Check out the new design

Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Bản dịch Shishiwā - Khālid Ibrāhīm Batiyālā * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Câu: (49) Chương: Al-Nisa'
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ يُزَكُّونَ أَنفُسَهُمۚ بَلِ ٱللَّهُ يُزَكِّي مَن يَشَآءُ وَلَا يُظۡلَمُونَ فَتِيلًا
Kodi sukuwaona omwe akudziyeretsa okha? Koma Allah amamuyeretsa amene wamufuna (pomulimbikitsa kuchita zabwino). Ndipo sadzaponderezedwa ngakhale ndi kachinthu kochepa konga kaulusi kokhala mkati mwakhokho la tende.[126]
[126] Ayuda adali kunyada chifukwa choti iwo adali nawo aneneri, ndiponso makolo awo omwe adali olungama. Ankati: “Poti makolo athu adali olungama palibe chochititsa mantha pa ife. Uchimo uliwonse umene ife tingachite Allah adzatikhululukira ngakhale uchimowo utakhala waukulu chotani.” Iwo ankadzitchanso kuti adali okondedwa a Allah. Ndipo iwowo ngomwe akuwatchula m’ndime iyi kuti “Kodi saona amene akudziyeretsa okha ndi mawu okha ochokera m’milomo popanda kuchita zimene adawalamula ndi kusiya zomwe adawaletsa?” Mwa Asilamu aliponso ena omwe ali ndi maganizo onga amenewa. Amangonyadira zochita zamakolo awo popanda kutsanzira chikhalidwe chamakolo awowo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Câu: (49) Chương: Al-Nisa'
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Bản dịch Shishiwā - Khālid Ibrāhīm Batiyālā - Mục lục các bản dịch

Người dịch Khalid Ibrahim Bitala.

Đóng lại