Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима * - Таржималар мундарижаси


Маънолар таржимаси Оят: (59) Сура: Нисо сураси
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَطِيعُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُواْ ٱلرَّسُولَ وَأُوْلِي ٱلۡأَمۡرِ مِنكُمۡۖ فَإِن تَنَٰزَعۡتُمۡ فِي شَيۡءٖ فَرُدُّوهُ إِلَى ٱللَّهِ وَٱلرَّسُولِ إِن كُنتُمۡ تُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۚ ذَٰلِكَ خَيۡرٞ وَأَحۡسَنُ تَأۡوِيلًا
E inu amene mwakhulupirira! Mumvereni Allah ndiponso mumvereni Mtumiki, ndi omwe ali ndi udindo pa inu. Ngati Mutatsutsana pa chinthu chilichonse, chibwezeni kwa Allah ndi Mtumiki Wake, ngatidi mukukhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro, kutero ndibwino; ndipo zotere zili ndi zotsatira zabwino.[131]
[131] Aliyense amene amdzoza utsogoleri nkofunika kuti anthu amumvere ngati iye akulamula zabwino. Pagulu la anthu ngati sipakhala mtsogoleri womumvera, ndiye kuti pamapezeka zisokonezo ndi ziwawa kotero kuti zinthu zawo siziyenda bwino. Chisilamu sichiloleza machitidwe achipolowe ndi ziwawa. Chisilamu chimakonda bata ndi mtendere ndi kuti pasapezeke anthu ena owachenjelera anzawo. Komatu atsogoleriwo awamvere akalamula mwa chilungamo popanda kulakwira Allah. Koma ngati akulakwira Allah asawamvere. Pamenepo atsate chomwe Allah wawalamula ndi Mtumiki Wake.
Арабча тафсирлар:
 
Маънолар таржимаси Оят: (59) Сура: Нисо сураси
Суралар мундарижаси Бет рақами
 
Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима - Таржималар мундарижаси

Қуръон Карим маъноларининг чевача таржимаси, мутаржим: Холид Иброҳим Бетала, 2020 йилда нашр қилинган

Ёпиш