クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 節: (260) 章: 雌牛章
وَإِذۡ قَالَ إِبۡرَٰهِـۧمُ رَبِّ أَرِنِي كَيۡفَ تُحۡيِ ٱلۡمَوۡتَىٰۖ قَالَ أَوَلَمۡ تُؤۡمِنۖ قَالَ بَلَىٰ وَلَٰكِن لِّيَطۡمَئِنَّ قَلۡبِيۖ قَالَ فَخُذۡ أَرۡبَعَةٗ مِّنَ ٱلطَّيۡرِ فَصُرۡهُنَّ إِلَيۡكَ ثُمَّ ٱجۡعَلۡ عَلَىٰ كُلِّ جَبَلٖ مِّنۡهُنَّ جُزۡءٗا ثُمَّ ٱدۡعُهُنَّ يَأۡتِينَكَ سَعۡيٗاۚ وَٱعۡلَمۡ أَنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٞ
Ndipo (kumbukira) pamene Ibrahim adati: “E Mbuye wanga!, Ndionetseni mmene mudzaaukitsire akufa.” (Allah) adati: “Kodi sunakhulupirirebe?” Adati: “Iyayi, (ndikukhulupirira), koma (ndikufuna kuona zimenezo) kuti mtima wanga ukhazikike.” (Allah) adati: “Choncho katenge mbalame zinayi; uzisonkhanitse kwa iwe (mpaka uyizindikire mbalame iliyonse mmene ilili, ndipo kenako uziduledule zonsezo zidutswazidutswa ndikuzisakaniza ndi kuzigawa mzigawo zinayi). Ndipo paphiri lililonse ukaikepo gawo limodzi la zimenezo, ndipo kenako uziitane. Zikudzera zikuthamanga. Ndipo dziwa kuti Allah ndi Mwini mphamvu zoposa, Ngwanzem zakuya.”[52]
[52] Mneneri Ibrahim adalakalaka kuti aone mmene akufa adzaukira kuti chikhulupiliro chake chiwonjezeke mphamvu. Tero Allah adamulamula kuti azinge mbalame zinayi zosiyanasiyana mitundu. Kenako azisakanize ziwalo zake. Ziwalo za mbalame ina zilowe kumbalame ina. Tsono azigawe miyulu inayi. Mulu uliwonse akauike pa phiri lakelake. Kenako aziitane mbalame zija. Ndipo aona kuti chiwalo chilichonse chikuthamangira kumbalame yake, pompo zonsezo zikhalanso mbalame zamoyo monga momwe zidalili poyamba.
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 節: (260) 章: 雌牛章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる