《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (268) 章: 拜格勒
ٱلشَّيۡطَٰنُ يَعِدُكُمُ ٱلۡفَقۡرَ وَيَأۡمُرُكُم بِٱلۡفَحۡشَآءِۖ وَٱللَّهُ يَعِدُكُم مَّغۡفِرَةٗ مِّنۡهُ وَفَضۡلٗاۗ وَٱللَّهُ وَٰسِعٌ عَلِيمٞ
Satana amakuopsezani ndi umphawi ndi kukulamulirani kuchita zoipa (monga umbombo), pomwe Allah akukulonjezani chikhululuko kuchokera kwa Iye ndi ubwino (waukulu ngati mupereka); ndipo Allah ali nazo zambiri, Ngodziwa.[54]
[54] (Ndime 268-271) apa Allah akuwalimbikitsa mtima amene akupereka kuti panthawi iliyonse pamene akupereka Allah adzawaonjezera. Ndipo akuwachenjeza kuti asamamvetsere udyerekezi wa satana umene amauthira m’mitima yawo powauza kuti: “Ngati mupereka, musauka.” Koma Allah akuwauza kuti: “Perekani simusauka. M’malomwake mupeza bwino pa dziko lapansi ndi pa tsiku lachimaliziro.”
M’ndime zomwezi Allah wafotokoza za (lonjezo) “naziri” kuti naziri iliyonse imene tikumlonjeza Allah akuidziwa.
Mawu oti “Naziri” nga Chiarabu. M’chichewa akuthandauza kuti, “ndikapeza chakuti ndidzachita chakutichakuti,” “kapena kuti, akachira m’bale wanga ndidzapereka chakutichakuti kwa Allah.”
Mawu anaziriwa siabwino pa malamulo a Chisilamu, ngakhale kuti anthu ambiri amakonda kuchita naziri poganizira kuti akatero Allah awayankha mwachangu namaganiziranso kuti naziri nchinthu chabwino m’Chisilamu pomwe chili chosafunika m’Chisilamu.
Kusafunika kwa naziri m’Chisilamu kuli kotere: Umati: “Allah akandichitira chakutichakuti inenso ndichita chakutichakuti.” Mawu oterewa sali mawu abwino ndiponso akusonyeza kupanda mwambo ndiponso akusonyeza umbombo.
Chifukwa chakuti munthu ofuna kupereka kanthu sanganene kuti: “Muyambe mwandichitira chakuti ndipo ndikupatsani.” Koma ngakhale zili choncho akwaniritsebe malonjezowo. Koma ngati malonjezowo ali pa chinthu choletsedwa asawakwaniritse, ndipo m’malo mwake apereke dipo.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (268) 章: 拜格勒
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭