《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (1) 章: 尼萨仪

尼萨仪

يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ ٱتَّقُواْ رَبَّكُمُ ٱلَّذِي خَلَقَكُم مِّن نَّفۡسٖ وَٰحِدَةٖ وَخَلَقَ مِنۡهَا زَوۡجَهَا وَبَثَّ مِنۡهُمَا رِجَالٗا كَثِيرٗا وَنِسَآءٗۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ ٱلَّذِي تَسَآءَلُونَ بِهِۦ وَٱلۡأَرۡحَامَۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلَيۡكُمۡ رَقِيبٗا
E inu anthu! Opani Mbuye wanu yemwe adakulengani kuchokera mwa munthu mmodzi (Adam) ndipo adalenga mmenemo mkazi wake (Hawa), ndipo adafalitsa amuna ndi akazi ambiri kuchokera mwa awiriwo. Ndipo opani Allah yemwe kupyolera mwa Iye mumapemphana. Ndipo (sungani) chibale. Ndithudi Allah Ndimyang’aniri pa inu (akuona chilichonse chimene muchita).[105]
[105] Ndime iyi ikulimbikitsa za kuopa Allah ndi kumulemekeza potsatira malamulo ake ndi kupewa zomwe Iye waletsa. Iye ndi amene adakulenga. Ndiyemwenso adalenga zonse zimene iwe adakulengera. Ngakhale iwe amene utafuna chithandizo kwa anzako umampempha ponena kuti: ‘‘Ndikukupempha m’dzina la Allah kuti undichitire chakuti.” Izi umachita poona kuti iye adzalemekeza dzina la Allah, ndipo adzakwaniritsa chomwe ukufunacho. Koma nanga bwanji ukuchita zimene Allah waletsa? Bwanji sukulemekeza lamulo lake pomwe iwe ukufuna kuti anthu achite zomwe sukuchita. Apa akutiuzanso kuti Allah akuona chilichonse chimene anthu ake akuchita, ngakhale chikhale chochepa chotani.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (1) 章: 尼萨仪
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭