Check out the new design

Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима * - Таржималар мундарижаси


Маънолар таржимаси Сура: Фуссилат   Оят:

Fussilat

حمٓ
Hâ-Mîm:
Арабча тафсирлар:
تَنزِيلٞ مِّنَ ٱلرَّحۡمَٰنِ ٱلرَّحِيمِ
(Qur’an iyi) ndichivumbulutso chochokera kwa (Allah) Wachifundo chambiri, Wachisoni chosatha.
Арабча тафсирлар:
كِتَٰبٞ فُصِّلَتۡ ءَايَٰتُهُۥ قُرۡءَانًا عَرَبِيّٗا لِّقَوۡمٖ يَعۡلَمُونَ
(Ili) ndi buku lomwe ma Ayah ake afotokozedwa (bwino pokhudza malamulo a zamdziko ndi tsiku lachimaliziro); chowerengedwa (chimene chavumbulutsidwa) m’chiyankhulo cha Chiarabu kwa anthu ozindikira (tsatanetsatane wa malamulo ake).
Арабча тафсирлар:
بَشِيرٗا وَنَذِيرٗا فَأَعۡرَضَ أَكۡثَرُهُمۡ فَهُمۡ لَا يَسۡمَعُونَ
Likunena nkhani yabwino (kwa ochita zabwino) ndi kuchenjeza (anthu ochita zoipa); koma ambiri a iwo (Aquraish) ainyoza kotero kuti sakumva; (kumva kothandizidwa nalo ndi kulilingalira).
Арабча тафсирлар:
وَقَالُواْ قُلُوبُنَا فِيٓ أَكِنَّةٖ مِّمَّا تَدۡعُونَآ إِلَيۡهِ وَفِيٓ ءَاذَانِنَا وَقۡرٞ وَمِنۢ بَيۡنِنَا وَبَيۡنِكَ حِجَابٞ فَٱعۡمَلۡ إِنَّنَا عَٰمِلُونَ
Ndipo akunena (kuti): “Mitima yathu (yaphimbidwa) m’zivindikiro, ku zomwe ukutiitanirazo, ndipo m’makutu mwathu muli kulemera kwa ugonthi; choncho pakati pathu ndi pakati pa iwe pali chotsekereza (chotchinga); tero chita (zakozo); nafe tichita (zathu; aliyense wa ife asalowelere za mnzake).”
Арабча тафсирлар:
قُلۡ إِنَّمَآ أَنَا۠ بَشَرٞ مِّثۡلُكُمۡ يُوحَىٰٓ إِلَيَّ أَنَّمَآ إِلَٰهُكُمۡ إِلَٰهٞ وَٰحِدٞ فَٱسۡتَقِيمُوٓاْ إِلَيۡهِ وَٱسۡتَغۡفِرُوهُۗ وَوَيۡلٞ لِّلۡمُشۡرِكِينَ
Nena: “Ndithu, ine ndi munthu monga inu; kukuvumbulutsidwa kwa ine (kuchokera kwa Allah) kuti ndithu Mulungu wanu ndi Mulungu Mmodzi; choncho lungamani kwa Iye ndipo mpempheni chikhululuko (pa zimene mwakhala mukumchimwira)” Ndipo kuonongeka kwakukulu kuli pa ophatikiza (Allah ndi zinthu zina).
Арабча тафсирлар:
ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡتُونَ ٱلزَّكَوٰةَ وَهُم بِٱلۡأٓخِرَةِ هُمۡ كَٰفِرُونَ
Amene sapereka chopereka (Zakaat), ndiomwe akukanira za tsiku lachimaliziro.
Арабча тафсирлар:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ لَهُمۡ أَجۡرٌ غَيۡرُ مَمۡنُونٖ
Ndithu amene akhulupirira ndi kumachita zabwino, pa iwo padzakhala malipiro osadukiza (osatha).
Арабча тафсирлар:
۞ قُلۡ أَئِنَّكُمۡ لَتَكۡفُرُونَ بِٱلَّذِي خَلَقَ ٱلۡأَرۡضَ فِي يَوۡمَيۡنِ وَتَجۡعَلُونَ لَهُۥٓ أَندَادٗاۚ ذَٰلِكَ رَبُّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Nena: “Kodi inu mukumkanira yemwe adalenga nthaka mmasiku awiri (okha)? Ndipo mukumpangira milungu (ina)? Iyeyo ndiye Mbuye wa zolengedwa zonse.”
Арабча тафсирлар:
وَجَعَلَ فِيهَا رَوَٰسِيَ مِن فَوۡقِهَا وَبَٰرَكَ فِيهَا وَقَدَّرَ فِيهَآ أَقۡوَٰتَهَا فِيٓ أَرۡبَعَةِ أَيَّامٖ سَوَآءٗ لِّلسَّآئِلِينَ
Ndipo adaika pamenepo mapiri ataliatali pamwamba pake, ndi kudalitsapo (ndi madzi, mmera, ndi ziweto), ndipo adayesa mmenemo zakudya zake (za okhala pa nthakapo; zimenezi adadzichita) mmasiku anayi; (izi) nzokwanira kwa ofunsa (zakalengedwe ka nthaka ndi zamkati mwake).
Арабча тафсирлар:
ثُمَّ ٱسۡتَوَىٰٓ إِلَى ٱلسَّمَآءِ وَهِيَ دُخَانٞ فَقَالَ لَهَا وَلِلۡأَرۡضِ ٱئۡتِيَا طَوۡعًا أَوۡ كَرۡهٗا قَالَتَآ أَتَيۡنَا طَآئِعِينَ
Kenako adalunjika ku thambo (malunjikidwe ogwirizana ndimomwe Iye alili mosafanana ndi zolengedwa zake), pomwe ilo (thambolo) lidali utsi. Ndipo adati kwa ilo ndi nthaka: “Idzani, mofuna kapena mokakamizidwa (tsatirani lamulo Langa).” Izo zidayankha kuti: “Tadza mofuna.”
Арабча тафсирлар:
 
Маънолар таржимаси Сура: Фуссилат
Суралар мундарижаси Бет рақами
 
Қуръони Карим маъноларининг таржимаси - Чевача таржима - Таржималар мундарижаси

Таржима қилган Халид Иброҳим Бетала.

Ёпиш