《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (285) 章: 拜格勒
ءَامَنَ ٱلرَّسُولُ بِمَآ أُنزِلَ إِلَيۡهِ مِن رَّبِّهِۦ وَٱلۡمُؤۡمِنُونَۚ كُلٌّ ءَامَنَ بِٱللَّهِ وَمَلَٰٓئِكَتِهِۦ وَكُتُبِهِۦ وَرُسُلِهِۦ لَا نُفَرِّقُ بَيۡنَ أَحَدٖ مِّن رُّسُلِهِۦۚ وَقَالُواْ سَمِعۡنَا وَأَطَعۡنَاۖ غُفۡرَانَكَ رَبَّنَا وَإِلَيۡكَ ٱلۡمَصِيرُ
Mtumiki wakhulupirira zimene zavumbulutsidwa kwa iye kuchokera kwa Mbuye wake. Naonso asilamu (akhulupirira). Onse akhulupirira Allah, angelo Ake, mabuku Ake ndi atumiki Ake. (Iwo pamodzi ndi Mtumiki wawoyo akunena kuti): “Sitingalekanitse aliyense pakati pa atumiki Ake, (onse tikuwakhulupirira).” Ndipo akunena: “Tamva ndiponso tamvera, (choncho tikukupemphani) chikhululuko chanu. E Mbuye wathu! Ndipo kwa Inu nkobwerera.”[59]
[59] (Ndime 285-286) ndime ziwirizi zili ndi ubwino ndi madalitso ambiri monga momwe ilili ndime ya Ayatu Kursii yanambala 255 m’sura yomweyi.
Akutilangiza kuziwerenga ndimezi m’malo monse momwe Ayatu Kursii imawerengedwa. Qur’an yonse ikuphunzitsa asilamu kuti asasiyanitse pakati pa aneneri. Koma awavomereze onse ndi kuwakhulupilira amene adadza patsogolo pa Mtumiki Muhammad (s.a.w). Mtumiki Muhammad (s.a.w) ndiye womaliza mwa aneneriwo. Ndipo amadziwika ndi dzina lakuti “Khatamu nNabiyyina’’ “womaliza mwa Aneneri.” Ndipo amene sakhulupilira kuti Muhammad (s.a.w) ngomaliza mwa aneneri nakhulupilira munthu wamba yemwe akungodzinamiza kuti iye ndi mneneri, monga momwe chikhulupiliro cha Akadiyani chilili ndiye kuti iyeyo watuluka m’Chisilamu ndipo ndi munthu wakunja.
Asilamu sakana mneneri aliyense mwa Aneneri omwe adalipo Mtumiki Muhammad (s.a.w) asanadze. Koma iwo amakhulupilira kuti malamulo akayendetsedwe ka zipembedzo zawo kadafafanizidwa chifukwa chakudza kwa mtumiki Muhammad (s.a.w). Nyengo ino ndinyengo yotsatira mtumiki Muhammad (s.a.w) pazochitachita. Koma pazinthu zokhudza chikhulupiliro, Aneneri onse adadza ndi lamulo limodzi monga momwe Allah akufotokozera m’ndime ya 13, Sûrat Shura.
Ndipo m’ndime zimenezi za 285 ndi 286 zikuphunzitsanso miyambo ya Chisilamu ndi mapemphero (maduwa) momwe tingampemphere Allah. Ndimezi zikufotokoza za chisomo cha Allah chomwe chili pa ife anthu Ake kuti Allah sakakamiza koma chimene angathe kuchichita akapolo Ake. Ndiponso sawalanga ngati atachita zinthu molakwitsa kapena moiwala.
Ndime ziwirizi zikusonyeza makhalidwe a Asilamu ndi zinthu zawo zimene amazikhulupilira.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (285) 章: 拜格勒
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭