Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Ala   Versículo:

Suratu Al-Ala

سَبِّحِ ٱسۡمَ رَبِّكَ ٱلۡأَعۡلَى
Lemekeza dzina la Mbuye wako Wapamwambamwamba (ndikuliyeretsa ku zinthu zosayenera).[417]
[417] Tanthauzo lakulemekeza dzina la Allah ndiko kukhulupilira kuti iye ndiwopatulika ku mbiri zilizonse zoipa zosamuyenera, monga kumufanizira ndizolengedwa; monga kuti anabereka kapena adaberekedwa, kapena kuti ali ndi mkazi kapenanso kuti alipo omwe amathandizana naye pa Umulungu Wake.
Os Tafssir em língua árabe:
ٱلَّذِي خَلَقَ فَسَوَّىٰ
Amene adalenga (chilichonse) ndikuchikonza bwinobwino (mkalengedwe kolingana).
Os Tafssir em língua árabe:
وَٱلَّذِي قَدَّرَ فَهَدَىٰ
Amene adalamuliratu (chilichonse zochita zake) ndi kuchiongolera.[418]
[418] Allah pambuyo polenga zolengedwa Zake sadangozileka kuti zisadziwe chochita, koma cholengedwa chilichonse adachilamuliratu kuti chichite zoyenera nacho, ndipo pambuyo pake adachiongolera pa chinthu chimenecho; chidadziwa, ndipo chidachita. Munthu adamusonyeza zomwe zili ndi mazunzo mkati mwake kuti adzitalikitse nazo ndiponso adamusonyeza zabwino kuti azichite.
Os Tafssir em língua árabe:
وَٱلَّذِيٓ أَخۡرَجَ ٱلۡمَرۡعَىٰ
Ndi Yemwenso akumeretsa msipu.
Os Tafssir em língua árabe:
فَجَعَلَهُۥ غُثَآءً أَحۡوَىٰ
Ndipo nausandutsa kukhala wouma ndi wodera.
Os Tafssir em língua árabe:
سَنُقۡرِئُكَ فَلَا تَنسَىٰٓ
Tikulakatulira (chivumbulutso Chathu) ndipo siuyiwala.[419]
[419] Mneneri Muhammad (s.a.w) adali munthu monga anthu ena ndipo adali ndi mbiri zonga anthu adalinazo, monga: kukonda ndi kusakonda, kuiwala ndi kukumbukira. Padapezeka kuti nthawi ina adaiwala ndi kupemphera maraka atatu m’Swala ya maraka anayi. Pachifukwa ichi pa nthawi yovumbulutsidwa Qur’an ndi Jibril, adali akubwereza bwereza mawu ovumbulutsidwawo kuopa kuti angaiwale. Choncho, apa Allah akumuletsa kuti asadzivutitse kumabwerezabwereza mawuwo pamene akuvumbulutsidwa ndipo adamupatsa lonjezo nthawi yomweyo kuti sadzaiwala. Ndipo adakwaniritsa lonjezo Lake. Mtumiki (s.a.w) adali kumtsikira ma surah aataliatali ndipo amatha kuwawerenga (molakatula) popanda kuonjezera kanthu kapena kuchepetsa, ngakhale kuti iye sadali kudziwa kuwerenga ndi kulemba. Kuwerenga kwake kudali kwakungolakatula pa mtima.
Os Tafssir em língua árabe:
إِلَّا مَا شَآءَ ٱللَّهُۚ إِنَّهُۥ يَعۡلَمُ ٱلۡجَهۡرَ وَمَا يَخۡفَىٰ
Kupatula chimene wafuna Allah (kuti uchiiwale); ndithu Iye amadziwa zoonekera ndi zimene zimabisika.
Os Tafssir em língua árabe:
وَنُيَسِّرُكَ لِلۡيُسۡرَىٰ
Ndipo tikufewetsera (njira yochitira zinthu) zabwino.[420]
[420] Tanthauzo la ‘kufewetsa’ ndiko kuti Shariya ya Chisilamu (malamulo) siili yovuta kuyikwaniritsa monga momwe adalili malamulo a zipembedzo zoyamba. Ndipo ndi malamulo othandiza anthu onse, nthawi zonse ndi pamalo paliponse.
Os Tafssir em língua árabe:
فَذَكِّرۡ إِن نَّفَعَتِ ٱلذِّكۡرَىٰ
Choncho akumbutse (wanthu powalalikira) ngati kukumbutsa kuthandiza.[421]
[421] Tanthauzo la apa sikuti Mtumiki (s.a.w) alalikire pokhapokha waona kuti ulalikiwo uthandiza ayi, koma alalikire ndithu kaya kulalikirako kuthandiza kapena ayi, monga momwe zalongosolera Ayah zotsatirazi. Kuyankhula kotere, Arabu amakutcha “iktifa.”
Os Tafssir em língua árabe:
سَيَذَّكَّرُ مَن يَخۡشَىٰ
(Palibe chikaiko ulalikiwo) aukumbukira (ndikuthandizidwa nawo) amene akuopa Allah.
Os Tafssir em língua árabe:
وَيَتَجَنَّبُهَا ٱلۡأَشۡقَى
Ndipo wamavuto ambiri, (wamakani ndi wokanira), adzitalikitsa ndi ulalikiwo.[422]
[422] “Wamavuto ambiri” apa, ndiko kuzunzika ndi matsoka. Allah akumutcha kafiri kuti “Wamavuto ambiri” chifukwa chakuti ali ndi mavuto padziko lino lapansi mpaka pa tsiku lachimaliziro. Mazunzo a tsiku lachimaliziro monga momwe tidziwira ndi chilango cha Moto chomwe chikumuyembekeza. Tsono “chilango cha padziko lapansi” ndiko kuti alibe chinthu chomutonthoza likampeza tsoka kapena vuto lililonse. Msilamu likampeza vuto amadzitonthoza ndi chikhulupiliro chake chakuti moyo wa munthu suwonjezeka ndiponso suchepa, ndikuti munthu amamwalira akamaliza moyo wake. Koma kafiri saganiza choncho; amangokukuta zala ndi kuwatukwana ma dokotala kuti sadziwa kanthu akadachita mwakutimwakuti munthuyo sakadafa. Msilamu kukampeza kusauka amadzitonthoza ndi kupilira pamodzi ndi chikhulupiliro choti “chilichonse chimachitika mchifuniro cha Allah.” Ndipo amakhala woyembekezera kuti lero kapena mawa, Allah amupatsa chisomo Chake. Koma anthu opanda chikhulupiliro amangoona kuti aponderezedwa; amayesetsa kufunafuna chuma mnjira zosayenera, ndipo akalephera amadzudzula uyu kapena kumenyana ndi uyu, ndipo amangodziona ngati wonyozeka kwambiri pa maso pa munthu wolemera.
Kotero kuti atauzidwa kuti amulambire wolemera uja kuti amupatse ndalama akhoza kuchita zotero. Ndipo tsiku lililonse njiru imamuondetsa; mwina amangodzipha monga momwe tionera masiku ano. Palibe mazunzo aakulu kuposa amenewa. Ngati muyang’ana ma Ayah 16 ndi 17 muona kuti akuthilira umboni pa zimene talongosolazi.
Os Tafssir em língua árabe:
ٱلَّذِي يَصۡلَى ٱلنَّارَ ٱلۡكُبۡرَىٰ
Amene adzalowa ku moto waukulu (umene wakonzedwa kuti udzakhale malipiro ake).
Os Tafssir em língua árabe:
ثُمَّ لَا يَمُوتُ فِيهَا وَلَا يَحۡيَىٰ
Ndipo sakafa m’menemo (ndikupumula kumazunzo), ndiponso sakakhala ndi moyo (wamtendere).
Os Tafssir em língua árabe:
قَدۡ أَفۡلَحَ مَن تَزَكَّىٰ
Ndithu wapambana amene wadziyeretsa (ku machimo),[423]
[423] Tanthauzo lake ndikuti amene wadziyeretsa posiya kumuphatikiza Allah ndi zolengedwa ndi kumchimwira ndi machimo onse. Machimo amaletsa ulaliki wabwino kulowa mu mtima wa munthu. (yang’anani ndemanga ya 14 mu surat ya Al-Mutaffifin).
Os Tafssir em língua árabe:
وَذَكَرَ ٱسۡمَ رَبِّهِۦ فَصَلَّىٰ
Ndikukumbukira dzina la Mbuye wake (ndi mtima wake, ndi lirime lake) uku akumapemphera.
Os Tafssir em língua árabe:
بَلۡ تُؤۡثِرُونَ ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا
Koma inu mukukonda kwambiri moyo wa dziko lapansi.
Os Tafssir em língua árabe:
وَٱلۡأٓخِرَةُ خَيۡرٞ وَأَبۡقَىٰٓ
Pamene moyo wa tsiku lachimaliziro ndiwabwino kwambiri ndiponso wamuyaya.
Os Tafssir em língua árabe:
إِنَّ هَٰذَا لَفِي ٱلصُّحُفِ ٱلۡأُولَىٰ
Ndithu izi (mukuuzidwa m’Qur’an) zilipo m’mabuku oyamba, akale,[424]
[424] Mawu akuti “wapambana amene wadziyeretsa ndi kumkumbukira Mbuye wake ndi kumapemphera,” ndiponso kuti: “ tsiku lachimaliziro ndilabwino kuposa dziko lapansi” mawuwa adanenedwanso m’mabuku oyamba; sikuti Qur’an ndiyo yayamba kunena zimenezi.
Os Tafssir em língua árabe:
صُحُفِ إِبۡرَٰهِيمَ وَمُوسَىٰ
Mabuku a Ibrahim ndi Mûsa.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Ala
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar