
وَإِذۡ قَالَ إِبۡرَٰهِـۧمُ رَبِّ أَرِنِي كَيۡفَ تُحۡيِ ٱلۡمَوۡتَىٰۖ قَالَ أَوَلَمۡ تُؤۡمِنۖ قَالَ بَلَىٰ وَلَٰكِن لِّيَطۡمَئِنَّ قَلۡبِيۖ قَالَ فَخُذۡ أَرۡبَعَةٗ مِّنَ ٱلطَّيۡرِ فَصُرۡهُنَّ إِلَيۡكَ ثُمَّ ٱجۡعَلۡ عَلَىٰ كُلِّ جَبَلٖ مِّنۡهُنَّ جُزۡءٗا ثُمَّ ٱدۡعُهُنَّ يَأۡتِينَكَ سَعۡيٗاۚ وَٱعۡلَمۡ أَنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٞ
Ndipo (kumbukira) pamene Ibrahim adati: “E Mbuye wanga!, Ndionetseni mmene mudzaaukitsire akufa.” (Allah) adati: “Kodi sunakhulupirirebe?” Adati: “Iyayi, (ndikukhulupirira), koma (ndikufuna kuona zimenezo) kuti mtima wanga ukhazikike.” (Allah) adati: “Choncho katenge mbalame zinayi; uzisonkhanitse kwa iwe (mpaka uyizindikire mbalame iliyonse mmene ilili, ndipo kenako uziduledule zonsezo zidutswazidutswa ndikuzisakaniza ndi kuzigawa mzigawo zinayi). Ndipo paphiri lililonse ukaikepo gawo limodzi la zimenezo, ndipo kenako uziitane. Zikudzera zikuthamanga. Ndipo dziwa kuti Allah ndi Mwini mphamvu zoposa, Ngwanzem zakuya.”[52]
[52] Mneneri Ibrahim adalakalaka kuti aone mmene akufa adzaukira kuti chikhulupiliro chake chiwonjezeke mphamvu. Tero Allah adamulamula kuti azinge mbalame zinayi zosiyanasiyana mitundu. Kenako azisakanize ziwalo zake. Ziwalo za mbalame ina zilowe kumbalame ina. Tsono azigawe miyulu inayi. Mulu uliwonse akauike pa phiri lakelake. Kenako aziitane mbalame zija. Ndipo aona kuti chiwalo chilichonse chikuthamangira kumbalame yake, pompo zonsezo zikhalanso mbalame zamoyo monga momwe zidalili poyamba.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Versículo: (260) Surah: Suratu Al-Baqarah
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar