Check out the new design

قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا * - ترجمے کی لسٹ


معانی کا ترجمہ سورت: فجر   آیت:

Al-Fajr

وَٱلۡفَجۡرِ
Ndikulumbilira kuyera kwa m’bandakucha; (pamene usiku uthawa).
عربی تفاسیر:
وَلَيَالٍ عَشۡرٖ
Ndi masiku khumi (a mwezi wa Dhul-Hijjah omwe ngopatulika kwa Allah).[430]
[430] Tanthauzo la Ayah iyi ndi masiku khumi olemekezeka omwe ali mkhumi loyamba la mwezi wa Thul-Hijjah umene ndi mwezi wa 12 pa kalendala ya Chisilamu. Amenewa ndi masiku olemekezeka kuposa masiku onse ngakhale masiku a Ramadan kupatula usiku wa LAILA-TUL-QADR, ndi masiku khumi omaliza a mwezi wa Ramadan. Choncho ndi bwino kuchulukitsa mapemphero m’masiku amenewa.
عربی تفاسیر:
وَٱلشَّفۡعِ وَٱلۡوَتۡرِ
Ndi Shaf’i ndi Witri: (nambala yogawika ndi yosagawika).[431]
[431] Shafi ndi nambala yotheka kugawa ndi 2 (even number) Witri ndi nambala yosatheka kuigawa ndi 2 (odd number). Cholinga cha Allah pamenepa ndi kuzilumbilira zinthu zonse zimene adazilenga, zowerengedwa mnjira zonse ziwiri.
عربی تفاسیر:
وَٱلَّيۡلِ إِذَا يَسۡرِ
Ndi usiku pamene ukupita (chifukwa cha kuyenda kwa dziko kodabwitsa).
عربی تفاسیر:
هَلۡ فِي ذَٰلِكَ قَسَمٞ لِّذِي حِجۡرٍ
Kodi m’zimene zatchulidwazi simuli kulumbira kokwanira, kwa munthu wa nzeru?
عربی تفاسیر:
أَلَمۡ تَرَ كَيۡفَ فَعَلَ رَبُّكَ بِعَادٍ
Kodi sudadziwe momwe Mbuye wako adawalangira Âdi (anthu a mneneri Hûd).
عربی تفاسیر:
إِرَمَ ذَاتِ ٱلۡعِمَادِ
Aku Irama; ataliatali ngati zipilala.[432]
[432] (Ndime 7-9) Âdi aku Irama ndi mtundu wa Mneneri Hud. Adali akuluakulu matupi a mphamvu kwambiri mwakuti ankanena kuti: “Ndani wamphamvu kuposa ife!” Thamudu (Samudu) ndi mtundu wa Mneneri Swaleh. Iwowa adali kukhala ku mpoto kwa chilumba cha Arabia.
عربی تفاسیر:
ٱلَّتِي لَمۡ يُخۡلَقۡ مِثۡلُهَا فِي ٱلۡبِلَٰدِ
Omwe onga iwo sadalengedwe m’maiko ena?
عربی تفاسیر:
وَثَمُودَ ٱلَّذِينَ جَابُواْ ٱلصَّخۡرَ بِٱلۡوَادِ
Ndi Asamudu, (anthu a mneneri Swaleh) amene adali kudula matanthwe ku chigwa (chotchedwa Wadi Qura ndi kumamanga nyumba zikuluzikulu)?
عربی تفاسیر:
وَفِرۡعَوۡنَ ذِي ٱلۡأَوۡتَادِ
Komanso Firiauna (Farawo) mwini magulu ankhondo (omwe amalimbikitsa ufumu wake monga momwe zichiri zimalimbikitsira tenti)?
عربی تفاسیر:
ٱلَّذِينَ طَغَوۡاْ فِي ٱلۡبِلَٰدِ
Amene adaipitsa m’maiko mopyola malire?
عربی تفاسیر:
فَأَكۡثَرُواْ فِيهَا ٱلۡفَسَادَ
Ndipo adachulukitsa m’menemo kuononga (pamwamba pa kuononga).[433]
[433] Mzinthu zoipa zimene Farawo adachita, ndi kudzitcha kuti iye ndi mulungu, kupha ana achimuna popanda chilungamo, ndi kuwazunza Aisraeli.
عربی تفاسیر:
فَصَبَّ عَلَيۡهِمۡ رَبُّكَ سَوۡطَ عَذَابٍ
Choncho Mbuye wako adawathira ndi mitundu ya zilango (zoopsa).
عربی تفاسیر:
إِنَّ رَبَّكَ لَبِٱلۡمِرۡصَادِ
Ndithu Mbuye wako ali tcheru (ndi zochita za anthu. Ndipo akuwasungira kuti adzawalipire).[434]
[434] Apa ndikuti Allah akuwaona anthu Ake nthawi ili yonse. Palibe chimene iwo achita popanda Iye kuchiona ndi kuchilemba.
عربی تفاسیر:
فَأَمَّا ٱلۡإِنسَٰنُ إِذَا مَا ٱبۡتَلَىٰهُ رَبُّهُۥ فَأَكۡرَمَهُۥ وَنَعَّمَهُۥ فَيَقُولُ رَبِّيٓ أَكۡرَمَنِ
Pamene munthu Mbuye wake akumuyesa (mayeso) ndikumulemekeza ndi kumpatsa mtendere (wachuma, ulemelero ndi mphamvu) amanena monyada: Mbuye wanga wandilemekeza (chifukwa zimenezi nzondiyenera ine).
عربی تفاسیر:
وَأَمَّآ إِذَا مَا ٱبۡتَلَىٰهُ فَقَدَرَ عَلَيۡهِ رِزۡقَهُۥ فَيَقُولُ رَبِّيٓ أَهَٰنَنِ
Koma akamuyesa mayeso ndi kumchepetsera rizq lake, (chuma) amanena (motaya rntima): Mbuye wanga wandinyoza!
عربی تفاسیر:
كَلَّاۖ بَل لَّا تُكۡرِمُونَ ٱلۡيَتِيمَ
Sichoncho ayi, (monga momwe mukuganizira) koma inu simuchitira za ufulu ana amasiye!
عربی تفاسیر:
وَلَا تَحَٰٓضُّونَ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلۡمِسۡكِينِ
Ndipo simulimbikitsana za kudyetsa osauka,
عربی تفاسیر:
وَتَأۡكُلُونَ ٱلتُّرَاثَ أَكۡلٗا لَّمّٗا
Ndipo mukudya chuma cha masiye; kudya kosusuka.[435]
[435] Arabu asadalowe m’Chisilamu akazi sadali kugawiridwa chuma cha masiye kudzanso ana aang’onoang’ono a masiye sadali kuchiona chumacho.
عربی تفاسیر:
وَتُحِبُّونَ ٱلۡمَالَ حُبّٗا جَمّٗا
Ndiponso mukukonda chuma; kukonda kopyola muyeso.
عربی تفاسیر:
كَلَّآۖ إِذَا دُكَّتِ ٱلۡأَرۡضُ دَكّٗا دَكّٗا
Sichoncho! (Siyani machitidwe amenewa); nthaka ikadzapondedwa (ndikuifafaniza).
عربی تفاسیر:
وَجَآءَ رَبُّكَ وَٱلۡمَلَكُ صَفّٗا صَفّٗا
Ndikubwera Mbuye wako (mmabweredwe omwe akuwadziwa Iye Mwini) ndi angelo ali mmizeremizere.
عربی تفاسیر:
 
معانی کا ترجمہ سورت: فجر
سورتوں کی لسٹ صفحہ نمبر
 
قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا - ترجمے کی لسٹ

خالد ابراہیم پیٹالا نے ترجمہ کیا۔

بند کریں