Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Versículo: (183) Surah: Suratu Ãli-Imran
ٱلَّذِينَ قَالُوٓاْ إِنَّ ٱللَّهَ عَهِدَ إِلَيۡنَآ أَلَّا نُؤۡمِنَ لِرَسُولٍ حَتَّىٰ يَأۡتِيَنَا بِقُرۡبَانٖ تَأۡكُلُهُ ٱلنَّارُۗ قُلۡ قَدۡ جَآءَكُمۡ رُسُلٞ مِّن قَبۡلِي بِٱلۡبَيِّنَٰتِ وَبِٱلَّذِي قُلۡتُمۡ فَلِمَ قَتَلۡتُمُوهُمۡ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Amene anenanso: “Allah Adatilamula ife kuti tisakhulupirire mtumiki aliyense mpaka atabwera ndi nsembe yopserezedwa ndi moto.” Nena: “Adakudzerani atumiki ndisanadze ndi zisonyezo zooneka ndi chimene mukunenachi. Nanga bwanji mudawapha, ngati mukunenadi zoona?”[103]
[103] Ayuda pamene Mtumiki (s.a.w) amawauza kuti amtsate amanena kuti: “Ife sadatilamule kutsata Mtumiki yemwe akuloleza sadaka. Koma atilamula kutsata atumiki okhawo omwe akulamula kuti sadaka zonse azisonkhanitse pamodzi kenako azitenthe ndi moto. Kapena moto udze kudzapsereza.” Zoonadi, atumiki otero adadza koma sadawatsate monga momwe Allah wanenera apa. Komabe sanawalamule kutsata atumiki otero okhawo. Kutero nkungofuna kupeza chonamizira basi.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Versículo: (183) Surah: Suratu Ãli-Imran
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar