Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Ajeti: (49) Surja: Suretu En Nisa
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ يُزَكُّونَ أَنفُسَهُمۚ بَلِ ٱللَّهُ يُزَكِّي مَن يَشَآءُ وَلَا يُظۡلَمُونَ فَتِيلًا
Kodi sukuwaona omwe akudziyeretsa okha? Koma Allah amamuyeretsa amene wamufuna (pomulimbikitsa kuchita zabwino). Ndipo sadzaponderezedwa ngakhale ndi kachinthu kochepa konga kaulusi kokhala mkati mwakhokho la tende.[126]
[126] Ayuda adali kunyada chifukwa choti iwo adali nawo aneneri, ndiponso makolo awo omwe adali olungama. Ankati: “Poti makolo athu adali olungama palibe chochititsa mantha pa ife. Uchimo uliwonse umene ife tingachite Allah adzatikhululukira ngakhale uchimowo utakhala waukulu chotani.” Iwo ankadzitchanso kuti adali okondedwa a Allah. Ndipo iwowo ngomwe akuwatchula m’ndime iyi kuti “Kodi saona amene akudziyeretsa okha ndi mawu okha ochokera m’milomo popanda kuchita zimene adawalamula ndi kusiya zomwe adawaletsa?” Mwa Asilamu aliponso ena omwe ali ndi maganizo onga amenewa. Amangonyadira zochita zamakolo awo popanda kutsanzira chikhalidwe chamakolo awowo.
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Ajeti: (49) Surja: Suretu En Nisa
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll