《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (65) 章: 尼萨仪
فَلَا وَرَبِّكَ لَا يُؤۡمِنُونَ حَتَّىٰ يُحَكِّمُوكَ فِيمَا شَجَرَ بَيۡنَهُمۡ ثُمَّ لَا يَجِدُواْ فِيٓ أَنفُسِهِمۡ حَرَجٗا مِّمَّا قَضَيۡتَ وَيُسَلِّمُواْ تَسۡلِيمٗا
Ndikulumbira (m’choonadi cha) Mbuye wako, iwo sangakhale okhulupirira moona pokhapokha akuyese muweruzi wawo pa zomwe akukangana pakati pawo. Kenako asaone vuto m’mitima yawo pa zomwe waweruza, ndipo adzipereke kwathunthu (pogonjera chiweruzo chako).[132]
[132] Ngati anthu atakangana pachinthu ena nati chimenechi nchofunika pomwe ena akuti nchosafunika, onsewo abwere nkuyang’ana kuti mawu a Allah ndi mawu a Mtumiki akunena chiyani pachinthu choterecho. Tsono akapeza malangizo a Allah ndi Mtumiki pachimenecho awatsatire. Aliyense wa iwo asakhumudwe poona kuti zomwe amalimbikira sindizo zomwe Mtumiki (s.a.w) adaphunzitsa. Koma agonjere kwathunthu kuzophunzitsa za Mtumikizo. Chilichonse chimene Mtumiki walangiza asawiringule nacho. Koma angotsatira basi.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (65) 章: 尼萨仪
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭