《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (59) 章: 尼萨仪
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ أَطِيعُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُواْ ٱلرَّسُولَ وَأُوْلِي ٱلۡأَمۡرِ مِنكُمۡۖ فَإِن تَنَٰزَعۡتُمۡ فِي شَيۡءٖ فَرُدُّوهُ إِلَى ٱللَّهِ وَٱلرَّسُولِ إِن كُنتُمۡ تُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِۚ ذَٰلِكَ خَيۡرٞ وَأَحۡسَنُ تَأۡوِيلًا
E inu amene mwakhulupirira! Mumvereni Allah ndiponso mumvereni Mtumiki, ndi omwe ali ndi udindo pa inu. Ngati Mutatsutsana pa chinthu chilichonse, chibwezeni kwa Allah ndi Mtumiki Wake, ngatidi mukukhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro, kutero ndibwino; ndipo zotere zili ndi zotsatira zabwino.[131]
[131] Aliyense amene amdzoza utsogoleri nkofunika kuti anthu amumvere ngati iye akulamula zabwino. Pagulu la anthu ngati sipakhala mtsogoleri womumvera, ndiye kuti pamapezeka zisokonezo ndi ziwawa kotero kuti zinthu zawo siziyenda bwino. Chisilamu sichiloleza machitidwe achipolowe ndi ziwawa. Chisilamu chimakonda bata ndi mtendere ndi kuti pasapezeke anthu ena owachenjelera anzawo. Komatu atsogoleriwo awamvere akalamula mwa chilungamo popanda kulakwira Allah. Koma ngati akulakwira Allah asawamvere. Pamenepo atsate chomwe Allah wawalamula ndi Mtumiki Wake.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (59) 章: 尼萨仪
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭