《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (253) 章: 拜格勒
۞ تِلۡكَ ٱلرُّسُلُ فَضَّلۡنَا بَعۡضَهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖۘ مِّنۡهُم مَّن كَلَّمَ ٱللَّهُۖ وَرَفَعَ بَعۡضَهُمۡ دَرَجَٰتٖۚ وَءَاتَيۡنَا عِيسَى ٱبۡنَ مَرۡيَمَ ٱلۡبَيِّنَٰتِ وَأَيَّدۡنَٰهُ بِرُوحِ ٱلۡقُدُسِۗ وَلَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ مَا ٱقۡتَتَلَ ٱلَّذِينَ مِنۢ بَعۡدِهِم مِّنۢ بَعۡدِ مَا جَآءَتۡهُمُ ٱلۡبَيِّنَٰتُ وَلَٰكِنِ ٱخۡتَلَفُواْ فَمِنۡهُم مَّنۡ ءَامَنَ وَمِنۡهُم مَّن كَفَرَۚ وَلَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ مَا ٱقۡتَتَلُواْ وَلَٰكِنَّ ٱللَّهَ يَفۡعَلُ مَا يُرِيدُ
۞ Amenewo ndi aneneri tidawapatsa ulemelero mosiyanitsa pakati pawo, ena kuposa ena. Mwa iwo alipo amene Allah adawalankhula; ndipo ena adawakwezera kwambiri maulemelero awo. Naye Isa (Yesu) mwana wa Mariya tidampatsa zisonyezo zooneka, ndi kumlimbikitsa ndi Mzimu Woyera (rnngelo Gabriel). Allah akadafuna skadamenyana amene adalipo pambuyo pawo, (pa atumikiwo) pambuyo powadzera zizindikiro zooneka, koma adasiyana. Choncho mwa iwo alipo amene adakhulupirira, ndipo ena mwa iwo sadakhulupirire. Ndipo Allah akadafuna, sakadamenyana; koma Allah amachita zimene akufuna.[47]
[47] Ndime iyi ikusonyeza kuti atumiki maulemelero awo ngosiyanasiyana kwa Allah monga momwenso alili anthu ndi angelo ndi zinthu zinanso. Amaposana pakalandiridwe ka ulemelero wawo kwa Allah chifukwa chakusiyana zochita zawo. Zochita za ena nzazikulu zedi kapena zochuluka kwambiri kuposa zochita za anzawo. Ndipo apa Allah watchulapo atatu mwa atumiki akuluakulu omwe ndi:-
(a) Musa amene Allah adayankhula naye ndi kumpatsa zozizwitsa zoonekera.
(b) Ndi mneneri Isa (Yesu) yemwe adampatsa ulemelero waukulu
(c) ndi mneneri Muhammad (s.a.w). Enanso mwa aneneri akuluakulu pali mneneri Ibrahim ndi mneneri Nuh monga momwe ikufotokozera ndime ya chisanu ndi ziwiri (7) yam’surati Ahzab.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (253) 章: 拜格勒
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭