《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (117) 章: 讨拜
لَّقَد تَّابَ ٱللَّهُ عَلَى ٱلنَّبِيِّ وَٱلۡمُهَٰجِرِينَ وَٱلۡأَنصَارِ ٱلَّذِينَ ٱتَّبَعُوهُ فِي سَاعَةِ ٱلۡعُسۡرَةِ مِنۢ بَعۡدِ مَا كَادَ يَزِيغُ قُلُوبُ فَرِيقٖ مِّنۡهُمۡ ثُمَّ تَابَ عَلَيۡهِمۡۚ إِنَّهُۥ بِهِمۡ رَءُوفٞ رَّحِيمٞ
Ndithu Allah wafunira zabwino Mtumiki Wake ndi Amuhajirina ndi Answari amene adamtsatira iye (Muhammad {s.a.w}) m’nthawi yamasautso (pokamenyana ndi Aroma pankhondo ya Tabuk), nthawi yomwe mitima ya ena a iwo idatsala pang’ono kupotoka (kutsata machitidwe achikafiri); kenako Allah adawatembenukira ndi chifundo. Ndithu Iye (Allah) kwa iwo Ngodekha, Ngwachisoni chosatha.[213]
[213] Nkhondo ya Tabuk idachitika m’mwezi wa Rajab m’chaka cha chisanu nchinayi chakusamuka. Idali pakati pa Asilamu ndi Aroma. Gulu lankhondo la Chisilamu lomwe lidapita kunkhondo linkatchedwa “Gulu la Masautso” chifukwa kukonzekera kwa nkhondoyi kudachitika m’nyengo ya masautso kwa anthu. Ndipo pamene Mtumiki adafika ku Tabuk, adadza msogoleri wa gulu lankhondo la Aroma wotchedwa Yohane namvana kuti pasakhale nkhondo. M’malo mwake iye adzapereka “Jiziya” (msonkho), motero Mtumiki adabwerera ku Madina. lyi idali nkhondo yake yomaliza.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (117) 章: 讨拜
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭