《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (283) 章: 拜格勒
۞ وَإِن كُنتُمۡ عَلَىٰ سَفَرٖ وَلَمۡ تَجِدُواْ كَاتِبٗا فَرِهَٰنٞ مَّقۡبُوضَةٞۖ فَإِنۡ أَمِنَ بَعۡضُكُم بَعۡضٗا فَلۡيُؤَدِّ ٱلَّذِي ٱؤۡتُمِنَ أَمَٰنَتَهُۥ وَلۡيَتَّقِ ٱللَّهَ رَبَّهُۥۗ وَلَا تَكۡتُمُواْ ٱلشَّهَٰدَةَۚ وَمَن يَكۡتُمۡهَا فَإِنَّهُۥٓ ءَاثِمٞ قَلۡبُهُۥۗ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ عَلِيمٞ
Ndipo ngati muli pa ulendo, ndipo simudapeze mlembi, choncho (wokongoza) apatsidwe chikole (pinyolo) m’manja mwake. Ngati wina wasungitsa mmodzi wa inu chinthu (pomudalira wokhulupirika) choncho amene wayesedwa wokhulupirikayo abweze chinthucho kwa mwini wake, ndipo aope Allah, Mbuye wake. Ndipo musabise umboni (ngakhale uli wokuipirani). Ndipo amene abise ndiye kuti mu mtima mwake mwalowa uchimo; ndipo Allah akudziwa zonse zimene mukuchita.[58]
[58] Apa akunena kuti ngati anthu ali pamalo pomwe palibe wodziwa kulemba ndipo akukongozana, wokongozedwayo apereke chikole kwa wokongoza kuti achisunge wokongozayo. Ndipo adzabwezera akadzabweza ngongoleyo. Ngati atalephera kubweza ngongoleyo chikolecho chigulitsidwe ndi muweruzi nkumpatsa wokongozayo ndalama zolingana nzomwe adamkongoza. Zotsalira pa chinthu chogulitsidwacho azipereke kwa mwini chikolecho. Uwu ndiwo ubwino wachikole pa malamulo a Chisilamu. Akalephera kubweza ngongoleyo chinthucho chimagulitsidwa ndi boma ndikumpatsa mwini ngongoleyo choyenerana naye pomwe chotsaliracho amachipereka kwa mwini wake. Kwa amene wagwirizira chikolecho saloledwa kuchita nacho chilichonse. Ngati akuchita nacho ntchito nkumachidyelera ndiye kuti akuchita machitidwe akatapira omwe ali oletsedwa. Koma chinthucho angochisunga.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (283) 章: 拜格勒
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭