Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا * - Mealler fihristi


Anlam tercümesi Ayet: (170) Sure: Sûratu'l-Bakarah
وَإِذَا قِيلَ لَهُمُ ٱتَّبِعُواْ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ قَالُواْ بَلۡ نَتَّبِعُ مَآ أَلۡفَيۡنَا عَلَيۡهِ ءَابَآءَنَآۚ أَوَلَوۡ كَانَ ءَابَآؤُهُمۡ لَا يَعۡقِلُونَ شَيۡـٔٗا وَلَا يَهۡتَدُونَ
Ndipo kukanenedwa kwa iwo (kuti): “Tsatirani zimene Allah wavumbulutsa;” akunena: “Koma tikutsatira zimene tidawapeza nazo atate athu.” Kodi ngakhale kuti atate awo sadali kuzindikira chilichonse ndiponso sadali oongoka (awatsatirabe)?[12]
[12] Chikhulupiliro cha munthu kuti chikhale champhamvu ndi chopindula pafunika kuti achidziwe bwinobwino chimene akuchikhulupiliracho. Asangotsatira ndikuchikhulupilira chifukwa choti auje ndi auje adali kuchikhulupilira chimenecho. Zinthu zotere zimawasokeretsa anthu ambiri. Anthu ena amachikhulupilira chinthu chifukwa chakuti makolo awo adali kuchikhulupilira pomwe chinthucho chili chachabe.
Allah adatipatsa dalitso lanzeru kuti tizirigwilitsira ntchito pofuna choonadi cha zinthu, osati kumangotsatira ngati wakhungu.
Arapça tefsirler:
 
Anlam tercümesi Ayet: (170) Sure: Sûratu'l-Bakarah
Surelerin fihristi Sayfa numarası
 
Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا - Mealler fihristi

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Kapat