Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Ayah: (156) Surah: Āl-‘Imrān
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَكُونُواْ كَٱلَّذِينَ كَفَرُواْ وَقَالُواْ لِإِخۡوَٰنِهِمۡ إِذَا ضَرَبُواْ فِي ٱلۡأَرۡضِ أَوۡ كَانُواْ غُزّٗى لَّوۡ كَانُواْ عِندَنَا مَا مَاتُواْ وَمَا قُتِلُواْ لِيَجۡعَلَ ٱللَّهُ ذَٰلِكَ حَسۡرَةٗ فِي قُلُوبِهِمۡۗ وَٱللَّهُ يُحۡيِۦ وَيُمِيتُۗ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرٞ
E inu amene mwakhulupirira! Musakhale ngati amene sadakhulupirire, nanena za anzawo pamene akuyenda pa dziko kapena pomwe akumenyana nkhondo (ndikufera konko): “Akadakhala ndi ife sakadafa, ndiponso sakadaphedwa.” Allah (adawathira maganizo amenewa) kuti azipange zimenezo kukhala zodandaulitsa m’mitima mwawo. Komatu Allah ndi amene amapereka moyo ndi imfa. Ndipo Allah akuona zonse zomwe mukuchita.[96]
[96] (Ndime 156-157) Apa Asilamu akuwapepesa kuti asaganizire kuti imfayo yawapeza anzawo chifukwa chopita ku nkhondo nkuti akadapanda kupitako sakadafa. Koma akuwauza kuti adafa chifukwa nthawi yawo yomwe Allah adawalembera kuti akhale pa dziko lapansi idatha. Ndipo ngakhale akadakhala m’nyumba zawo imfa ikadawapezabe. Ndipo akuwauzanso kuti imfa yofera ku nkhondo yoyera njabwino kuposa yofera pakhomo.
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Ayah: (156) Surah: Āl-‘Imrān
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara