《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (12) 章: 阿里欧姆拉尼
قُل لِّلَّذِينَ كَفَرُواْ سَتُغۡلَبُونَ وَتُحۡشَرُونَ إِلَىٰ جَهَنَّمَۖ وَبِئۡسَ ٱلۡمِهَادُ
Auze amene sadakhulupirire: “Posachedwapa mugonjetsedwa ndi kusonkhanitsidwa ndi kuponyedwa ku Moto. Taonani kuipa kwa malo wokakhazikikamo!”[62]
[62] Mawu adalandiridwa kuchokera kwa Saîd bun Jubair omwe iye adawalandiranso kuchokera kwa Ikrima pomwe nayenso Ikrima adawalandira kuchokera kwa Ibn Abbas (Allah asangalale nawo onse). Iye adati: “Ndithudi, Mtumiki (s.a.w) pamene adagonjetsa Aquraishi pa nkhondo ya Badri nabwerera ku Madina, adawasonkhanitsa Ayuda mu msika wa Bani Qainuqaa’ nawachenjeza kuti chingawapeze chomwe chidawapeza Aquraish. Iwo adati: “Usanyengedwe ndizimenezo. Ndithudi, iwe unakumana ndi mbuli za anthu zomwe sizidziwa kamenyedwe ka nkhondo. Ndipo nchifukwa chake wawagonjetsa. Ukadamenyana ndi ife ukadadziwa kuti ife ndife anthu.”
Pachifukwa ichi idavumbulutsidwa Ayah (ndime) yakuti: “Nena (kwa iwo iwe Muhammad {s.a.w}): “Inu Ayuda mugonjetsedwa posachedwapa pompano pa dziko lapansi. Chuma chanu ndi ana anu zisakunyengeni. Kupambana sikuli pa chifukwa cha kuchuluka kwanu, koma kuli m’manja mwa Allah Woyera.”
Mawuwa adatsimikizika powapha a Bani Nadhir ndi kugonjetsa mzinda wa Khaibar.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (12) 章: 阿里欧姆拉尼
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭