Check out the new design

แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - โดยคอลิด อิบรอฮีม เบตาลา * - สารบัญ​คำแปล


แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: Al-A‘rāf   อายะฮ์:
قَالُوٓاْ ءَامَنَّا بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Adati: “Takhulupirira Mbuye wa zolengedwa zonse.”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
رَبِّ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
“Mbuye wa Mûsa Ndi Harun.”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
قَالَ فِرۡعَوۡنُ ءَامَنتُم بِهِۦ قَبۡلَ أَنۡ ءَاذَنَ لَكُمۡۖ إِنَّ هَٰذَا لَمَكۡرٞ مَّكَرۡتُمُوهُ فِي ٱلۡمَدِينَةِ لِتُخۡرِجُواْ مِنۡهَآ أَهۡلَهَاۖ فَسَوۡفَ تَعۡلَمُونَ
Farawo adati: “Mwamkhulupirira chotani iye ndisanakupatseni chilolezo? Ndithu iyi ndi ndale yomwe mwaichita mu mzindamu (inu ndi Mûsa) kuti muwatulutsemo eni mzindawo. Koma posachedwa mudziwa (chimene ndikuchiteni).”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
لَأُقَطِّعَنَّ أَيۡدِيَكُمۡ وَأَرۡجُلَكُم مِّنۡ خِلَٰفٖ ثُمَّ لَأُصَلِّبَنَّكُمۡ أَجۡمَعِينَ
“Ndithudi, nditseteka manja anu ndi miyendo yanu mosinthanitsa; (kudula dzanja lakudzanjadzanja ndi mwendo wa kumanzere, kapena dzanja la kumanzere ndi mwendo wakudzanjadzanja). Kenako ndikupachikani nonsenu.”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
قَالُوٓاْ إِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا مُنقَلِبُونَ
(Iwo) adati: “Ndithu ife kwa Mbuye wathu ngobwerera.”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَا تَنقِمُ مِنَّآ إِلَّآ أَنۡ ءَامَنَّا بِـَٔايَٰتِ رَبِّنَا لَمَّا جَآءَتۡنَاۚ رَبَّنَآ أَفۡرِغۡ عَلَيۡنَا صَبۡرٗا وَتَوَفَّنَا مُسۡلِمِينَ
“Komatu palibe choipa chimene waona mwa ife kupatula kuti takhulupirira zizindikiro za Mbuye wathu pamene zatidzera. E Mbuye wathu! Titsanulireni chipiliro, ndipo tipatseni imfa uku tili Asilamu (ogonjera Inu).”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَقَالَ ٱلۡمَلَأُ مِن قَوۡمِ فِرۡعَوۡنَ أَتَذَرُ مُوسَىٰ وَقَوۡمَهُۥ لِيُفۡسِدُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَيَذَرَكَ وَءَالِهَتَكَۚ قَالَ سَنُقَتِّلُ أَبۡنَآءَهُمۡ وَنَسۡتَحۡيِۦ نِسَآءَهُمۡ وَإِنَّا فَوۡقَهُمۡ قَٰهِرُونَ
Ndipo nduna za mwa anthu a Farawo zidati (kwa Farawo): “Kodi umuleka Mûsa ndi anthu ake kuti abwere ndi chisokonezo m’dziko, ndi kuti akusiye iwe ndi milungu yako (yomwe adatilangiza makolo athu kuti tipembedze pamodzi ndi iwe)? (Farawo) Adati: “Tipha ana awo achimuna ndikuwasiya amoyo (ana awo) achikazi. Ndithudi ife pa iwo tili ndi mphamvu zowagonjetsera.”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
قَالَ مُوسَىٰ لِقَوۡمِهِ ٱسۡتَعِينُواْ بِٱللَّهِ وَٱصۡبِرُوٓاْۖ إِنَّ ٱلۡأَرۡضَ لِلَّهِ يُورِثُهَا مَن يَشَآءُ مِنۡ عِبَادِهِۦۖ وَٱلۡعَٰقِبَةُ لِلۡمُتَّقِينَ
Mûsa adauza anthu ake: “Pemphani chithandizo kwa Allah, ndipo pirirani. Ndithu dzikoli ndi la Allah; amalipereka kwa amene wamfuna mwa akapolo Ake. Ndipo mapeto abwino nga anthu olungama.”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
قَالُوٓاْ أُوذِينَا مِن قَبۡلِ أَن تَأۡتِيَنَا وَمِنۢ بَعۡدِ مَا جِئۡتَنَاۚ قَالَ عَسَىٰ رَبُّكُمۡ أَن يُهۡلِكَ عَدُوَّكُمۡ وَيَسۡتَخۡلِفَكُمۡ فِي ٱلۡأَرۡضِ فَيَنظُرَ كَيۡفَ تَعۡمَلُونَ
(Iwo) adati: “Takhala tikuzunzidwa usanatidzere ndiponso (tsopano) pamene watidzera.” (Mûsa) adati: “Mwina Mbuye wanu amuononga mdani wanu ndipo akuchitani kukhala alowammalo m’dzikoli, ndi kuti aone mmene mungachitire.”
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَلَقَدۡ أَخَذۡنَآ ءَالَ فِرۡعَوۡنَ بِٱلسِّنِينَ وَنَقۡصٖ مِّنَ ٱلثَّمَرَٰتِ لَعَلَّهُمۡ يَذَّكَّرُونَ
Ndithu tidawakhaulitsa anthu a Farawo ndi chilala, ndi kuchepekedwa zokolola; kuti mwina angakumbukire.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
 
แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: Al-A‘rāf
สารบัญสูเราะฮ์ หมายเลข​หน้า​
 
แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - โดยคอลิด อิบรอฮีม เบตาลา - สารบัญ​คำแปล

แปลโดย คอลิด อิบรอฮีม เบตาลา

ปิด