Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 隋法提   段:
مَا لَكُمۡ كَيۡفَ تَحۡكُمُونَ
Kodi nchiyani chakupezani (kuti muweruze mopanda chilungamo); nanga mukuweruza bwanji (zimenezi)?
阿拉伯语经注:
أَفَلَا تَذَكَّرُونَ
Kodi bwanji simukumbukira, (mwaiwala zisonyezo Zake zodabwitsa ndi kupatukana kwake ndi zimenezo)?
阿拉伯语经注:
أَمۡ لَكُمۡ سُلۡطَٰنٞ مُّبِينٞ
Kapena inu muli ndi umboni woonekera (wochokera kumwamba)?
阿拉伯语经注:
فَأۡتُواْ بِكِتَٰبِكُمۡ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Tabweretsani buku lanulo (momwe mwalembedwa zimenezi) ngati mukunena zoona.
阿拉伯语经注:
وَجَعَلُواْ بَيۡنَهُۥ وَبَيۡنَ ٱلۡجِنَّةِ نَسَبٗاۚ وَلَقَدۡ عَلِمَتِ ٱلۡجِنَّةُ إِنَّهُمۡ لَمُحۡضَرُونَ
Ndipo adapeka chibale pakati pa Iye (Allah) ndi ziwanda; (pomwe ziwanda nzobisika kwa iwo). Ndithu ziwanda zimadziwa kuti iwo osakhulupirira akaonekera (kwa Allah kuti aweruzidwe)!
阿拉伯语经注:
سُبۡحَٰنَ ٱللَّهِ عَمَّا يَصِفُونَ
Walemekezeka Allah! Ndi kupatukana ndi zimene akumnamizira!
阿拉伯语经注:
إِلَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
Koma akapolo a Allah oyeretsedwa (ali kutali ndi zimene akusimba osakhulupirirazi).
阿拉伯语经注:
فَإِنَّكُمۡ وَمَا تَعۡبُدُونَ
Ndithu inu (osakhulupirira) ndi zimene mukuzipembedza (kusiya Allah),
阿拉伯语经注:
مَآ أَنتُمۡ عَلَيۡهِ بِفَٰتِنِينَ
Ndi zimenezo simungamsokeretse aliyense.
阿拉伯语经注:
إِلَّا مَنۡ هُوَ صَالِ ٱلۡجَحِيمِ
Kupatula yemwe (Allah adadziwa kuti) ngolowa ku Jahannam.
阿拉伯语经注:
وَمَا مِنَّآ إِلَّا لَهُۥ مَقَامٞ مَّعۡلُومٞ
Ndipo (angelo adanena): “Aliyense mwa ife ali ndi malo ake odziwika.”
阿拉伯语经注:
وَإِنَّا لَنَحۡنُ ٱلصَّآفُّونَ
“Ndipo ndithu (ena mwa) ife ngondanda m’mizere (ya mapemphero nthawi zonse).”
阿拉伯语经注:
وَإِنَّا لَنَحۡنُ ٱلۡمُسَبِّحُونَ
“Ndipo (ena mwa) ife ngolemekeza (Allah nthawi zonse ndi kumtamanda ndi kumpatula ku zinthu zosayenerana ndi ulemelero wake).”
阿拉伯语经注:
وَإِن كَانُواْ لَيَقُولُونَ
Ndipo (osakhulupirira) ankati:
阿拉伯语经注:
لَوۡ أَنَّ عِندَنَا ذِكۡرٗا مِّنَ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Tikadakhala ndi buku monga lomwe anthu akale adali nalo.”
阿拉伯语经注:
لَكُنَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
“Tikadakhala akapolo a Allah, oyeretsedwa.”
阿拉伯语经注:
فَكَفَرُواْ بِهِۦۖ فَسَوۡفَ يَعۡلَمُونَ
Koma (pamene lidawadzera bukulo), adalikana; choncho posachedwa adziwa (zotsatira zake).
阿拉伯语经注:
وَلَقَدۡ سَبَقَتۡ كَلِمَتُنَا لِعِبَادِنَا ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndipo ndithu liwu lathu lidatsogola kwa akapolo athu otumidwa.
阿拉伯语经注:
إِنَّهُمۡ لَهُمُ ٱلۡمَنصُورُونَ
(Kuti) ndithu iwo ngopulumutsidwa.
阿拉伯语经注:
وَإِنَّ جُندَنَا لَهُمُ ٱلۡغَٰلِبُونَ
Ndipo ndithu asilikali Athu ndi opambana.
阿拉伯语经注:
فَتَوَلَّ عَنۡهُمۡ حَتَّىٰ حِينٖ
Choncho, asiye kwa kanthawi kochepa.
阿拉伯语经注:
وَأَبۡصِرۡهُمۡ فَسَوۡفَ يُبۡصِرُونَ
Ndipo ingowayang’ana basi; posachedwapa aona!
阿拉伯语经注:
أَفَبِعَذَابِنَا يَسۡتَعۡجِلُونَ
Kodi chilango chathu akuchifulumizitsa?
阿拉伯语经注:
فَإِذَا نَزَلَ بِسَاحَتِهِمۡ فَسَآءَ صَبَاحُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Choncho chikadzatsika pabwalo lawo, udzakhala mmawa woipa kwa ochenjezedwa!
阿拉伯语经注:
وَتَوَلَّ عَنۡهُمۡ حَتَّىٰ حِينٖ
Ndipo asiye kwa kanthawi kochepa.
阿拉伯语经注:
وَأَبۡصِرۡ فَسَوۡفَ يُبۡصِرُونَ
Ndipo ingowayang’ana basi; posachedwapa aona.
阿拉伯语经注:
سُبۡحَٰنَ رَبِّكَ رَبِّ ٱلۡعِزَّةِ عَمَّا يَصِفُونَ
Mbuye wako, Mwini ulemelero, wapatukana ndi zimene akumnamizira (osakhulupirira).
阿拉伯语经注:
وَسَلَٰمٌ عَلَى ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndipo mtendere ukhale pa atumiki onse.
阿拉伯语经注:
وَٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo kuyamikidwa konse nkwa Allah, Mbuye wa zolengedwa zonse.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 隋法提
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭