Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 艾哈拉布   段:
يَسۡـَٔلُكَ ٱلنَّاسُ عَنِ ٱلسَّاعَةِۖ قُلۡ إِنَّمَا عِلۡمُهَا عِندَ ٱللَّهِۚ وَمَا يُدۡرِيكَ لَعَلَّ ٱلسَّاعَةَ تَكُونُ قَرِيبًا
Anthu akukufunsa za (kudza kwa) nthawi (ya tsiku la chitsiriziro). Nena: “Kuzindikira kwa nthawiyo kuli ndi Allah (Yekha). Nanga nchiyani chikudziwitse kuti nthawi ya chimaliziro iri pafupi?”
阿拉伯语经注:
إِنَّ ٱللَّهَ لَعَنَ ٱلۡكَٰفِرِينَ وَأَعَدَّ لَهُمۡ سَعِيرًا
Ndithu Allah wawatembelera osakhulupirira ndi kuwakonzera Moto woyaka kwambiri.
阿拉伯语经注:
خَٰلِدِينَ فِيهَآ أَبَدٗاۖ لَّا يَجِدُونَ وَلِيّٗا وَلَا نَصِيرٗا
Adzakhala nrmenemo nthawi yaitali. Sadzapeza bwenzi ngakhale mthandizi.
阿拉伯语经注:
يَوۡمَ تُقَلَّبُ وُجُوهُهُمۡ فِي ٱلنَّارِ يَقُولُونَ يَٰلَيۡتَنَآ أَطَعۡنَا ٱللَّهَ وَأَطَعۡنَا ٱلرَّسُولَا۠
Tsiku limene nkhope zawo zikatembenuzidwa ku Moto (zikutenthedwa), uku akunena: “Kalanga ife! Tikadamumvera Allah ndi kumveranso Mtumiki (s.a.w), (sibwenzi tili m’chilangomu).”
阿拉伯语经注:
وَقَالُواْ رَبَّنَآ إِنَّآ أَطَعۡنَا سَادَتَنَا وَكُبَرَآءَنَا فَأَضَلُّونَا ٱلسَّبِيلَا۠
Ndipo adzanena: “E Mbuye wathu! Ndithu ife tidamvera olemekezeka athu ndi akuluakulu athu, choncho adatisokeza njira.”
阿拉伯语经注:
رَبَّنَآ ءَاتِهِمۡ ضِعۡفَيۡنِ مِنَ ٱلۡعَذَابِ وَٱلۡعَنۡهُمۡ لَعۡنٗا كَبِيرٗا
Mbuye wathu! Apatseni chilango pamwamba pa chilango ndipo atembelereni, kutembelera kwakukulu.”
阿拉伯语经注:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَكُونُواْ كَٱلَّذِينَ ءَاذَوۡاْ مُوسَىٰ فَبَرَّأَهُ ٱللَّهُ مِمَّا قَالُواْۚ وَكَانَ عِندَ ٱللَّهِ وَجِيهٗا
E inu amene mwakhulupirira! Musakhale monga amene adamvutitsa Mûsa; koma Allah adamuyeretsa kuzimene ankamnenera. Ndipo iye kwa Allah adali wolemekezeka.[331]
[331] M’ndime iyi, Allah akulangiza Asilamu kuti asamuvutitse Mtumiki ndi kumnenera mawu opanda ulemu monga momwe Ayuda ankamunenera Musa. Ana a Israeli adamunamizira Musa kuti ali ndi khate pathupi lake, kapena kuti ali ndi matenda a mwera (phudzi). Koma Allah adamuyeretsa kuzomwe adali kumunamizirazo. Adamuyeretsa motere monga momwe Bukhari akunenera muhadisi yomwe idalandiridwa kuchokera kwa Abu Huraira (r.a) kuti Mtumiki (s.a.w) adati: Musa adali munthu wamanyazi, ndipo amabisa thupi lake. Khungu lake silimaoneka chifukwa cha manyazi ake. Ndipo adamuvutitsa ena mwa ana a Israeli. Adati: “Sangadzibise motere koma pa khungu lake pali chochititsa manyazi, mwina khate kapena matenda amphepo yamwera (phudzi), kapena matenda ena aliwonse!” Ndipo Allah adafuna kumuyeretsa ku zimene ankamunamizirazo. Tsiku lina Musa adakhala payekha navula nsalu zake naika pa mwala. Kenako adayamba kusamba. Pamene adamaliza kusamba adacheukira komwe adaika nsalu zake kuti azitenge. Adaona mwala ukuthawitsa nsalu zake. Musa adatenga ndodo yake nkumathamangira mwalawo uku akunena: “Nsalu zanga, iwe mwala! Nsalu zanga iwe mwala!’’ Mpaka adadutsa pomwe adakhala akuluakulu a ana a Israeli namuona thupi lake lili losalala kwabasi; lopanda chilema chilichonse. Potero Allah adamuyeretsa ku zomwe ankamunenerazo.
阿拉伯语经注:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَقُولُواْ قَوۡلٗا سَدِيدٗا
E inu amene mwakhulupirira! Opani Allah (pokwaniritsa malamulo Ake, ndi kusiya zoletsedwa), ndipo nenani mawu olungama.
阿拉伯语经注:
يُصۡلِحۡ لَكُمۡ أَعۡمَٰلَكُمۡ وَيَغۡفِرۡ لَكُمۡ ذُنُوبَكُمۡۗ وَمَن يُطِعِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ فَقَدۡ فَازَ فَوۡزًا عَظِيمًا
Akukonzerani bwino zochita zanu ndi kukukhululukirani machimo anu. ndipo amene akumvera Allah ndi Mtumiki Wake, ndithu apambana; kupambana kwakukulu.
阿拉伯语经注:
إِنَّا عَرَضۡنَا ٱلۡأَمَانَةَ عَلَى ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَٱلۡجِبَالِ فَأَبَيۡنَ أَن يَحۡمِلۡنَهَا وَأَشۡفَقۡنَ مِنۡهَا وَحَمَلَهَا ٱلۡإِنسَٰنُۖ إِنَّهُۥ كَانَ ظَلُومٗا جَهُولٗا
Ndithu Ife tidapereka udindo (otsatira malamulo) ku thambo ndi nthaka ndi mapiri; koma zidakana kuwusenza (udindowo); ndipo zidauopa. Koma munthu adawusenza; ndithu iye ngwachinyengo kwambiri ndiponso mbuli.
阿拉伯语经注:
لِّيُعَذِّبَ ٱللَّهُ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ وَٱلۡمُنَٰفِقَٰتِ وَٱلۡمُشۡرِكِينَ وَٱلۡمُشۡرِكَٰتِ وَيَتُوبَ ٱللَّهُ عَلَى ٱلۡمُؤۡمِنِينَ وَٱلۡمُؤۡمِنَٰتِۗ وَكَانَ ٱللَّهُ غَفُورٗا رَّحِيمَۢا
Kuti Allah adzawalange achiphamaso aamuna ndi aakazi, ndi opembedza mafano achimuna ndi achikazi ndi kuti adzawakhululukire okhulupirira achimuna ndi achikazi. Ndipo Allah Ngokhululuka kwabasi, Ngwachisoni chosatha.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 艾哈拉布
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭