పవిత్ర ఖురాన్ యొక్క భావార్థాల అనువాదం - చిచియో అనువాదం * - అనువాదాల విషయసూచిక


భావార్ధాల అనువాదం సూరహ్: సూరహ్ అల్ ఖమర్   వచనం:

సూరహ్ అల్ ఖమర్

ٱقۡتَرَبَتِ ٱلسَّاعَةُ وَٱنشَقَّ ٱلۡقَمَرُ
Nthawi ya chimaliziro (Qiyâma) yayandikira ndipo mwezi wagawikana.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَإِن يَرَوۡاْ ءَايَةٗ يُعۡرِضُواْ وَيَقُولُواْ سِحۡرٞ مُّسۡتَمِرّٞ
Koma akaona chozizwitsa akunyoza ndi kunena kuti: “Awa ndi matsenga womkeramkera patsogolo.”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَكَذَّبُواْ وَٱتَّبَعُوٓاْ أَهۡوَآءَهُمۡۚ وَكُلُّ أَمۡرٖ مُّسۡتَقِرّٞ
Ndipo adatsutsa (choonadi) ndi kutsatira zilakolako (zawo zoipa) koma chinthu chilichonse (cha Allah) nchokhazikika.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ جَآءَهُم مِّنَ ٱلۡأَنۢبَآءِ مَا فِيهِ مُزۡدَجَرٌ
Ndipo ndithu zidawafika nkhani zomwe zili zokwanira kuwaopseza.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
حِكۡمَةُۢ بَٰلِغَةٞۖ فَمَا تُغۡنِ ٱلنُّذُرُ
Nzeru zokwana koma machenjezo (kwa iwo) sanawathandize.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فَتَوَلَّ عَنۡهُمۡۘ يَوۡمَ يَدۡعُ ٱلدَّاعِ إِلَىٰ شَيۡءٖ نُّكُرٍ
Choncho, apewe (iwe Mtumiki) osakhulupirira, (yembekezani) tsiku loitana woitana (wa Allah) ku chinthu chovuta kwambiri, (chodedwa ndi mitima).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
خُشَّعًا أَبۡصَٰرُهُمۡ يَخۡرُجُونَ مِنَ ٱلۡأَجۡدَاثِ كَأَنَّهُمۡ جَرَادٞ مُّنتَشِرٞ
Maso awo ali zyoli chifukwa chakuopsa; adzatuluka m’manda uku ali ngati dzombe lobalalika (chifukwa cha kuchuluka),
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
مُّهۡطِعِينَ إِلَى ٱلدَّاعِۖ يَقُولُ ٱلۡكَٰفِرُونَ هَٰذَا يَوۡمٌ عَسِرٞ
Akuthamangira kwa woitana (uku atatukula mitu yawo, osatha kucheukira kwina). Adzanena osakhulupirira (tsiku lachiweruziro): “Ili nditsiku lovuta kwambiri.”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
۞ كَذَّبَتۡ قَبۡلَهُمۡ قَوۡمُ نُوحٖ فَكَذَّبُواْ عَبۡدَنَا وَقَالُواْ مَجۡنُونٞ وَٱزۡدُجِرَ
Patsogolo pawo (Aquraishi) anthu a Nuh nawo adatsutsa, adamtsutsa kapolo Wathu nanena kuti: “Uyu ngwamisala!” Ndipo adaopsezedwa (ndi kuzunzidwa ndi mazunzo osiyanasiyana).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فَدَعَا رَبَّهُۥٓ أَنِّي مَغۡلُوبٞ فَٱنتَصِرۡ
(Nuh) adaitana Mbuye wake (nati): “Ine ndagonjetsedwa (ndi anthu anga); choncho ndipulumutseni (kwa iwo).”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فَفَتَحۡنَآ أَبۡوَٰبَ ٱلسَّمَآءِ بِمَآءٖ مُّنۡهَمِرٖ
Tero tidatsekula makomo akumwamba ndi madzi otsika mopitiriza, mwamphamvu.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَفَجَّرۡنَا ٱلۡأَرۡضَ عُيُونٗا فَٱلۡتَقَى ٱلۡمَآءُ عَلَىٰٓ أَمۡرٖ قَدۡ قُدِرَ
Ndipo tidaing’amba nthaka kukhala ndi akasupe (ofwamphuka madzi mwamphamvu). Choncho adakumana madzi (akumwamba ndi am’nthaka kuti awaononge) pamuyeso wopimidwa ndi kulamulidwa (ndi Allah).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَحَمَلۡنَٰهُ عَلَىٰ ذَاتِ أَلۡوَٰحٖ وَدُسُرٖ
Ndipo tidamnyamula Nuh pa chombo chamatabwa chokhomedwa ndi misomali (yamitengo).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
تَجۡرِي بِأَعۡيُنِنَا جَزَآءٗ لِّمَن كَانَ كُفِرَ
Chinkayandama pamadzi ndi kuyang’aniridwa ndi Ife. Iyi ndi mphoto ya (Nuh) yemwe adakanidwa ndi anthu ake.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَد تَّرَكۡنَٰهَآ ءَايَةٗ فَهَلۡ مِن مُّدَّكِرٖ
Ndipo ndithu tidachisiya (chigumula) kukhala phunziro (pakuonongeka kwa osakhulupirira ndi kupulumuka kwa okhulupirira). Kodi alipo wolikumbukira (ndi kupeza nalo malango abwino?)
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فَكَيۡفَ كَانَ عَذَابِي وَنُذُرِ
Kodi chidali bwanji chilango Changa ndi machenjezo Anga (kwa onyoza!)
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ يَسَّرۡنَا ٱلۡقُرۡءَانَ لِلذِّكۡرِ فَهَلۡ مِن مُّدَّكِرٖ
Ndipo ndithu taifewetsa Qur’an kuti ikhale chikumbutso. Kodi alipo woikumbukira (ndi kupeza nayo malangizo abwino?)
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
كَذَّبَتۡ عَادٞ فَكَيۡفَ كَانَ عَذَابِي وَنُذُرِ
Âdi adamtsutsa (mneneri wawo Hud), kodi chidali bwanji chilango Changa ndi machenjezo Anga (kwa onyoza)!
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
إِنَّآ أَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمۡ رِيحٗا صَرۡصَرٗا فِي يَوۡمِ نَحۡسٖ مُّسۡتَمِرّٖ
Ndithu Ife tidawatumizira mphepo yozizira, yaphokoso, m’tsiku latsoka lopitilira,
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
تَنزِعُ ٱلنَّاسَ كَأَنَّهُمۡ أَعۡجَازُ نَخۡلٖ مُّنقَعِرٖ
Idawazula anthu (kuchoka m’malo mwawo ndi kuwaponya panthaka ali akufa) ngati matsinde a mitengo yakanjedza ozulidwa m’malo mwake.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فَكَيۡفَ كَانَ عَذَابِي وَنُذُرِ
Kodi chidali bwanji chilango Changa ndi machenjezo Anga (kwa onyoza)!
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ يَسَّرۡنَا ٱلۡقُرۡءَانَ لِلذِّكۡرِ فَهَلۡ مِن مُّدَّكِرٖ
Ndipo ndithu taifewetsa Qur’an kuti ikhale chikumbutso. Kodi alipo woikumbukira (ndi kupeza nayo malangizo abwino?)
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ بِٱلنُّذُرِ
Asamudu adatsutsa machenjezo.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فَقَالُوٓاْ أَبَشَرٗا مِّنَّا وَٰحِدٗا نَّتَّبِعُهُۥٓ إِنَّآ إِذٗا لَّفِي ضَلَٰلٖ وَسُعُرٍ
Ndipo adati: “Kodi titsatire munthu mmodzi wochokera mwa ife? Ndithu ife ngati titamtsatira ndiye kuti tili nkusokera ndiponso misala.”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
أَءُلۡقِيَ ٱلذِّكۡرُ عَلَيۡهِ مِنۢ بَيۡنِنَا بَلۡ هُوَ كَذَّابٌ أَشِرٞ
Kodi am’vumbulutsira iye chikumbutso pakati pathu, (pomwe tili nawo oposa iye pa ulemelero)? Koma iye ndiwabodza ndi wodzitukumu.”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
سَيَعۡلَمُونَ غَدٗا مَّنِ ٱلۡكَذَّابُ ٱلۡأَشِرُ
Mawa lino adzadziwa (tsiku lakuwatsikira chilango,) kuti ndiyani wabodza wodzitukumula (iwo kapena Swaleh).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
إِنَّا مُرۡسِلُواْ ٱلنَّاقَةِ فِتۡنَةٗ لَّهُمۡ فَٱرۡتَقِبۡهُمۡ وَٱصۡطَبِرۡ
(Tidamuuza mneneriyo kuti) ndithu Ife titumiza ngamira yaikazi kuti ikhale mayeso kwa iwo. Choncho adikire, ndipo pirira.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَنَبِّئۡهُمۡ أَنَّ ٱلۡمَآءَ قِسۡمَةُۢ بَيۡنَهُمۡۖ كُلُّ شِرۡبٖ مُّحۡتَضَرٞ
Ndipo auze kuti madzi agawidwa pakati pawo (ndi ngamira). Aliyense ali ndi tsiku lopita kukatunga.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فَنَادَوۡاْ صَاحِبَهُمۡ فَتَعَاطَىٰ فَعَقَرَ
Koma adaitana mnzawo (wa mphulupulu). Choncho adakonzeka kupha ngamirayo ndipo adaipha.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فَكَيۡفَ كَانَ عَذَابِي وَنُذُرِ
Kodi chidali bwanji chilango Changa ndi machenjezo Anga (kwa anthu otsutsa)!
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
إِنَّآ أَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمۡ صَيۡحَةٗ وَٰحِدَةٗ فَكَانُواْ كَهَشِيمِ ٱلۡمُحۡتَظِرِ
Ndithu tidawatumizira nkuwe umodzi choncho adakhala ngati udzu ndi mitengo youma yaomanga khola.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ يَسَّرۡنَا ٱلۡقُرۡءَانَ لِلذِّكۡرِ فَهَلۡ مِن مُّدَّكِرٖ
Ndipo ndithu taifewetsa Qur’an kuti ikhale chikumbutso. Kodi alipo woikumbukira (ndi kupeza nayo malangizo abwino?)
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
كَذَّبَتۡ قَوۡمُ لُوطِۭ بِٱلنُّذُرِ
Anthu a Luti adatsutsa machenjezo (a mneneri wawo).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
إِنَّآ أَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمۡ حَاصِبًا إِلَّآ ءَالَ لُوطٖۖ نَّجَّيۡنَٰهُم بِسَحَرٖ
Ndithu Ife tidawatumizira chimphepo champhamvu choulutsa miyala (ndi kuwagenda), kupatula akubanja la Luti; tidawapulumutsa (ku chilangocho) m’bandakucha,
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
نِّعۡمَةٗ مِّنۡ عِندِنَاۚ كَذَٰلِكَ نَجۡزِي مَن شَكَرَ
(Choncho kupulumukako kudali) chisomo chochokera kwa Ife (pa iwo). Momwemo ndimo timamlipirira wothokoza.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ أَنذَرَهُم بَطۡشَتَنَا فَتَمَارَوۡاْ بِٱلنُّذُرِ
Ndipo ndithu (Luti) adawachenjeza anthu ake za kulanga Kwathu koopsa. Koma adakaikira machenjezo (ake ndi kumtsutsa).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ رَٰوَدُوهُ عَن ضَيۡفِهِۦ فَطَمَسۡنَآ أَعۡيُنَهُمۡ فَذُوقُواْ عَذَابِي وَنُذُرِ
Ndipo ndithu adafuna kwa iye kuti awapatse alendo ake (kuti achite nawo zauve), koma tidafafaniza maso awo (kuti ikhale mphoto pa zimene adafunazo). (Ndipo tidawauza): “Choncho lawani chilango Changa ndi machenjezo Anga.”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ صَبَّحَهُم بُكۡرَةً عَذَابٞ مُّسۡتَقِرّٞ
Ndipo ndithu chidawadzera mwadzidzidzi chilango chokhazikika, nthawi yam’mamawa.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فَذُوقُواْ عَذَابِي وَنُذُرِ
Choncho (kudanenedwa kwa iwo) “Lawani chilango Changa ndi machenjezo Anga.”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ يَسَّرۡنَا ٱلۡقُرۡءَانَ لِلذِّكۡرِ فَهَلۡ مِن مُّدَّكِرٖ
Ndipo ndithu taifewetsa Qur’an (kuti ikhale chikumbutso). Kodi alipo woikumbukira (ndi kupeza nayo malangizo abwino)?
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ جَآءَ ءَالَ فِرۡعَوۡنَ ٱلنُّذُرُ
Ndipo ndithu machenjezo (ondondozana) adawadzera anthu a Farawo (ndi iye mwini).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا كُلِّهَا فَأَخَذۡنَٰهُمۡ أَخۡذَ عَزِيزٖ مُّقۡتَدِرٍ
Adatsutsa zozizwitsa Zathu zonse (zimene zidadza kupyolera m’manja mwa aneneri Athu). Choncho tidawalanga, kulanga kwa Wamphamvu (Wosapambanidwa), Wokhoza.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
أَكُفَّارُكُمۡ خَيۡرٞ مِّنۡ أُوْلَٰٓئِكُمۡ أَمۡ لَكُم بَرَآءَةٞ فِي ٱلزُّبُرِ
Kodi osakhulupirira anuwa ndi abwino kuposa iwo (kotero kuti sadzaonongedwa)? Kapena zalembedwa m’mabuku kuti inu mdzasiyidwa (sadzakuonongani monga momwe adawaonongera akale?)
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
أَمۡ يَقُولُونَ نَحۡنُ جَمِيعٞ مُّنتَصِرٞ
Kapena akunena kuti: “Ife ndiochuluka titha kudziteteza (palibe angatipambane)?”
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
سَيُهۡزَمُ ٱلۡجَمۡعُ وَيُوَلُّونَ ٱلدُّبُرَ
(Auze): Gululo ligonjetsedwa ndipo athawa ndi kutembenuza misana.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
بَلِ ٱلسَّاعَةُ مَوۡعِدُهُمۡ وَٱلسَّاعَةُ أَدۡهَىٰ وَأَمَرُّ
Koma lonjezo la chilango chawo ndi tsiku la chiweruziro, ndipo tsiku la chiweruziro ndi latsoka lalikulu, lowawa kwabasi (kwa osakhulupirira).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
إِنَّ ٱلۡمُجۡرِمِينَ فِي ضَلَٰلٖ وَسُعُرٖ
Ndithu oipa (mwa awa ndi aja) ali nkusokera ndi misala.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
يَوۡمَ يُسۡحَبُونَ فِي ٱلنَّارِ عَلَىٰ وُجُوهِهِمۡ ذُوقُواْ مَسَّ سَقَرَ
Tsiku limene adzakokedwera ku Moto ndi nkhope zawo, (kudzanenedwa kwa iwo:) “Lawani zowawa za Jahena (ndi kutentha kwake)!
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
إِنَّا كُلَّ شَيۡءٍ خَلَقۡنَٰهُ بِقَدَرٖ
Ndithu Ife tachilenga chinthu chilichonse ndi muyeso (kulingana ndi zolinga).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَمَآ أَمۡرُنَآ إِلَّا وَٰحِدَةٞ كَلَمۡحِۭ بِٱلۡبَصَرِ
Ndipo silili lamulo Lathu (pa chinthu tikachifuna) koma liwu limodzi, (timangoti kwa chinthucho: “Chitika.” Ndipo chimachitika mwachangu) ngati kuphethira kwa diso.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَلَقَدۡ أَهۡلَكۡنَآ أَشۡيَاعَكُمۡ فَهَلۡ مِن مُّدَّكِرٖ
Ndipo ndithu tidawaononga anzanu (onga inu osakhulupirira): Kodi alipo wokumbuka?
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَكُلُّ شَيۡءٖ فَعَلُوهُ فِي ٱلزُّبُرِ
Ndipo chinthu chilichonse adachichita iwowo (pa dziko lapansi) chili mkaundula.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
وَكُلُّ صَغِيرٖ وَكَبِيرٖ مُّسۡتَطَرٌ
Ndipo ntchito iliyonse, yaing’ono kapena yaikulu, idalembedwa; (palibe chimene chingamsowe).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
إِنَّ ٱلۡمُتَّقِينَ فِي جَنَّٰتٖ وَنَهَرٖ
Ndithu oopa Allah adzakhala m’Minda ya ulemelero waukulu ndi Mitsinje (yosiyanasiyana).
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
فِي مَقۡعَدِ صِدۡقٍ عِندَ مَلِيكٖ مُّقۡتَدِرِۭ
Pokhala pabwino pachoonadi, (popanda mawu achabe ndi machimo), kwa Mfumu yokhoza chilichonse.
అరబీ భాషలోని ఖుర్ఆన్ వ్యాఖ్యానాలు:
 
భావార్ధాల అనువాదం సూరహ్: సూరహ్ అల్ ఖమర్
సూరాల విషయసూచిక పేజీ నెంబరు
 
పవిత్ర ఖురాన్ యొక్క భావార్థాల అనువాదం - చిచియో అనువాదం - అనువాదాల విషయసూచిక

చిచియో భాషలో అల్ ఖుర్ఆన్ అల్ కరీమ్ భావానువాదం - అనువాదం ఖాలిద్ ఇబ్రాహీమ్ బైతాలా - 2020 ముద్రణ.

మూసివేయటం