Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Ayah: (9) Surah: Al-Ahzāb
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱذۡكُرُواْ نِعۡمَةَ ٱللَّهِ عَلَيۡكُمۡ إِذۡ جَآءَتۡكُمۡ جُنُودٞ فَأَرۡسَلۡنَا عَلَيۡهِمۡ رِيحٗا وَجُنُودٗا لَّمۡ تَرَوۡهَاۚ وَكَانَ ٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ بَصِيرًا
E inu amene mwakhulupirira! Kumbukirani chisomo cha Allah chimene chili pa inu, pamene adakudzerani magulu a nkhondo. Ndipo tidawatumizira mphepo ndi magulu a nkhondo (a angelo) amene simudawaone. Ndipo Allah akuona (zonse) zimene mukuchita.[318]
[318] Pamene Mtumiki (s.a.w) adali mu mzinda wa Madina adamzinga magulu ambiri a nkhondo omwe ena a iwo adali a mtundu wa Ghatfan, Ayuda a Chikuraidha ndi Ayuda a Bani Nadhir. Adali ochuluka 12,000.
Pamene Mtumiki (s.a.w) adamva za kudza kwawo adakumba chidzenje chachikulu kumbali ina ya mzinda wa Madina yomwe adaiganizira kuti adani angalowereko. Izi zidachitika potsatira malangizo a Salman Farisiyu. Kenako Mtumiki (s.a.w) adatuluka ndi ankhondo ake okwana 3,000 nakamanga mahema awo pafupi ndi chidzenjecho moyang’anizana ndi adani awo. Asilamu adagwidwa ndi mantha aakulu kotero kuti achiphamaso adayamba kuthawa. Koma pompo Allah adatumizira adaniwo chimphepo ndi magulu a nkhondo a angelo omwe sadathe kuwaona ndi maso awo, nawabalalitsa adaniwo ndi kuwatayira katundu wawo kutali.
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Ayah: (9) Surah: Al-Ahzāb
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara