Check out the new design

పవిత్ర ఖురాన్ యొక్క భావార్థాల అనువాదం - షిషివా అనువాదం - ఖాలిద్ ఇబ్రాహీమ్ బీతాలా * - అనువాదాల విషయసూచిక


భావార్ధాల అనువాదం సూరహ్: అల్-ఇస్రా   వచనం:
وَإِن كَادُواْ لَيَسۡتَفِزُّونَكَ مِنَ ٱلۡأَرۡضِ لِيُخۡرِجُوكَ مِنۡهَاۖ وَإِذٗا لَّا يَلۡبَثُونَ خِلَٰفَكَ إِلَّا قَلِيلٗا
Ndipo padatsala pang’ono kuti akusowetse mtendere m’dziko ili (la Makka) kuti akutulutse m’menemo; koma pambuyo pako sakadakhala (ndi moyo) kupatula (nthawi) yochepa.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
سُنَّةَ مَن قَدۡ أَرۡسَلۡنَا قَبۡلَكَ مِن رُّسُلِنَاۖ وَلَا تَجِدُ لِسُنَّتِنَا تَحۡوِيلًا
Chimenechi ndi chikhalidwe cha omwe tidawatuma patsogolo pako mwa atumiki Athu, ndipo supeza kusintha pachikhalidwe Chathu.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
أَقِمِ ٱلصَّلَوٰةَ لِدُلُوكِ ٱلشَّمۡسِ إِلَىٰ غَسَقِ ٱلَّيۡلِ وَقُرۡءَانَ ٱلۡفَجۡرِۖ إِنَّ قُرۡءَانَ ٱلۡفَجۡرِ كَانَ مَشۡهُودٗا
Pemphera Swala (za Farazi), dzuwa likapendeka mpaka mu mdima wausiku (zomwe ndi Swala za Dhuhri, Asri, Maghrib ndi Isha), ndipo pempheranso Swala ya Fajir: ndithu Swala ya Fajir amaichitira umboni (angelo).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَمِنَ ٱلَّيۡلِ فَتَهَجَّدۡ بِهِۦ نَافِلَةٗ لَّكَ عَسَىٰٓ أَن يَبۡعَثَكَ رَبُّكَ مَقَامٗا مَّحۡمُودٗا
Ndipo pakati pa usiku, dzuka mtulo ndi kupemphera Swala; ilo ndipemphero loonjezera pa iwe, kuti Mbuye wako akakuimike pamalo pa ulemu potamandidwa (ndi zolengedwa zonse pa tsiku la Qiyâma.)
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَقُل رَّبِّ أَدۡخِلۡنِي مُدۡخَلَ صِدۡقٖ وَأَخۡرِجۡنِي مُخۡرَجَ صِدۡقٖ وَٱجۡعَل لِّي مِن لَّدُنكَ سُلۡطَٰنٗا نَّصِيرٗا
Ndipo nena (mawu awa pomwe ukupemphera): “Mbuye wanga! Ndilowetseni, kulowetsa kwabwino (paliponse pamene ndikulowa), ndiponso nditulutseni, kutulutsa kwabwino (paliponse pamene ndikutuluka); ndipatseni mphamvu zochokera kwa Inu zondithandiza ndi kugonjetsera adani.”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَقُلۡ جَآءَ ٱلۡحَقُّ وَزَهَقَ ٱلۡبَٰطِلُۚ إِنَّ ٱلۡبَٰطِلَ كَانَ زَهُوقٗا
Ndipo nena: “Choonadi chafika, ndipo chachabe chachoka; ndithu chachabe ndichochoka (ngakhale patapita nthawi yaitali).”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَنُنَزِّلُ مِنَ ٱلۡقُرۡءَانِ مَا هُوَ شِفَآءٞ وَرَحۡمَةٞ لِّلۡمُؤۡمِنِينَ وَلَا يَزِيدُ ٱلظَّٰلِمِينَ إِلَّا خَسَارٗا
Ndipo tikuivumbulutsa Qur’an yomwe imachiritsa (matenda a mmitima) ndiponso ndi chifundo kwa okhulupirira. Komabe osalungama siikuwaonjezera (kanthu kena) koma kutayika.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَإِذَآ أَنۡعَمۡنَا عَلَى ٱلۡإِنسَٰنِ أَعۡرَضَ وَنَـَٔا بِجَانِبِهِۦ وَإِذَا مَسَّهُ ٱلشَّرُّ كَانَ يَـُٔوسٗا
Ndipo tikampatsa chisomo munthu, (monga moyo wangwiro ndikupeza bwino), amatembenuka (ndikusiya kutikumbukira ndikutipempha), ndipo amadziika kutali (ndi Ife chifukwa chakudzitama ndikudzikuza), koma masautso akamkhudza, (monga matenda ndi umphawi) amataya mtima kwambiri.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
قُلۡ كُلّٞ يَعۡمَلُ عَلَىٰ شَاكِلَتِهِۦ فَرَبُّكُمۡ أَعۡلَمُ بِمَنۡ هُوَ أَهۡدَىٰ سَبِيلٗا
Nena (iwe Mneneri, kwa osakhulupirira a Chikuraishi,): “Aliyense (wa ife ndi inu) akuchita ntchito (zake ndikuyenda panjira yake) ndipo Mbuye wanu Ngodziwa kwambiri za yemwe ali panjira yolondola (potsatira choonadi).”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَيَسۡـَٔلُونَكَ عَنِ ٱلرُّوحِۖ قُلِ ٱلرُّوحُ مِنۡ أَمۡرِ رَبِّي وَمَآ أُوتِيتُم مِّنَ ٱلۡعِلۡمِ إِلَّا قَلِيلٗا
Ndipo akukufunsa (iwe, Muhammad (s.a.w), anthu ako mokhwiriziridwa ndi Ayuda) za Mzimu. Nena: “Mzimu ndi chinthu chomwe akuchidziwa Mbuye wanga Yekha; ndipo inu simudapatsidwe nzeru (zozindikilira zinthu) koma pang’ono chabe, (poyerekeza ndi nzeru za Allah).”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَئِن شِئۡنَا لَنَذۡهَبَنَّ بِٱلَّذِيٓ أَوۡحَيۡنَآ إِلَيۡكَ ثُمَّ لَا تَجِدُ لَكَ بِهِۦ عَلَيۡنَا وَكِيلًا
Ndipo tikadafuna kufufuta Qur’an (pachifuwa chako) yomwe takuvumbulutsira, (tikadatha kutero). Kenako sukadapeza kwa Ife wokuimilira ndi kukupulumutsa.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
 
భావార్ధాల అనువాదం సూరహ్: అల్-ఇస్రా
సూరాల విషయసూచిక పేజీ నెంబరు
 
పవిత్ర ఖురాన్ యొక్క భావార్థాల అనువాదం - షిషివా అనువాదం - ఖాలిద్ ఇబ్రాహీమ్ బీతాలా - అనువాదాల విషయసూచిక

దానిని అనువదించినది ఖాలిద్ ఇబ్రాహీం బీతాలా.

మూసివేయటం