Check out the new design

Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Khalid Ibrahim Batyala * - Índice de tradução


Tradução dos significados Surah: Al-Maidah   Versículo:
۞ يَوۡمَ يَجۡمَعُ ٱللَّهُ ٱلرُّسُلَ فَيَقُولُ مَاذَآ أُجِبۡتُمۡۖ قَالُواْ لَا عِلۡمَ لَنَآۖ إِنَّكَ أَنتَ عَلَّٰمُ ٱلۡغُيُوبِ
(Kumbukirani) tsiku lomwe Allah adzasonkhanitsa, atumiki ndikuwafunsa kuti: “Kodi mudayankhidwa chiyani?” Iwo adzati: “Ife sitidziwa. Ndithudi, Inuyo ndiye Wodziwa zamseri.”
Os Tafssir em língua árabe:
إِذۡ قَالَ ٱللَّهُ يَٰعِيسَى ٱبۡنَ مَرۡيَمَ ٱذۡكُرۡ نِعۡمَتِي عَلَيۡكَ وَعَلَىٰ وَٰلِدَتِكَ إِذۡ أَيَّدتُّكَ بِرُوحِ ٱلۡقُدُسِ تُكَلِّمُ ٱلنَّاسَ فِي ٱلۡمَهۡدِ وَكَهۡلٗاۖ وَإِذۡ عَلَّمۡتُكَ ٱلۡكِتَٰبَ وَٱلۡحِكۡمَةَ وَٱلتَّوۡرَىٰةَ وَٱلۡإِنجِيلَۖ وَإِذۡ تَخۡلُقُ مِنَ ٱلطِّينِ كَهَيۡـَٔةِ ٱلطَّيۡرِ بِإِذۡنِي فَتَنفُخُ فِيهَا فَتَكُونُ طَيۡرَۢا بِإِذۡنِيۖ وَتُبۡرِئُ ٱلۡأَكۡمَهَ وَٱلۡأَبۡرَصَ بِإِذۡنِيۖ وَإِذۡ تُخۡرِجُ ٱلۡمَوۡتَىٰ بِإِذۡنِيۖ وَإِذۡ كَفَفۡتُ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ عَنكَ إِذۡ جِئۡتَهُم بِٱلۡبَيِّنَٰتِ فَقَالَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ مِنۡهُمۡ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ مُّبِينٞ
Kumbukiraninso pamene Allah adzati: “Iwe Isa (Yesu) mwana wa Mariya! Kumbuka chisomo Changa pa iwe ndi pa mayi wako, pamene ndinakuthandiza ndi mzimu woyera (Gabriel), (kotero kuti) udalankhula kwa anthu (mawu omveka) pamene udali mchikuta ndiponso pamene udali wamkulu. Ndipo (kumbuka) pamene ndidakuphunzitsa kulemba, nzeru; (ndinakuzindikiritsanso buku la) Taurat ndi Injili. (Kumbukanso) pamene udaumba dongo chithunzi chambalame mwa lamulo Langa. Utatero udauziramo ndipo zidasanduka mbalame mwa lamulo Langa. Ndipamene udali kuchiza akhungu ndi achinawa, mwa lamulo Langa. Ndipamene unkawatulutsa (m’manda) ena mwa akufa mwa lamulo Langa. Ndipamene ndinawatsekereza ana a Israyeli kwa iwe (kuti asakuzunze) pamene udawadzera ndi zisonyezo zooneka, ndipo aja mwa iwo omwe sadakhulupirire, adati: “Ichi sichina, koma ndi matsenga owonekera.”
Os Tafssir em língua árabe:
وَإِذۡ أَوۡحَيۡتُ إِلَى ٱلۡحَوَارِيِّـۧنَ أَنۡ ءَامِنُواْ بِي وَبِرَسُولِي قَالُوٓاْ ءَامَنَّا وَٱشۡهَدۡ بِأَنَّنَا مُسۡلِمُونَ
Ndipo (kumbukira) pamene ndidawaululira ophunzira ako kuti: “Ndikhulupirireni Ine ndi Mtumiki Wanga (uyu Isa {Yesu}).” Iwo adati: “Takhulupirira; ndipo khalani mboni kuti ife ndife Asilamu (ogonjera mwa Inu).”
Os Tafssir em língua árabe:
إِذۡ قَالَ ٱلۡحَوَارِيُّونَ يَٰعِيسَى ٱبۡنَ مَرۡيَمَ هَلۡ يَسۡتَطِيعُ رَبُّكَ أَن يُنَزِّلَ عَلَيۡنَا مَآئِدَةٗ مِّنَ ٱلسَّمَآءِۖ قَالَ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَ إِن كُنتُم مُّؤۡمِنِينَ
(Kumbukira) pamene ophunzira ako adati: “E iwe Isa (Yesu) mwana wa Mariya: Kodi Mbuye wako angathe kutitsitsira chakudya kuchokera kumwamba?” (Isa {Yesu}) adati: “Opani Allah, ngati inu mulidi okhulupirira. (Musamangopempha zozizwitsa).”
Os Tafssir em língua árabe:
قَالُواْ نُرِيدُ أَن نَّأۡكُلَ مِنۡهَا وَتَطۡمَئِنَّ قُلُوبُنَا وَنَعۡلَمَ أَن قَدۡ صَدَقۡتَنَا وَنَكُونَ عَلَيۡهَا مِنَ ٱلشَّٰهِدِينَ
(Iwo) adati: “Tikufuna kudya chimenecho, ndikuti mitima yathu ikhazikike, ndikutinso tidziwe kuti watiuza choona; tero kuti tikhale oikira umboni pa chimenecho.”
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Surah: Al-Maidah
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Khalid Ibrahim Batyala - Índice de tradução

Tradução por Khaled Ibrahim Bitala.

Fechar