Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Ayah: (170) Surah: Surah Al-Baqarah
وَإِذَا قِيلَ لَهُمُ ٱتَّبِعُواْ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ قَالُواْ بَلۡ نَتَّبِعُ مَآ أَلۡفَيۡنَا عَلَيۡهِ ءَابَآءَنَآۚ أَوَلَوۡ كَانَ ءَابَآؤُهُمۡ لَا يَعۡقِلُونَ شَيۡـٔٗا وَلَا يَهۡتَدُونَ
Ndipo kukanenedwa kwa iwo (kuti): “Tsatirani zimene Allah wavumbulutsa;” akunena: “Koma tikutsatira zimene tidawapeza nazo atate athu.” Kodi ngakhale kuti atate awo sadali kuzindikira chilichonse ndiponso sadali oongoka (awatsatirabe)?[12]
[12] Chikhulupiliro cha munthu kuti chikhale champhamvu ndi chopindula pafunika kuti achidziwe bwinobwino chimene akuchikhulupiliracho. Asangotsatira ndikuchikhulupilira chifukwa choti auje ndi auje adali kuchikhulupilira chimenecho. Zinthu zotere zimawasokeretsa anthu ambiri. Anthu ena amachikhulupilira chinthu chifukwa chakuti makolo awo adali kuchikhulupilira pomwe chinthucho chili chachabe.
Allah adatipatsa dalitso lanzeru kuti tizirigwilitsira ntchito pofuna choonadi cha zinthu, osati kumangotsatira ngati wakhungu.
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Ayah: (170) Surah: Surah Al-Baqarah
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup