Check out the new design

Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - 齐切瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·白塔俩 * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Chương: Al-Kafirun   Câu:

Al-Kâfirun

قُلۡ يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡكَٰفِرُونَ
Nena (iwe Mtumiki) (s.a.w): E inu anthu osakhulupirira![493]
[493] (Ndime 1-6) Osakhulupilira a mu mzinda wa Makka pamene adaona kuti atopa, sangathe kuzimitsa dangalira la Usilamu ndipo adamuona Mneneri (s.a.w) tsiku lililonse akuonjezera khama pa ntchito yake, chipembedzo nacho chikunkerankera mtsogolo, adapempha Muhammad (s.a.w) kuti pakhale chimvano pakati pa iwo ndi iye choti amupembedze Mulungu wa Mneneri (s.a.w) chaka chimodzi pamodzi naye, nayenso pa chaka chinacho asakanikirane nawo popembedza milungu yawo chaka chimodzinso. Kumeneku ndiko kuti chaka, apembedze Mulungu wa Mneneri (s.a.w), nayenso apembedze milungu yawo chaka chinacho. Apa ndipo pamene idavumbulutsidwa Surayi. Cholinga chake ndi ichi: Inu muli ndi milungu yanu, inenso ndili ndi Mulungu wanga. Sizingatheke kusakanikirana pakati pa milungu yanu yonama ndi Mulungu wanga woona, ngakhalenso ndi mapemphero anu onama ndi mapemphero anga owona. Inu muli ndi chipembedzo ndichikhulupiliro chanu, inenso ndili ndi chipembedzo ndi chikhulupiliro changa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لَآ أَعۡبُدُ مَا تَعۡبُدُونَ
Sindipembedza chimene inu mukuchipembedza (kusiya Allah).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَآ أَنتُمۡ عَٰبِدُونَ مَآ أَعۡبُدُ
Inunso simumpembedza amene ine ndikumpembedza (yemwe ndi Allah).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَآ أَنَا۠ عَابِدٞ مَّا عَبَدتُّمۡ
Ndiponso ine sindidzapembedza chimene inu mwakhala mukuchipembedza (chifukwa inu ndinu ophatikiza Allah ndi zinthu zina).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَآ أَنتُمۡ عَٰبِدُونَ مَآ أَعۡبُدُ
Ndipo inu simudzampembedza amene ine ndikumpembedza (yemwe ndi Allah).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لَكُمۡ دِينُكُمۡ وَلِيَ دِينِ
Inu muli ndi chipembedzo chanu (chimene mukuchikhulupirira), inenso ndili ndi chipembedzo changa (chimene Allah wandisankhira).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Chương: Al-Kafirun
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - 齐切瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·白塔俩 - Mục lục các bản dịch

哈利德·伊布拉欣·白塔俩翻译

Đóng lại