《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (174) 章: 拜格勒
إِنَّ ٱلَّذِينَ يَكۡتُمُونَ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ مِنَ ٱلۡكِتَٰبِ وَيَشۡتَرُونَ بِهِۦ ثَمَنٗا قَلِيلًا أُوْلَٰٓئِكَ مَا يَأۡكُلُونَ فِي بُطُونِهِمۡ إِلَّا ٱلنَّارَ وَلَا يُكَلِّمُهُمُ ٱللَّهُ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِ وَلَا يُزَكِّيهِمۡ وَلَهُمۡ عَذَابٌ أَلِيمٌ
Ndithudi, amene akubisa zomwe Allah adavumbulutsa m’buku (la Baibulo) m’malo mwake nasankha zinthu zamtengo wochepa, iwo sadya china mmimba mwawo koma moto basi; ndipo Allah sadzawayankhula tsiku lachimaliziro (mwachifundo koma mokwiya); ndipo sadzawayeretsa. Ndipo iwo adzapeza chilango chopweteka.[14]
[14] Ibunu Abbas adati ndime iyi ikufotokoza za atsogoleri a Chiyuda monga Kaabi bun Ashirafi ndi Maliki bun Swaifi ndi Huyaye bun Akhatwabi. Anthuwa adali kulandira mphatso zambiri zochokera kwa anthu awo owatsatira. Pamene Muhammad (s.a.w) adampatsa uneneri iwo sadakhulupirire chifukwa choopa kuti sapeza mitulo yochokera kwa anthu awo. Tero anabisa kwa anthu za uneneri wa Muhammad (s.a.w). Apa mpamene Allah adavumbulutsa Ayah (ndime) iyi, yakuti “Ndithudi, amene akubisa zomwe Allah adavumbulutsa m’buku (la Baibulo) m’malo mwake nasankha zinthu za mtengo wochepa iwo sadya china m’mimba mwawo koma moto basi.”
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (174) 章: 拜格勒
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭