Check out the new design

Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - 齐切瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·白塔俩 * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Chương: Al-Tawbah   Câu:
كَٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِكُمۡ كَانُوٓاْ أَشَدَّ مِنكُمۡ قُوَّةٗ وَأَكۡثَرَ أَمۡوَٰلٗا وَأَوۡلَٰدٗا فَٱسۡتَمۡتَعُواْ بِخَلَٰقِهِمۡ فَٱسۡتَمۡتَعۡتُم بِخَلَٰقِكُمۡ كَمَا ٱسۡتَمۡتَعَ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِكُم بِخَلَٰقِهِمۡ وَخُضۡتُمۡ كَٱلَّذِي خَاضُوٓاْۚ أُوْلَٰٓئِكَ حَبِطَتۡ أَعۡمَٰلُهُمۡ فِي ٱلدُّنۡيَا وَٱلۡأٓخِرَةِۖ وَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡخَٰسِرُونَ
(Inu osakhulupirira) ndinu ofanana ndi amene adalipo patsogolo panu. (Tikuonongani monga tidawaonongera iwo; koma) iwo adali ndi nyonga zambiri kuposa inu; adalinso ndi chuma chambiri ndi ana ambiri kuposa inu. Choncho, adasangalalira gawo lawo, inunso mukusangalalira gawo lanu monga momwe adasangalalira gawo lawo omwe adalipo patsogolo panu, ndipo mwamira m’zoipa monga momwe adamilira iwo. Awo ndi amene zochita zawo zidapita pachabe padziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro. Awo ndi omwe ali otaika (oluza).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَلَمۡ يَأۡتِهِمۡ نَبَأُ ٱلَّذِينَ مِن قَبۡلِهِمۡ قَوۡمِ نُوحٖ وَعَادٖ وَثَمُودَ وَقَوۡمِ إِبۡرَٰهِيمَ وَأَصۡحَٰبِ مَدۡيَنَ وَٱلۡمُؤۡتَفِكَٰتِۚ أَتَتۡهُمۡ رُسُلُهُم بِٱلۡبَيِّنَٰتِۖ فَمَا كَانَ ٱللَّهُ لِيَظۡلِمَهُمۡ وَلَٰكِن كَانُوٓاْ أَنفُسَهُمۡ يَظۡلِمُونَ
Kodi siidawadzere nkhani ya amene adalipo patsogolo pawo anthu a Nuh, Âdi ndi Samudu; anthu a Ibrahim ndi anthu a ku Madiyan ndi (anthu) a m’midzi imene idatembenuzidwa kumwamba kukhala pansi, pansi kukhala kumwamba? Atumiki awo adawadzera ndi zisonyezo zoonekera (koma adakana kuwatsata. Choncho, Allah adawaononga). Allah sadawachitire choipa, koma ankadzichitira okha zoipa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱلۡمُؤۡمِنُونَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتُ بَعۡضُهُمۡ أَوۡلِيَآءُ بَعۡضٖۚ يَأۡمُرُونَ بِٱلۡمَعۡرُوفِ وَيَنۡهَوۡنَ عَنِ ٱلۡمُنكَرِ وَيُقِيمُونَ ٱلصَّلَوٰةَ وَيُؤۡتُونَ ٱلزَّكَوٰةَ وَيُطِيعُونَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥٓۚ أُوْلَٰٓئِكَ سَيَرۡحَمُهُمُ ٱللَّهُۗ إِنَّ ٱللَّهَ عَزِيزٌ حَكِيمٞ
Okhulupirira aamuna ndi okhulupirira aakazi, ndiabwenzi omvana pakati pawo. Amalamula zabwino ndikuletsa zoipa ndipo amapemphera Swala ndi kupereka chopereka (zakaat), ndipo amamvera Allah ndi Mtumiki Wake. Awo ndi omwe Allah adzawachitira chifundo. Ndithu Allah Ngwamphamvu zoposa, Ngwanzeru zakuya.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَعَدَ ٱللَّهُ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتِ جَنَّٰتٖ تَجۡرِي مِن تَحۡتِهَا ٱلۡأَنۡهَٰرُ خَٰلِدِينَ فِيهَا وَمَسَٰكِنَ طَيِّبَةٗ فِي جَنَّٰتِ عَدۡنٖۚ وَرِضۡوَٰنٞ مِّنَ ٱللَّهِ أَكۡبَرُۚ ذَٰلِكَ هُوَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
Allah waalonjeza okhulupirira aamuna ndi okhulupirira aakazi Minda yomwe pansi (ndi patsogolo) pake mitsinje ikuyenda, adzakhala m’menemo nthawi yaitali. Ndi mokhala mwabwino m’Minda ya Edeni. Ndipo chiyanjo chochokera kwa Allah ndichachikulu (omwe ndi mtendere waukulu kwambiri kuposa zonse). Kumeneko ndiko kupambana zedi.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Chương: Al-Tawbah
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - 齐切瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·白塔俩 - Mục lục các bản dịch

哈利德·伊布拉欣·白塔俩翻译

Đóng lại