《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (4) 章: 则里扎莱
يَوۡمَئِذٖ تُحَدِّثُ أَخۡبَارَهَا
Tsiku limenelo idzanena nkhani zake zonse, (zabwino kapena zoipa).[470]
[470] Idzanena nthaka pa tsiku limenelo pamene Allah adzaiuza kuti inene monga momwe amazinenetsera zinthu zimene chikhalire sizilankhula, pakuti Allah ndi Wamphamvu zonse. Kapena m’mene iti idzakhalire nthaka kudzakwanira munthu kudziwa kuti ikutanthauza chakuti, popanda kutulutsa mawu monga momwe timadziwira munthu wosangalala ndi wachisoni; wanjala ndi wokhuta popanda kuyankhula. Nkhani zomwe idzafotokoza nthaka pa tsiku limenelo, monga momwe adanenera Mneneri Muhammad (s.a.w), ndi izi:- Tsiku la chiweruziro nthaka idzamuikira umboni munthu aliyense kapena m’badwo uliwonse pa chimene adachita pamwamba pake (pamwamba pa nthaka). Limeneli ndilo tanthauzo la mawu aja oti “ Nthaka idzanena nkhani zake.”
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (4) 章: 则里扎莱
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭