Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 安法里   段:
وَٱذۡكُرُوٓاْ إِذۡ أَنتُمۡ قَلِيلٞ مُّسۡتَضۡعَفُونَ فِي ٱلۡأَرۡضِ تَخَافُونَ أَن يَتَخَطَّفَكُمُ ٱلنَّاسُ فَـَٔاوَىٰكُمۡ وَأَيَّدَكُم بِنَصۡرِهِۦ وَرَزَقَكُم مِّنَ ٱلطَّيِّبَٰتِ لَعَلَّكُمۡ تَشۡكُرُونَ
Ndipo kumbukirani (inu Asilamu) pamene mudali owerengeka, ochepa, onyozeka m’dziko. Mumakhala moopa anthu kuti angakufwambeni, koma anakupatsani pamalo pabwino pokhala, nakulimbikitsani ndi chipulumutso Chake, nakuninkhani zinthu zabwino kuti muyamike (Allah).[197]
[197] Anthu akakhala mu mtendere nkofunika kumakumbukira za nthawi yomwe adali m’masautso kuti amuyamike Allah pa mtendere umene wawapatsawo ndi kupewa machimo chifukwa chakuti palibe chomwe chimachotsa mtendere choposa machimo ndikusamuyamika mwini mtenderewo.
阿拉伯语经注:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ لَا تَخُونُواْ ٱللَّهَ وَٱلرَّسُولَ وَتَخُونُوٓاْ أَمَٰنَٰتِكُمۡ وَأَنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Musachitire Allah ndi Mtumiki (Wake) chinyengo (pa kutsata zimene mwaletsedwa). Ndipo musazichitire chinyengo zimene mwakhulupirika nazo uku mukudziwa (kuti kutero ndikulakwa).
阿拉伯语经注:
وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّمَآ أَمۡوَٰلُكُمۡ وَأَوۡلَٰدُكُمۡ فِتۡنَةٞ وَأَنَّ ٱللَّهَ عِندَهُۥٓ أَجۡرٌ عَظِيمٞ
Ndipo dziwani kuti chuma chanu ndi ana anu ndimayesero (oyesedwa ndi Allah kuti aone mmene mungagwiritsire nazo ntchito). Ndi kuti kwa Allah kuli malipiro aakulu.
阿拉伯语经注:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِن تَتَّقُواْ ٱللَّهَ يَجۡعَل لَّكُمۡ فُرۡقَانٗا وَيُكَفِّرۡ عَنكُمۡ سَيِّـَٔاتِكُمۡ وَيَغۡفِرۡ لَكُمۡۗ وَٱللَّهُ ذُو ٱلۡفَضۡلِ ٱلۡعَظِيمِ
E inu amene mwakhulupirira! Ngati muopa Allah, adzakupatsani chilekanitso (cholekanitsa pakati pa choonadi ndi chachabe), ndiponso akufafanizirani zoipa zanu ndi kukukhululukirani. Ndipo Allah ndi Mwini ubwino waukulu.[198]
[198] Munthu ngati akuopa Allah moona mtima, ndiye kuti Allah amutsekulira makomo amadalitso pano pa dziko lapansi ndi pa tsiku la chimaliziro.
阿拉伯语经注:
وَإِذۡ يَمۡكُرُ بِكَ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لِيُثۡبِتُوكَ أَوۡ يَقۡتُلُوكَ أَوۡ يُخۡرِجُوكَۚ وَيَمۡكُرُونَ وَيَمۡكُرُ ٱللَّهُۖ وَٱللَّهُ خَيۡرُ ٱلۡمَٰكِرِينَ
Ndipo (kumbukira) pamene omwe sadakhulupirire amakuchitira chiwembu kuti akunjate, kapena akuphe, kapena akutulutse (m’dziko lawo la Makka mwachipongwe). Ndipo amachita chiwembu, naye Allah anawononga chiwembu chawocho. Ndipo Allah ndiwokhoza koposa poononga ziwembu (za anthu oipa).[199]
[199] Apa pakutchulidwa ziwembu za Aquraish zomwe adamchitira Mtumiki (s.a.w) asanasamuke ku Makka. Iwo adasonkhana m’nyumba yochitiramo upo nayamba kukambirana za chomwe angachite naye Mneneri Muhammad, chimene chingamuonongeretu. Ena anapereka maganizo akuti akamponye m’ndende konko ku Makka popanda kumpatsa chakudya. Kapena ampatse chakudya chochepa kwambiri kufikira afe ndi njala. Ndipo ena adati koma amtseke maso ndi milomo ndi kumnjata goli m’manja kenako kumkweza pa ngamira nkukamtaya kuchipululu chamchenga kuti akafere konko.
Ena amapereka ganizo oti asankhe anyamata ochokera m’mafuko amfulu kuti onse pamodzi akammenye ndi kumupha. Ganizoli ndi lomwe anavomerezana. Koma usiku omwe adapangana kuti amuphe, ndi umene Mtumiki (s.a.w) adasamuka kunka ku Madina. potero adalephera kumupha.
阿拉伯语经注:
وَإِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِمۡ ءَايَٰتُنَا قَالُواْ قَدۡ سَمِعۡنَا لَوۡ نَشَآءُ لَقُلۡنَا مِثۡلَ هَٰذَآ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّآ أَسَٰطِيرُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Ndipo (Aquraish) zikawerengedwa Ayah (ndime) Zathu kwa iwo amanena: “Tidazimva (izi kale). Tikadafuna tikadanena zonga izi. Izi sikanthu koma ndinthano za anthu akale.”
阿拉伯语经注:
وَإِذۡ قَالُواْ ٱللَّهُمَّ إِن كَانَ هَٰذَا هُوَ ٱلۡحَقَّ مِنۡ عِندِكَ فَأَمۡطِرۡ عَلَيۡنَا حِجَارَةٗ مِّنَ ٱلسَّمَآءِ أَوِ ٱئۡتِنَا بِعَذَابٍ أَلِيمٖ
Ndipo (kumbukira) pamene adati: “E Inu Allah! Ngati ichi (chimene wadza nacho Muhammad {s.a.w}) chili choonadi chochokera kwa Inu, tivumbwitsireni mvula ya miyala yochokera kumwamba, kapena mutibweretsere chilango chowawa kwambiri.”[200]
[200] Ayah iyi ikusonyeza kuti sadali kuchifuna choonadi, chilungamo ndi zabwino zomwe adadza nazo Mneneri Muhammad (s.a.w).
阿拉伯语经注:
وَمَا كَانَ ٱللَّهُ لِيُعَذِّبَهُمۡ وَأَنتَ فِيهِمۡۚ وَمَا كَانَ ٱللَّهُ مُعَذِّبَهُمۡ وَهُمۡ يَسۡتَغۡفِرُونَ
Koma Allah sangawalange pomwe iwe uli nawo. Ndipo Allah sakadawalanga pomwe (ena mwa iwo) akupempha chikhululuko.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 安法里
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭