Check out the new design

Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - Përkthimi çiçevë - Khalid Ibrahim Betiala * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Surja: El Enam   Ajeti:
۞ إِنَّمَا يَسۡتَجِيبُ ٱلَّذِينَ يَسۡمَعُونَۘ وَٱلۡمَوۡتَىٰ يَبۡعَثُهُمُ ٱللَّهُ ثُمَّ إِلَيۡهِ يُرۡجَعُونَ
Ndithudi amene akuvomereza, ngomwe akumva (ndipo anthu awa amene safuna kumvera chilichonse ndi akufa ngakhale ali moyo). Ndipo akufa Allah adzawaukitsa (m’manda mwawo) kenako adzabwezedwa kwa Iye.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَقَالُواْ لَوۡلَا نُزِّلَ عَلَيۡهِ ءَايَةٞ مِّن رَّبِّهِۦۚ قُلۡ إِنَّ ٱللَّهَ قَادِرٌ عَلَىٰٓ أَن يُنَزِّلَ ءَايَةٗ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَهُمۡ لَا يَعۡلَمُونَ
Ndipo akumanena: “Bwanji sichinatsitsidwe chozizwitsa kwa iye kuchokera kwa Mbuye wake?” Nena: “Ndithudi, Allah Ngokhoza kutsitsa chozizwitsa koma ambiri a iwo sadziwa (zomwe Allah afuna).”
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَا مِن دَآبَّةٖ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَا طَٰٓئِرٖ يَطِيرُ بِجَنَاحَيۡهِ إِلَّآ أُمَمٌ أَمۡثَالُكُمۚ مَّا فَرَّطۡنَا فِي ٱلۡكِتَٰبِ مِن شَيۡءٖۚ ثُمَّ إِلَىٰ رَبِّهِمۡ يُحۡشَرُونَ
Ndipo palibe nyama ili yonse pa nthaka, ngakhale mbalame yowuluka ndi mapiko ake awiri koma ndi magulu a zolengedwa ngati inu (zomwe Allah adazilenga). Sitinasiye chinthu chilichonse kapena kuchinyozera chilichonse m’buku (chomwe nchofunika koma tachifotokoza). Ndipo tero kwa Mbuye wawo adzasonkhanitsidwa.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا صُمّٞ وَبُكۡمٞ فِي ٱلظُّلُمَٰتِۗ مَن يَشَإِ ٱللَّهُ يُضۡلِلۡهُ وَمَن يَشَأۡ يَجۡعَلۡهُ عَلَىٰ صِرَٰطٖ مُّسۡتَقِيمٖ
Ndipo amene atsutsa zizindikiro Zathu, ndiagonthi ndiponso abubu, ali mu m’dima (wa umbuli). Amene Allah wamfuna amamlekelera kusokera. Ndipo amene wamfuna amamuika pa njira yolunjika (yomwe ndi njira ya Chisilamu).
Tefsiret në gjuhën arabe:
قُلۡ أَرَءَيۡتَكُمۡ إِنۡ أَتَىٰكُمۡ عَذَابُ ٱللَّهِ أَوۡ أَتَتۡكُمُ ٱلسَّاعَةُ أَغَيۡرَ ٱللَّهِ تَدۡعُونَ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Nena: “Tandiuzani ngati mazunzo a Allah atakufikani (pompano pa dziko lapansi), kapena kukufikani nthawi (ya chilango cha tsiku lachimaliziro) kodi mudzaitana yemwe sali Allah (kuti akupulumutseni) ngati inu muli owona.”
Tefsiret në gjuhën arabe:
بَلۡ إِيَّاهُ تَدۡعُونَ فَيَكۡشِفُ مَا تَدۡعُونَ إِلَيۡهِ إِن شَآءَ وَتَنسَوۡنَ مَا تُشۡرِكُونَ
“Koma Iye yekha ndi Yemwe mudzampempha, ndipo Iye adzakuchotserani zomwe mukumpempha (kuti akuchotsereni) ngati atafuna. Ndipo mudzaiwala zomwe mudali kuziphatikiza (ndi Allah).”
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَلَقَدۡ أَرۡسَلۡنَآ إِلَىٰٓ أُمَمٖ مِّن قَبۡلِكَ فَأَخَذۡنَٰهُم بِٱلۡبَأۡسَآءِ وَٱلضَّرَّآءِ لَعَلَّهُمۡ يَتَضَرَّعُونَ
Ndithu tidawatumiza (atumiki) ku mibadwo yomwe idalipo iwe usadadze. Ndipo tidaikhaulitsa (mibadwoyo) ndi mazunzo ndi masautso kuti iyo idzichepetse (pambuyo podzikuza).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَلَوۡلَآ إِذۡ جَآءَهُم بَأۡسُنَا تَضَرَّعُواْ وَلَٰكِن قَسَتۡ قُلُوبُهُمۡ وَزَيَّنَ لَهُمُ ٱلشَّيۡطَٰنُ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Pamene masautso adawafika kuchokera kwa Ife, bwanji sadaphunzire kudzichepetsa? Koma mitima yawo idali youma, ndipo satana adawakometsera machimo omwe iwo adali kuchita.
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَلَمَّا نَسُواْ مَا ذُكِّرُواْ بِهِۦ فَتَحۡنَا عَلَيۡهِمۡ أَبۡوَٰبَ كُلِّ شَيۡءٍ حَتَّىٰٓ إِذَا فَرِحُواْ بِمَآ أُوتُوٓاْ أَخَذۡنَٰهُم بَغۡتَةٗ فَإِذَا هُم مُّبۡلِسُونَ
Ndipo pamene adanyozera zimene ankakumbutsidwa tidawatsekulira makomo a chinthu chilichonse (chimene adali kuchifuna) kufikira pamene adasangalala ndi zomwe adapatsidwa, tidawagwira mwadzidzidzi; pompo adataya mtima.
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Surja: El Enam
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - Përkthimi çiçevë - Khalid Ibrahim Betiala - Përmbajtja e përkthimeve

E përktheu Khalid Ibrahim Betala.

Mbyll