ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني سورة: المطففين   آية:

المطففين

وَيۡلٞ لِّلۡمُطَفِّفِينَ
Kuonongeka koopsa kukawapeza opunguza miyeso ya malonda.
التفاسير العربية:
ٱلَّذِينَ إِذَا ٱكۡتَالُواْ عَلَى ٱلنَّاسِ يَسۡتَوۡفُونَ
Amene amati akamadziyezera zinthu kwa anthu amafuna kulandira miyeso yodzadza.
التفاسير العربية:
وَإِذَا كَالُوهُمۡ أَو وَّزَنُوهُمۡ يُخۡسِرُونَ
Koma pamene iwo akamawayesera pa muyeso wa mbale kapena wa sikelo amapungula (choyenera kulandira ogulawo).
التفاسير العربية:
أَلَا يَظُنُّ أُوْلَٰٓئِكَ أَنَّهُم مَّبۡعُوثُونَ
Kodi amenewa (akupungula miyeso pamalondawo) sakuganiza kuti adzaukitsidwa;
التفاسير العربية:
لِيَوۡمٍ عَظِيمٖ
Pa tsiku lalikulu (ndiponso loopsa)?
التفاسير العربية:
يَوۡمَ يَقُومُ ٱلنَّاسُ لِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Tsiku limene adzaimilira anthu pamaso pa Mbuye wa zolengedwa.
التفاسير العربية:
كَلَّآ إِنَّ كِتَٰبَ ٱلۡفُجَّارِ لَفِي سِجِّينٖ
Ayi! Ndithu (siyani chinyengo pamalonda ndi kusalabadira kuuka mmanda); zolembedwa za ntchito ya oipa zili mu Sijjin.
التفاسير العربية:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سِجِّينٞ
Nanga nchiyani chitakudziwitse za Sijjin?
التفاسير العربية:
كِتَٰبٞ مَّرۡقُومٞ
Ameneyu ndi kaundula wamkulu yemwe walembedwa (mkati mwake ntchito za anthu oipa).
التفاسير العربية:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Chilango chaukali tsiku limenelo chili pa otsutsa,[401]
[401] Kutsutsa kulipo kwa mitundu itatu:
(a) Kutsutsa kwa mawu ndi zochita;
(b) Kutsutsa kwa zochita zokha, monga ukauzidwa kuti chinthu ichi nchoipa, munthu nkudziwa kuti zoona nchoipadi koma nkudzachichita chimenecho mosalabadira;
(c) Kutsutsa ndi zolankhula zokha. Kumeneko ndiko monga munthu akudziwa kuti chakutichakuti ncholetsedwa (haramu) koma m’malo mwake iye nkumati chimenecho nchovomerezeka (halali)
التفاسير العربية:
ٱلَّذِينَ يُكَذِّبُونَ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Amene akutsutsa za tsiku la malipiro.
التفاسير العربية:
وَمَا يُكَذِّبُ بِهِۦٓ إِلَّا كُلُّ مُعۡتَدٍ أَثِيمٍ
Ndipo palibe angalitsutse koma yekhayo wopyola malire (pochita zoipa), wa machimo ambiri;
التفاسير العربية:
إِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِ ءَايَٰتُنَا قَالَ أَسَٰطِيرُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Pamene ma Ayah Athu akuwerengedwa kwa iye (onena za tsiku la malipiro ndikuuka mmanda) amanena kuti: “Izi ndi nthano za anthu akale.”
التفاسير العربية:
كَلَّاۖ بَلۡۜ رَانَ عَلَىٰ قُلُوبِهِم مَّا كَانُواْ يَكۡسِبُونَ
Iyayi, sichoncho! Koma yaphimbidwa mitima yawo ndi dzimbiri (la machimo) omwe akhala akukolola.[402]
[402] Munthu akachita choipa koyamba ndipo osalapa, limalowa dontho lakuda mu mtima mwake; nthawi iliyonse pamene akuonjezera machimo, dontho lija limakulirakulira mpaka kuuphimba mtima wonse. Dontho limeneli ndilo likutchedwa “Ran.” Tsono mtima ngati utaphimbidwa chotere sulabadira kuchita zoipa, ngakhale kuti auongole sungaongoke.
التفاسير العربية:
كَلَّآ إِنَّهُمۡ عَن رَّبِّهِمۡ يَوۡمَئِذٖ لَّمَحۡجُوبُونَ
Ayi ndithu iwo (okanira) tsiku limenelo) adzatchingidwa kwa Mbuye wawo; (sadzamuona).
التفاسير العربية:
ثُمَّ إِنَّهُمۡ لَصَالُواْ ٱلۡجَحِيمِ
Pambuyo pake adzalowa ku Moto; (oyaka)
التفاسير العربية:
ثُمَّ يُقَالُ هَٰذَا ٱلَّذِي كُنتُم بِهِۦ تُكَذِّبُونَ
Kenaka adzauzidwa (powaliritsa) “Ichi nchilango chomwe mudali kuchitsutsa (pa dziko lapansi).”
التفاسير العربية:
كَلَّآ إِنَّ كِتَٰبَ ٱلۡأَبۡرَارِ لَفِي عِلِّيِّينَ
Zoona, ndithu kaundula wa anthu abwino (ochita ntchito zabwino) ali mu Illiyyun.
التفاسير العربية:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا عِلِّيُّونَ
Nanga nchiyani chitakudziwitse za Illiyyun?
التفاسير العربية:
كِتَٰبٞ مَّرۡقُومٞ
Ameneyu ndi kaundula (wamkulu) yemwe walembedwa (mkati mwake ntchito za anthu abwino);
التفاسير العربية:
يَشۡهَدُهُ ٱلۡمُقَرَّبُونَ
Amamuyikira umboni (angelo) amene ayandikitsidwa (kwa Allah).
التفاسير العربية:
إِنَّ ٱلۡأَبۡرَارَ لَفِي نَعِيمٍ
Ndithu ochita zabwino adzakhala mu mtendere,
التفاسير العربية:
عَلَى ٱلۡأَرَآئِكِ يَنظُرُونَ
Atakhala pa mipando ya ulemu uku akuyang’ana (zimene Allah wawapatsa monga mtendere ndi ulemelero).
التفاسير العربية:
تَعۡرِفُ فِي وُجُوهِهِمۡ نَضۡرَةَ ٱلنَّعِيمِ
Udzaona kuwala kwa mtendere pa nkhope zawo;
التفاسير العربية:
يُسۡقَوۡنَ مِن رَّحِيقٖ مَّخۡتُومٍ
Adzamwetsedwa vinyo (woyeretsedwa) wotsekeredwa ndi zitsekerero zolimba;
التفاسير العربية:
خِتَٰمُهُۥ مِسۡكٞۚ وَفِي ذَٰلِكَ فَلۡيَتَنَافَسِ ٱلۡمُتَنَٰفِسُونَ
Komalizira kwake (kwa vinyoyo) kuzikatuluka fungo la misk; kuti akapeze zimenezi, apikisane opikisana.[403]
[403] Apa, akutilamula kupikisana pakuchita zabwino kuti tipeze madalitso amene awakonzera anthu abwino. Kumeneko ndikuti munthu aliyense alimbikire kuchita mapemphero ndi zina zabwino.
التفاسير العربية:
وَمِزَاجُهُۥ مِن تَسۡنِيمٍ
Ndipo chosakanizira cha vinyoyo ndi madzi a Tasnim.
التفاسير العربية:
عَيۡنٗا يَشۡرَبُ بِهَا ٱلۡمُقَرَّبُونَ
(Tasnim ameneyo) ndi kasupe amene azikamwa amene ayandikitsidwa (kwa Allah.)
التفاسير العربية:
إِنَّ ٱلَّذِينَ أَجۡرَمُواْ كَانُواْ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ يَضۡحَكُونَ
Ndithu amene adachita machimo adali kuwaseka (mwachipongwe) okhulupirira (pa dziko lapansi);
التفاسير العربية:
وَإِذَا مَرُّواْ بِهِمۡ يَتَغَامَزُونَ
(Okhulupirira) akadutsa pafupi ndi iwo ankakodolerana maso (mwachipongwe);
التفاسير العربية:
وَإِذَا ٱنقَلَبُوٓاْ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِمُ ٱنقَلَبُواْ فَكِهِينَ
Ndipo akabwerera kwa anzawo amabwerera akusangalala (ndi kunyozedwa kwa okhulupirira);
التفاسير العربية:
وَإِذَا رَأَوۡهُمۡ قَالُوٓاْ إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ لَضَآلُّونَ
Ndipo (nthawi zonse) akawaona Asilamu amanena: “Ndithu awa ndi osokera (chifukwa chomkhulupirira Mtumiki).” (s.a.w)
التفاسير العربية:
وَمَآ أُرۡسِلُواْ عَلَيۡهِمۡ حَٰفِظِينَ
Sanatumizidwe (Akafiri) kukhala ayang’aniri kwa okhulupirira (ndikuwaweruza zakulungama ndi kusokera).
التفاسير العربية:
فَٱلۡيَوۡمَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مِنَ ٱلۡكُفَّارِ يَضۡحَكُونَ
Basi lero okhulupirira awaseka osakhulupirira (powabwezera chipongwe chawo chimene ankachita pa dziko lapansi),[404]
[404] (Ndime 34-36) Tanthauzo lake ndikuti okhulupilira, tsiku lachimaliziro adzakhala m’mipando ya ulemu uku akuwayang’ana ndi kuwaseka anthu osakhulupilira ali m’mavuto monga momwe iwo adali kuseka okhulupilira pa dziko lapansi.
التفاسير العربية:
عَلَى ٱلۡأَرَآئِكِ يَنظُرُونَ
Atakhala pa mipando ya ulemu uku akuyang’ana (mtendere umene Allah wawapatsa).
التفاسير العربية:
هَلۡ ثُوِّبَ ٱلۡكُفَّارُ مَا كَانُواْ يَفۡعَلُونَ
Kodi alipidwa osakhulupirira pa zomwe ankachita zija (pa dziko lapansi)?
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني سورة: المطففين
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - فهرس التراجم

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

إغلاق