Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu El Mutaffifin   Ajeti:

Suretu El Mutaffifin

وَيۡلٞ لِّلۡمُطَفِّفِينَ
Kuonongeka koopsa kukawapeza opunguza miyeso ya malonda.
Tefsiret në gjuhën arabe:
ٱلَّذِينَ إِذَا ٱكۡتَالُواْ عَلَى ٱلنَّاسِ يَسۡتَوۡفُونَ
Amene amati akamadziyezera zinthu kwa anthu amafuna kulandira miyeso yodzadza.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَإِذَا كَالُوهُمۡ أَو وَّزَنُوهُمۡ يُخۡسِرُونَ
Koma pamene iwo akamawayesera pa muyeso wa mbale kapena wa sikelo amapungula (choyenera kulandira ogulawo).
Tefsiret në gjuhën arabe:
أَلَا يَظُنُّ أُوْلَٰٓئِكَ أَنَّهُم مَّبۡعُوثُونَ
Kodi amenewa (akupungula miyeso pamalondawo) sakuganiza kuti adzaukitsidwa;
Tefsiret në gjuhën arabe:
لِيَوۡمٍ عَظِيمٖ
Pa tsiku lalikulu (ndiponso loopsa)?
Tefsiret në gjuhën arabe:
يَوۡمَ يَقُومُ ٱلنَّاسُ لِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Tsiku limene adzaimilira anthu pamaso pa Mbuye wa zolengedwa.
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّآ إِنَّ كِتَٰبَ ٱلۡفُجَّارِ لَفِي سِجِّينٖ
Ayi! Ndithu (siyani chinyengo pamalonda ndi kusalabadira kuuka mmanda); zolembedwa za ntchito ya oipa zili mu Sijjin.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سِجِّينٞ
Nanga nchiyani chitakudziwitse za Sijjin?
Tefsiret në gjuhën arabe:
كِتَٰبٞ مَّرۡقُومٞ
Ameneyu ndi kaundula wamkulu yemwe walembedwa (mkati mwake ntchito za anthu oipa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Chilango chaukali tsiku limenelo chili pa otsutsa,[401]
[401] Kutsutsa kulipo kwa mitundu itatu:
(a) Kutsutsa kwa mawu ndi zochita;
(b) Kutsutsa kwa zochita zokha, monga ukauzidwa kuti chinthu ichi nchoipa, munthu nkudziwa kuti zoona nchoipadi koma nkudzachichita chimenecho mosalabadira;
(c) Kutsutsa ndi zolankhula zokha. Kumeneko ndiko monga munthu akudziwa kuti chakutichakuti ncholetsedwa (haramu) koma m’malo mwake iye nkumati chimenecho nchovomerezeka (halali)
Tefsiret në gjuhën arabe:
ٱلَّذِينَ يُكَذِّبُونَ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Amene akutsutsa za tsiku la malipiro.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَا يُكَذِّبُ بِهِۦٓ إِلَّا كُلُّ مُعۡتَدٍ أَثِيمٍ
Ndipo palibe angalitsutse koma yekhayo wopyola malire (pochita zoipa), wa machimo ambiri;
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِ ءَايَٰتُنَا قَالَ أَسَٰطِيرُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Pamene ma Ayah Athu akuwerengedwa kwa iye (onena za tsiku la malipiro ndikuuka mmanda) amanena kuti: “Izi ndi nthano za anthu akale.”
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّاۖ بَلۡۜ رَانَ عَلَىٰ قُلُوبِهِم مَّا كَانُواْ يَكۡسِبُونَ
Iyayi, sichoncho! Koma yaphimbidwa mitima yawo ndi dzimbiri (la machimo) omwe akhala akukolola.[402]
[402] Munthu akachita choipa koyamba ndipo osalapa, limalowa dontho lakuda mu mtima mwake; nthawi iliyonse pamene akuonjezera machimo, dontho lija limakulirakulira mpaka kuuphimba mtima wonse. Dontho limeneli ndilo likutchedwa “Ran.” Tsono mtima ngati utaphimbidwa chotere sulabadira kuchita zoipa, ngakhale kuti auongole sungaongoke.
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّآ إِنَّهُمۡ عَن رَّبِّهِمۡ يَوۡمَئِذٖ لَّمَحۡجُوبُونَ
Ayi ndithu iwo (okanira) tsiku limenelo) adzatchingidwa kwa Mbuye wawo; (sadzamuona).
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ إِنَّهُمۡ لَصَالُواْ ٱلۡجَحِيمِ
Pambuyo pake adzalowa ku Moto; (oyaka)
Tefsiret në gjuhën arabe:
ثُمَّ يُقَالُ هَٰذَا ٱلَّذِي كُنتُم بِهِۦ تُكَذِّبُونَ
Kenaka adzauzidwa (powaliritsa) “Ichi nchilango chomwe mudali kuchitsutsa (pa dziko lapansi).”
Tefsiret në gjuhën arabe:
كَلَّآ إِنَّ كِتَٰبَ ٱلۡأَبۡرَارِ لَفِي عِلِّيِّينَ
Zoona, ndithu kaundula wa anthu abwino (ochita ntchito zabwino) ali mu Illiyyun.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا عِلِّيُّونَ
Nanga nchiyani chitakudziwitse za Illiyyun?
Tefsiret në gjuhën arabe:
كِتَٰبٞ مَّرۡقُومٞ
Ameneyu ndi kaundula (wamkulu) yemwe walembedwa (mkati mwake ntchito za anthu abwino);
Tefsiret në gjuhën arabe:
يَشۡهَدُهُ ٱلۡمُقَرَّبُونَ
Amamuyikira umboni (angelo) amene ayandikitsidwa (kwa Allah).
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّ ٱلۡأَبۡرَارَ لَفِي نَعِيمٍ
Ndithu ochita zabwino adzakhala mu mtendere,
Tefsiret në gjuhën arabe:
عَلَى ٱلۡأَرَآئِكِ يَنظُرُونَ
Atakhala pa mipando ya ulemu uku akuyang’ana (zimene Allah wawapatsa monga mtendere ndi ulemelero).
Tefsiret në gjuhën arabe:
تَعۡرِفُ فِي وُجُوهِهِمۡ نَضۡرَةَ ٱلنَّعِيمِ
Udzaona kuwala kwa mtendere pa nkhope zawo;
Tefsiret në gjuhën arabe:
يُسۡقَوۡنَ مِن رَّحِيقٖ مَّخۡتُومٍ
Adzamwetsedwa vinyo (woyeretsedwa) wotsekeredwa ndi zitsekerero zolimba;
Tefsiret në gjuhën arabe:
خِتَٰمُهُۥ مِسۡكٞۚ وَفِي ذَٰلِكَ فَلۡيَتَنَافَسِ ٱلۡمُتَنَٰفِسُونَ
Komalizira kwake (kwa vinyoyo) kuzikatuluka fungo la misk; kuti akapeze zimenezi, apikisane opikisana.[403]
[403] Apa, akutilamula kupikisana pakuchita zabwino kuti tipeze madalitso amene awakonzera anthu abwino. Kumeneko ndikuti munthu aliyense alimbikire kuchita mapemphero ndi zina zabwino.
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمِزَاجُهُۥ مِن تَسۡنِيمٍ
Ndipo chosakanizira cha vinyoyo ndi madzi a Tasnim.
Tefsiret në gjuhën arabe:
عَيۡنٗا يَشۡرَبُ بِهَا ٱلۡمُقَرَّبُونَ
(Tasnim ameneyo) ndi kasupe amene azikamwa amene ayandikitsidwa (kwa Allah.)
Tefsiret në gjuhën arabe:
إِنَّ ٱلَّذِينَ أَجۡرَمُواْ كَانُواْ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ يَضۡحَكُونَ
Ndithu amene adachita machimo adali kuwaseka (mwachipongwe) okhulupirira (pa dziko lapansi);
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَإِذَا مَرُّواْ بِهِمۡ يَتَغَامَزُونَ
(Okhulupirira) akadutsa pafupi ndi iwo ankakodolerana maso (mwachipongwe);
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَإِذَا ٱنقَلَبُوٓاْ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِمُ ٱنقَلَبُواْ فَكِهِينَ
Ndipo akabwerera kwa anzawo amabwerera akusangalala (ndi kunyozedwa kwa okhulupirira);
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَإِذَا رَأَوۡهُمۡ قَالُوٓاْ إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ لَضَآلُّونَ
Ndipo (nthawi zonse) akawaona Asilamu amanena: “Ndithu awa ndi osokera (chifukwa chomkhulupirira Mtumiki).” (s.a.w)
Tefsiret në gjuhën arabe:
وَمَآ أُرۡسِلُواْ عَلَيۡهِمۡ حَٰفِظِينَ
Sanatumizidwe (Akafiri) kukhala ayang’aniri kwa okhulupirira (ndikuwaweruza zakulungama ndi kusokera).
Tefsiret në gjuhën arabe:
فَٱلۡيَوۡمَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مِنَ ٱلۡكُفَّارِ يَضۡحَكُونَ
Basi lero okhulupirira awaseka osakhulupirira (powabwezera chipongwe chawo chimene ankachita pa dziko lapansi),[404]
[404] (Ndime 34-36) Tanthauzo lake ndikuti okhulupilira, tsiku lachimaliziro adzakhala m’mipando ya ulemu uku akuwayang’ana ndi kuwaseka anthu osakhulupilira ali m’mavuto monga momwe iwo adali kuseka okhulupilira pa dziko lapansi.
Tefsiret në gjuhën arabe:
عَلَى ٱلۡأَرَآئِكِ يَنظُرُونَ
Atakhala pa mipando ya ulemu uku akuyang’ana (mtendere umene Allah wawapatsa).
Tefsiret në gjuhën arabe:
هَلۡ ثُوِّبَ ٱلۡكُفَّارُ مَا كَانُواْ يَفۡعَلُونَ
Kodi alipidwa osakhulupirira pa zomwe ankachita zija (pa dziko lapansi)?
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Surja: Suretu El Mutaffifin
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll