Check out the new design

แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - โดยคอลิด อิบรอฮีม เบตาลา * - สารบัญ​คำแปล


แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: Al-Munāfiqūn   อายะฮ์:

Al-Munâfiqûn

إِذَا جَآءَكَ ٱلۡمُنَٰفِقُونَ قَالُواْ نَشۡهَدُ إِنَّكَ لَرَسُولُ ٱللَّهِۗ وَٱللَّهُ يَعۡلَمُ إِنَّكَ لَرَسُولُهُۥ وَٱللَّهُ يَشۡهَدُ إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ لَكَٰذِبُونَ
Akakudzera achiphamaso akunena kuti: “Tikuikira umboni kuti ndithu iwe ndiwe Mtumiki wa Allah, ndipo Allah akudziwa kuti iwe ndiwe mtumiki Wake. Ndipo Allah akuikira umboni kuti achiphamaso ngabodza (pa zomwe akunena).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ٱتَّخَذُوٓاْ أَيۡمَٰنَهُمۡ جُنَّةٗ فَصَدُّواْ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِۚ إِنَّهُمۡ سَآءَ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Kulumbira kwawo (kwa bodza) akuchita kukhala chotetezera (chuma chawo ndi matupi awo). Tero atsekereza (anthu kuyenda) panjira ya Allah. Ndithu nzoipa zedi zimene amachita.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ذَٰلِكَ بِأَنَّهُمۡ ءَامَنُواْ ثُمَّ كَفَرُواْ فَطُبِعَ عَلَىٰ قُلُوبِهِمۡ فَهُمۡ لَا يَفۡقَهُونَ
Zimenezo nchifukwa chakuti iwo adakhulupirira (modzionetsera), kenako adakana (mobisa). Choncho mitima yawo idatsekedwa kotero kuti iwo sangathe kuzindikira (chimene chingawapulumutse ku chilango cha Allah.)
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
۞ وَإِذَا رَأَيۡتَهُمۡ تُعۡجِبُكَ أَجۡسَامُهُمۡۖ وَإِن يَقُولُواْ تَسۡمَعۡ لِقَوۡلِهِمۡۖ كَأَنَّهُمۡ خُشُبٞ مُّسَنَّدَةٞۖ يَحۡسَبُونَ كُلَّ صَيۡحَةٍ عَلَيۡهِمۡۚ هُمُ ٱلۡعَدُوُّ فَٱحۡذَرۡهُمۡۚ قَٰتَلَهُمُ ٱللَّهُۖ أَنَّىٰ يُؤۡفَكُونَ
Ndipo ukawaona, akukondweretsa matupi awo; ndipo akayankhula umvetsera zoyankhula zawo (chifukwa chakuthwa kwa malirime awo, pomwe mkati mwawo ndiming’oma yopanda kanthu); iwo ali ngati matsinde a mitengo yomwe yayadzamiritsidwa (ku chipupa); (mwa iwo mulibe moyo). Mkuwe uliwonse (umene akuumva) akuganiza kuti ukulinga iwo, (chifukwa cha kuzindikira chinyengo chawo); iwowa ndiadani; chenjerani nawo. Allah awatembelere! Mwanjira yanji akuchotsedwa (ku choonadi)!
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
 
แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: Al-Munāfiqūn
สารบัญสูเราะฮ์ หมายเลข​หน้า​
 
แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - โดยคอลิด อิบรอฮีม เบตาลา - สารบัญ​คำแปล

แปลโดย คอลิด อิบรอฮีม เบตาลา

ปิด