Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Câu: (1) Chương: Chương Al-Masad

Chương Al-Masad

تَبَّتۡ يَدَآ أَبِي لَهَبٖ وَتَبَّ
Aonongeka manja a Abi Lahab (omwe adali kuwagwiritsa ntchito pozunza Asilamu). Nayenso wawonongeka.[497]
[497] (Ndime 1-4) Pa chiyambi cha uneneri wa Muhammad (s.a.w) adalamulidwa kuti aulalikire uthenga wabwinowo kwa abale ake apafupi; adawasonkhanitsa ndipo adawalalikira ndi kuwachenjeza za chilango cha tsiku lachimaliziro. Koma Abu Lahab adali m’bale watate wa Mtumiki Muhammad (s.a.w) adakwiya ndipo adanena kuti: “Waonongeka iwe! Waonongeka iwe! Chimenechi ndi chimene watisonkhanitsira?’’ Pa chifukwa ichi idavumbulutsidwa Sura imeneyi. Allah adamubwezera Abu Lahab pamodzi ndi mkazi wake, Ummu Jamil, mawu otembelera. Ummu Jamil ankalimbikira kwambiri kumuzunza Mtumiki (s.a.w) ndi kuwakaikitsa amuna kuti asamutsatire. Ndipo adayesetsa kutsekereza kuti asamutsatire. Ndipo adayesetsa kutsekereza kuti Chisilamu chisafalikire madera ena. “Aonongeka manja a Abu Lahab’’ kumeneku ndi kutembelera komutembelera Abu Lahab kuti aonongeke m’malo moonongeka Mneneri (s.a.w). Pakuti amene amatembelera apayu ndi Mwini Allah, ndiye kuti matembelero adamufikiradi iye.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Câu: (1) Chương: Chương Al-Masad
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại