Check out the new design

Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Khalid Ibrahim Batyala * - Índice de tradução


Tradução dos significados Surah: As-Saffat   Versículo:
مَا لَكُمۡ كَيۡفَ تَحۡكُمُونَ
Kodi nchiyani chakupezani (kuti muweruze mopanda chilungamo); nanga mukuweruza bwanji (zimenezi)?
Os Tafssir em língua árabe:
أَفَلَا تَذَكَّرُونَ
Kodi bwanji simukumbukira, (mwaiwala zisonyezo Zake zodabwitsa ndi kupatukana kwake ndi zimenezo)?
Os Tafssir em língua árabe:
أَمۡ لَكُمۡ سُلۡطَٰنٞ مُّبِينٞ
Kapena inu muli ndi umboni woonekera (wochokera kumwamba)?
Os Tafssir em língua árabe:
فَأۡتُواْ بِكِتَٰبِكُمۡ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Tabweretsani buku lanulo (momwe mwalembedwa zimenezi) ngati mukunena zoona.
Os Tafssir em língua árabe:
وَجَعَلُواْ بَيۡنَهُۥ وَبَيۡنَ ٱلۡجِنَّةِ نَسَبٗاۚ وَلَقَدۡ عَلِمَتِ ٱلۡجِنَّةُ إِنَّهُمۡ لَمُحۡضَرُونَ
Ndipo adapeka chibale pakati pa Iye (Allah) ndi ziwanda; (pomwe ziwanda nzobisika kwa iwo). Ndithu ziwanda zimadziwa kuti iwo osakhulupirira akaonekera (kwa Allah kuti aweruzidwe)!
Os Tafssir em língua árabe:
سُبۡحَٰنَ ٱللَّهِ عَمَّا يَصِفُونَ
Walemekezeka Allah! Ndi kupatukana ndi zimene akumnamizira!
Os Tafssir em língua árabe:
إِلَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
Koma akapolo a Allah oyeretsedwa (ali kutali ndi zimene akusimba osakhulupirirazi).
Os Tafssir em língua árabe:
فَإِنَّكُمۡ وَمَا تَعۡبُدُونَ
Ndithu inu (osakhulupirira) ndi zimene mukuzipembedza (kusiya Allah),
Os Tafssir em língua árabe:
مَآ أَنتُمۡ عَلَيۡهِ بِفَٰتِنِينَ
Ndi zimenezo simungamsokeretse aliyense.
Os Tafssir em língua árabe:
إِلَّا مَنۡ هُوَ صَالِ ٱلۡجَحِيمِ
Kupatula yemwe (Allah adadziwa kuti) ngolowa ku Jahannam.
Os Tafssir em língua árabe:
وَمَا مِنَّآ إِلَّا لَهُۥ مَقَامٞ مَّعۡلُومٞ
Ndipo (angelo adanena): “Aliyense mwa ife ali ndi malo ake odziwika.”
Os Tafssir em língua árabe:
وَإِنَّا لَنَحۡنُ ٱلصَّآفُّونَ
“Ndipo ndithu (ena mwa) ife ngondanda m’mizere (ya mapemphero nthawi zonse).”
Os Tafssir em língua árabe:
وَإِنَّا لَنَحۡنُ ٱلۡمُسَبِّحُونَ
“Ndipo (ena mwa) ife ngolemekeza (Allah nthawi zonse ndi kumtamanda ndi kumpatula ku zinthu zosayenerana ndi ulemelero wake).”
Os Tafssir em língua árabe:
وَإِن كَانُواْ لَيَقُولُونَ
Ndipo (osakhulupirira) ankati:
Os Tafssir em língua árabe:
لَوۡ أَنَّ عِندَنَا ذِكۡرٗا مِّنَ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Tikadakhala ndi buku monga lomwe anthu akale adali nalo.”
Os Tafssir em língua árabe:
لَكُنَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
“Tikadakhala akapolo a Allah, oyeretsedwa.”
Os Tafssir em língua árabe:
فَكَفَرُواْ بِهِۦۖ فَسَوۡفَ يَعۡلَمُونَ
Koma (pamene lidawadzera bukulo), adalikana; choncho posachedwa adziwa (zotsatira zake).
Os Tafssir em língua árabe:
وَلَقَدۡ سَبَقَتۡ كَلِمَتُنَا لِعِبَادِنَا ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndipo ndithu liwu lathu lidatsogola kwa akapolo athu otumidwa.
Os Tafssir em língua árabe:
إِنَّهُمۡ لَهُمُ ٱلۡمَنصُورُونَ
(Kuti) ndithu iwo ngopulumutsidwa.
Os Tafssir em língua árabe:
وَإِنَّ جُندَنَا لَهُمُ ٱلۡغَٰلِبُونَ
Ndipo ndithu asilikali Athu ndi opambana.
Os Tafssir em língua árabe:
فَتَوَلَّ عَنۡهُمۡ حَتَّىٰ حِينٖ
Choncho, asiye kwa kanthawi kochepa.
Os Tafssir em língua árabe:
وَأَبۡصِرۡهُمۡ فَسَوۡفَ يُبۡصِرُونَ
Ndipo ingowayang’ana basi; posachedwapa aona!
Os Tafssir em língua árabe:
أَفَبِعَذَابِنَا يَسۡتَعۡجِلُونَ
Kodi chilango chathu akuchifulumizitsa?
Os Tafssir em língua árabe:
فَإِذَا نَزَلَ بِسَاحَتِهِمۡ فَسَآءَ صَبَاحُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Choncho chikadzatsika pabwalo lawo, udzakhala mmawa woipa kwa ochenjezedwa!
Os Tafssir em língua árabe:
وَتَوَلَّ عَنۡهُمۡ حَتَّىٰ حِينٖ
Ndipo asiye kwa kanthawi kochepa.
Os Tafssir em língua árabe:
وَأَبۡصِرۡ فَسَوۡفَ يُبۡصِرُونَ
Ndipo ingowayang’ana basi; posachedwapa aona.
Os Tafssir em língua árabe:
سُبۡحَٰنَ رَبِّكَ رَبِّ ٱلۡعِزَّةِ عَمَّا يَصِفُونَ
Mbuye wako, Mwini ulemelero, wapatukana ndi zimene akumnamizira (osakhulupirira).
Os Tafssir em língua árabe:
وَسَلَٰمٌ عَلَى ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndipo mtendere ukhale pa atumiki onse.
Os Tafssir em língua árabe:
وَٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo kuyamikidwa konse nkwa Allah, Mbuye wa zolengedwa zonse.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Surah: As-Saffat
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Khalid Ibrahim Batyala - Índice de tradução

Tradução por Khaled Ibrahim Bitala.

Fechar