የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: ሱረቱ አስ ሷፋት   አንቀጽ:

ሱረቱ አስ ሷፋት

وَٱلصَّٰٓفَّٰتِ صَفّٗا
Ndikulumbira (angelo) amene amandanda m’mizere yondondozana, (popembedza ndi kugonjera Mbuye wawo).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱلزَّٰجِرَٰتِ زَجۡرٗا
Ndi omwe amaletsa zoipa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱلتَّٰلِيَٰتِ ذِكۡرًا
Ndi omwe amalalika ulaliki (wa Allah ndi kumtamanda mochulukira).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّ إِلَٰهَكُمۡ لَوَٰحِدٞ
Ndithu Mulungu wanu ndi mmodzi basi.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
رَّبُّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَا وَرَبُّ ٱلۡمَشَٰرِقِ
Mbuye wathambo ndi nthaka, ndi zapakati pake; ndiponso Mbuye wa kuvuma konse.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّا زَيَّنَّا ٱلسَّمَآءَ ٱلدُّنۡيَا بِزِينَةٍ ٱلۡكَوَاكِبِ
Ndithu tidalikongoletsa thambo lapafupi (ndi inu) ndi chokongoletsa cha nyenyezi (zowala).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَحِفۡظٗا مِّن كُلِّ شَيۡطَٰنٖ مَّارِدٖ
Ndi kuti lisungidwe ku satana aliyense wogalukira (lamulo la Allah).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
لَّا يَسَّمَّعُونَ إِلَى ٱلۡمَلَإِ ٱلۡأَعۡلَىٰ وَيُقۡذَفُونَ مِن كُلِّ جَانِبٖ
Kuti asamvere (zomwe zikunenedwa ndi) gulu lolemekezeka (la angelo). Ndipo akugendedwa (ndi kupirikitsidwa) mbali zonse.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
دُحُورٗاۖ وَلَهُمۡ عَذَابٞ وَاصِبٌ
Kuthamangitsidwa mwamphamvu; ndipo chilango chonkerankera patsogolo chili pa iwo.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِلَّا مَنۡ خَطِفَ ٱلۡخَطۡفَةَ فَأَتۡبَعَهُۥ شِهَابٞ ثَاقِبٞ
Kupatula amene wazembetsa mawu (akumwamba), ndipo chikumtsatira iye chenje cha moto chowala kwambiri.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱسۡتَفۡتِهِمۡ أَهُمۡ أَشَدُّ خَلۡقًا أَم مَّنۡ خَلَقۡنَآۚ إِنَّا خَلَقۡنَٰهُم مِّن طِينٖ لَّازِبِۭ
Tawafunsa (otsutsa zouka ku imfa): “Kodi iwo ngovuta kuwalenga kuposa zimene tidalenga, (monga: thambo, nthaka, nyenyezi ndi zina zotere)?” Ndithu Ife tidawalenga kuchokera ku dongo lonyata.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
بَلۡ عَجِبۡتَ وَيَسۡخَرُونَ
Koma iwe (Mneneri) ukudabwa (za kutsutsa kwawo kuuka ku imfa pomwe zisonyezo zilipo zambirimbiri), ndipo akukuchitira chipongwe (kudabwa kwako).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِذَا ذُكِّرُواْ لَا يَذۡكُرُونَ
Ndipo akalalikiridwa, salalikirika.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِذَا رَأَوۡاْ ءَايَةٗ يَسۡتَسۡخِرُونَ
Ndipo akachiona chisonyezo (chosonyeza kukhoza kwa Allah,) amachichitira chipongwe.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَقَالُوٓاْ إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا سِحۡرٞ مُّبِينٌ
Ndipo osakhulupirira amanena: “Palibe chilipo apa, koma ndi matsenga woonekera poyera.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَءِذَا مِتۡنَا وَكُنَّا تُرَابٗا وَعِظَٰمًا أَءِنَّا لَمَبۡعُوثُونَ
“Kodi tikadzafa ndi kusanduka fumbi ndi mafupa, tidzatulutsidwanso (kuchokera m’manda tili amoyo)?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَوَءَابَآؤُنَا ٱلۡأَوَّلُونَ
“Pamodzi ndi makolo athu akale?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
قُلۡ نَعَمۡ وَأَنتُمۡ دَٰخِرُونَ
Nena (iwe Mneneri): “Inde (mudzaukitsidwa inu pamodzi ndi makolo anu) uku inu muli onyozeka.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَإِنَّمَا هِيَ زَجۡرَةٞ وَٰحِدَةٞ فَإِذَا هُمۡ يَنظُرُونَ
Ndithu (kuukako) ndimkuwe umodzi adzangodzidzimuka ali moyo, akuyang’ana.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَقَالُواْ يَٰوَيۡلَنَا هَٰذَا يَوۡمُ ٱلدِّينِ
Ndipo adzanena (okanawo): “Kalanga ife! Kuonongeka nkwathu! Ili nditsiku lija lamalipiro!”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
هَٰذَا يَوۡمُ ٱلۡفَصۡلِ ٱلَّذِي كُنتُم بِهِۦ تُكَذِّبُونَ
(Adzawauza): “Ili nditsiku la chiweruziro lomwe mumalitsutsa lija.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
۞ ٱحۡشُرُواْ ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْ وَأَزۡوَٰجَهُمۡ وَمَا كَانُواْ يَعۡبُدُونَ
(Kudzanenedwa kwa angelo): “Asonkhanitseni amene adali osalungama pamodzi ndi akazi awo (okana Allah) ndi milungu yawo imene amaipembedza,”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
مِن دُونِ ٱللَّهِ فَٱهۡدُوهُمۡ إِلَىٰ صِرَٰطِ ٱلۡجَحِيمِ
“Kusiya Allah, ndipo asonyezeni njira ya ku Jahannam.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَقِفُوهُمۡۖ إِنَّهُم مَّسۡـُٔولُونَ
“Koma aimikeni pano chifukwa iwo afunsidwa (za chikhulupiliro chawo ndi zochita zawo):”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
مَا لَكُمۡ لَا تَنَاصَرُونَ
“Kodi nchifukwa ninji inu (opembedza mafano) simukupulumutsana (monga mumanenera pa dziko lapansi kuti mudzapulumutsana)?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
بَلۡ هُمُ ٱلۡيَوۡمَ مُسۡتَسۡلِمُونَ
Koma iwo pa tsikulo adzagonjera ndi kudzipereka (ku lamulo la Allah).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَأَقۡبَلَ بَعۡضُهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖ يَتَسَآءَلُونَ
Ndipo adzatembenukirana ndi kuyamba kufunsana (ndi kudzudzulana).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
قَالُوٓاْ إِنَّكُمۡ كُنتُمۡ تَأۡتُونَنَا عَنِ ٱلۡيَمِينِ
Ndipo (ofooka) adzanena (kwa odzikweza): “Inu mumatidzera kumbali komwe timakuganizira kuti nkwabwino (ndi kutichotsako kunka nafe ku njira yopotoka).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
قَالُواْ بَل لَّمۡ تَكُونُواْ مُؤۡمِنِينَ
(Odzikweza) adzayankha: “Koma simudali okhulupirira.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَمَا كَانَ لَنَا عَلَيۡكُم مِّن سُلۡطَٰنِۭۖ بَلۡ كُنتُمۡ قَوۡمٗا طَٰغِينَ
“Ndipo tidalibe nyonga zokuponderezerani inu, koma mudali anthu opyola malire (ndi kutuluka ku choonadi cha Allah).”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَحَقَّ عَلَيۡنَا قَوۡلُ رَبِّنَآۖ إِنَّا لَذَآئِقُونَ
“Choncho mawu a Mbuye wathu (onena za chilango) atsimikizika pa ife; ndithu ife tichilawa (chilango).”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَأَغۡوَيۡنَٰكُمۡ إِنَّا كُنَّا غَٰوِينَ
“Tidakusokeretsani; nafenso tidali osokera. (Choncho musatidzudzule).”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَإِنَّهُمۡ يَوۡمَئِذٖ فِي ٱلۡعَذَابِ مُشۡتَرِكُونَ
Ndithu iwo akathandizana chilango tsiku limenelo (la chiweruziro).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَفۡعَلُ بِٱلۡمُجۡرِمِينَ
Ndithu (chilango chonga chimenecho) ndimomwe timawachitira olakwira (Allah).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّهُمۡ كَانُوٓاْ إِذَا قِيلَ لَهُمۡ لَآ إِلَٰهَ إِلَّا ٱللَّهُ يَسۡتَكۡبِرُونَ
Ndithu iwo ankati akauzidwa kuti palibe wopembedzedwa mwa choonadi koma Allah ankadzitukumula.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَيَقُولُونَ أَئِنَّا لَتَارِكُوٓاْ ءَالِهَتِنَا لِشَاعِرٖ مَّجۡنُونِۭ
Ndipo ankanena: “Kodi ife tisiye kupembedza milungu yathu chifukwa cha zonena za mlakatuli, wopenga?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
بَلۡ جَآءَ بِٱلۡحَقِّ وَصَدَّقَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Iyayi koma adawadzera ndi choonadi (Mthenga wawo Muhammad yemwe siwamisala kapena wolakatula zopeka) ndipo adawatsimikizira za atumiki.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّكُمۡ لَذَآئِقُواْ ٱلۡعَذَابِ ٱلۡأَلِيمِ
Ndithu inu (osakhulupirira) mudzalawa chilango chowawa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَمَا تُجۡزَوۡنَ إِلَّا مَا كُنتُمۡ تَعۡمَلُونَ
Ndipo simudzalipidwa kupatula zokhazo zimene mumachita.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِلَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
Kupatula akapolo a Allah oyeretsedwa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ رِزۡقٞ مَّعۡلُومٞ
Kwa iwo kuli zopatsidwa zodziwika (ndi Mbuye wawo Allah),
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَوَٰكِهُ وَهُم مُّكۡرَمُونَ
Zipatso (zamtundu uliwonse); ndipo iwo adzalandira ulemu (waukulu),
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فِي جَنَّٰتِ ٱلنَّعِيمِ
M’minda ya mtendere.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
عَلَىٰ سُرُرٖ مُّتَقَٰبِلِينَ
Adzakhala pa makama (a mtengo wapatali) uku akuyang’anizana.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
يُطَافُ عَلَيۡهِم بِكَأۡسٖ مِّن مَّعِينِۭ
Uku zikuwazungulira zikho zodzazidwa ndi zakumwa zochokera m’kasupe woyenda nthawi zonse.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
بَيۡضَآءَ لَذَّةٖ لِّلشَّٰرِبِينَ
Woyera, wokoma kwa akumwa (zakumwazo).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
لَا فِيهَا غَوۡلٞ وَلَا هُمۡ عَنۡهَا يُنزَفُونَ
(M’zakumwazo) mulibe zopweteketsa mutu (kwa ozimwa) ndiponso iwo sadzaledzera nazo.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَعِندَهُمۡ قَٰصِرَٰتُ ٱلطَّرۡفِ عِينٞ
Ndipo kwa iwo kudzakhala akazi oyang’ana iwo okha, ophanuka maso (okongola).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
كَأَنَّهُنَّ بَيۡضٞ مَّكۡنُونٞ
Onga ngati dzira (la nthiwatiwa) losungidwa (m’mapiko).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَأَقۡبَلَ بَعۡضُهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖ يَتَسَآءَلُونَ
Ndipo adzayang’anizana ndi kuyamba kufunsana (pakati pawo.)
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
قَالَ قَآئِلٞ مِّنۡهُمۡ إِنِّي كَانَ لِي قَرِينٞ
Adzanena wonena mmodzi wa iwo: “Ine ndidali ndi mnzanga (wopembedza mafano amene amatsutsana nane za chipembedzo ndi zophunzitsa za Qur’an yolemekezeka).”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
يَقُولُ أَءِنَّكَ لَمِنَ ٱلۡمُصَدِّقِينَ
Yemwe amandiuza: “Kodi iwe ndiwe mmodzi wa ovomereza?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَءِذَا مِتۡنَا وَكُنَّا تُرَابٗا وَعِظَٰمًا أَءِنَّا لَمَدِينُونَ
“Zakuti tikadzafa ndi kusanduka fumbi ndi mafupa, (tidzaukanso) ndi kulandira malipiro (pa zochita zathu)?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
قَالَ هَلۡ أَنتُم مُّطَّلِعُونَ
(Wokhulupirira) adzanena (kwa anzake: “Inu anthu a kumtendere) kodi simungasuzumire (nane ku moto kuti timuone)?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱطَّلَعَ فَرَءَاهُ فِي سَوَآءِ ٱلۡجَحِيمِ
Choncho adzayang’ana ndipo adzamuona ali mkatikati mwa moto.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
قَالَ تَٱللَّهِ إِن كِدتَّ لَتُرۡدِينِ
Adzanena: “Ndikulumbilira Allah! Udatsala pang’ono kuti undiononge (ndikadakuvomera paja pa dziko lapansi).”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَلَوۡلَا نِعۡمَةُ رَبِّي لَكُنتُ مِنَ ٱلۡمُحۡضَرِينَ
“Ndipo pakadapanda chisomo cha Mbuye wanga, ndikadakhala mmodzi mwa opezeka ku Moto.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَفَمَا نَحۡنُ بِمَيِّتِينَ
“Kodi zili choncho kuti sitidzafanso (tizingosangalala m’Munda wamtendere).”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِلَّا مَوۡتَتَنَا ٱلۡأُولَىٰ وَمَا نَحۡنُ بِمُعَذَّبِينَ
“Kupatula imfa yathu yoyamba ija, ndi kutinso ife sitilangidwa?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّ هَٰذَا لَهُوَ ٱلۡفَوۡزُ ٱلۡعَظِيمُ
Ndithu izi (zimene Allah waika m’Munda wamtendere) ndiko kupambana kwakukulu.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
لِمِثۡلِ هَٰذَا فَلۡيَعۡمَلِ ٱلۡعَٰمِلُونَ
(Pofuna kupeza) zonga zimenezi ogwira ntchito agwire.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَذَٰلِكَ خَيۡرٞ نُّزُلًا أَمۡ شَجَرَةُ ٱلزَّقُّومِ
Kodi zimenezo ndilo phwando labwino kapena mtengo wa Zaqqum (wowawa kwambiri womwe anthu a ku Moto azikadya)?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّا جَعَلۡنَٰهَا فِتۡنَةٗ لِّلظَّٰلِمِينَ
Ndithu Ife taupanga (mtengo umenewu) kukhala mayeso ndi chilango cha anthu ochimwa (podzichitira okha chinyengo ndi kupembedza mafano.)
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّهَا شَجَرَةٞ تَخۡرُجُ فِيٓ أَصۡلِ ٱلۡجَحِيمِ
Umenewu ndimtengo omwe umatuluka pakatikati pa Jahannam (adaulenga kuchokera ku Moto).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
طَلۡعُهَا كَأَنَّهُۥ رُءُوسُ ٱلشَّيَٰطِينِ
Zipatso zake (nzoipa) ngati mitu ya asatana.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَإِنَّهُمۡ لَأٓكِلُونَ مِنۡهَا فَمَالِـُٔونَ مِنۡهَا ٱلۡبُطُونَ
Ndithu iwo akadya mtengowo ndi kudzaza mimba zawo ndi zipatso zake (pakuti sakapeza chakudya china kupatula zipatso za mtengowo).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ثُمَّ إِنَّ لَهُمۡ عَلَيۡهَا لَشَوۡبٗا مِّنۡ حَمِيمٖ
Kenako, ndithu kuwawa kwa mtengowo kosakanikirana ndi madzi owira kuzakhala pa iwo.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ثُمَّ إِنَّ مَرۡجِعَهُمۡ لَإِلَى ٱلۡجَحِيمِ
Kenako ndithu kobwerera kwawo ndi ku Jahannam.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّهُمۡ أَلۡفَوۡاْ ءَابَآءَهُمۡ ضَآلِّينَ
Ndithu iwo adapeza makolo awo ali osokera.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَهُمۡ عَلَىٰٓ ءَاثَٰرِهِمۡ يُهۡرَعُونَ
Ndipo iwonso adatsata mapazi awo mothamanga.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَلَقَدۡ ضَلَّ قَبۡلَهُمۡ أَكۡثَرُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Ndipo, ndithu akale ambiri adasokera patsogolo pawo.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَلَقَدۡ أَرۡسَلۡنَا فِيهِم مُّنذِرِينَ
Ndipo, ndithu tidatuma achenjezi kwa iwo.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱنظُرۡ كَيۡفَ كَانَ عَٰقِبَةُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Tapenya momwe adalili mapeto a omwe adachenjezedwa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِلَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
Kupatula akapolo a Allah, oyeretsedwa (iwo ndiwo anthu a ku Munda wamtendere).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَلَقَدۡ نَادَىٰنَا نُوحٞ فَلَنِعۡمَ ٱلۡمُجِيبُونَ
Ndithu Nuh adatiitana, (ndipo tidamuyankha mayankho abwino), taonani kukhala bwino Ife Oyankha.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَنَجَّيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥ مِنَ ٱلۡكَرۡبِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo tidampulumutsa iye ndi anthu ake ku vuto lalikulu.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَجَعَلۡنَا ذُرِّيَّتَهُۥ هُمُ ٱلۡبَاقِينَ
Ndipo tidazichita zidzukulu zake kukhala zotsala (pa dziko, oipa ataonongeka).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَتَرَكۡنَا عَلَيۡهِ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndipo tidamsiira mbiri yabwino kwa mibadwo yodza pambuyo pake.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
سَلَٰمٌ عَلَىٰ نُوحٖ فِي ٱلۡعَٰلَمِينَ
Mtendere ukhale pa Nuh pa zolengedwa zonse.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndithu umu ndimomwe Ife tilipirira ochita zabwino.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّهُۥ مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithu iye ndi mmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Kenako tidawamiza enawo.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
۞ وَإِنَّ مِن شِيعَتِهِۦ لَإِبۡرَٰهِيمَ
Ndipo ndithu m’gulu lake (la Nuh) muli Ibrahim.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِذۡ جَآءَ رَبَّهُۥ بِقَلۡبٖ سَلِيمٍ
Kumbuka pamene adadza kwa Mbuye wake ndi mtima wabwino (wogonjera malamulo).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِذۡ قَالَ لِأَبِيهِ وَقَوۡمِهِۦ مَاذَا تَعۡبُدُونَ
Pomwe adanena kwa bambo wake ndi anthu ake: “Mukupembedza chiyani?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَئِفۡكًا ءَالِهَةٗ دُونَ ٱللَّهِ تُرِيدُونَ
“Ha! Milungu yopeka kusiya Allah, ndi imene mukuifuna?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَمَا ظَنُّكُم بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Kodi maganizo anu ngotani pa Mbuye wa zolengedwa zonse?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَنَظَرَ نَظۡرَةٗ فِي ٱلنُّجُومِ
Ndipo adayang’ana nyenyezi mozama.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَقَالَ إِنِّي سَقِيمٞ
Ndipo adanena: “Ine ndine wodwala!”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَتَوَلَّوۡاْ عَنۡهُ مُدۡبِرِينَ
Choncho iwo adatembenuka ndi kumsiya.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَرَاغَ إِلَىٰٓ ءَالِهَتِهِمۡ فَقَالَ أَلَا تَأۡكُلُونَ
(Ibrahim) adapita mozemba ku mafano awo, ndipo adawauza (mwachipongwe:) “Bwanji simukudya (chakudya chomwe chaikidwa patsogolo panupo)?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
مَا لَكُمۡ لَا تَنطِقُونَ
“Bwanji simukuyankhula?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَرَاغَ عَلَيۡهِمۡ ضَرۡبَۢا بِٱلۡيَمِينِ
Atatero adawatembenukira ndi kuwamenya (mwamphamvu) ndi dzanja lamanja.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَأَقۡبَلُوٓاْ إِلَيۡهِ يَزِفُّونَ
(Pamene adamva eni mafanowo) adadza kwa iye akuthamanga.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
قَالَ أَتَعۡبُدُونَ مَا تَنۡحِتُونَ
Anati: “Kodi mukupembedza (miyala) imene mwasema?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَٱللَّهُ خَلَقَكُمۡ وَمَا تَعۡمَلُونَ
“Chikhalirecho Allah ndiye adakulengani ndi zimene mukuchita!”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
قَالُواْ ٱبۡنُواْ لَهُۥ بُنۡيَٰنٗا فَأَلۡقُوهُ فِي ٱلۡجَحِيمِ
Iwo adati: “Mmangireni ng’anjo, ndipo mponyeni m’motowo.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَأَرَادُواْ بِهِۦ كَيۡدٗا فَجَعَلۡنَٰهُمُ ٱلۡأَسۡفَلِينَ
Adafuna kumchita chiwembu (kuti amuphe ndi moto), koma tidawachita kukhala onyozeka.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَقَالَ إِنِّي ذَاهِبٌ إِلَىٰ رَبِّي سَيَهۡدِينِ
Ndipo (Ibrahim) adati: “Ndithu ine ndikupita kwa Mbuye wanga, Iye andiongolera.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
رَبِّ هَبۡ لِي مِنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
“E Mbuye wanga! Ndipatseni mwana yemwe adzakhale (mmodzi) mwa olungama!”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَبَشَّرۡنَٰهُ بِغُلَٰمٍ حَلِيمٖ
Ndipo tidamuuza nkhani yabwino ya mwana wofatsa, (mwanayo ndi Ismaila).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَلَمَّا بَلَغَ مَعَهُ ٱلسَّعۡيَ قَالَ يَٰبُنَيَّ إِنِّيٓ أَرَىٰ فِي ٱلۡمَنَامِ أَنِّيٓ أَذۡبَحُكَ فَٱنظُرۡ مَاذَا تَرَىٰۚ قَالَ يَٰٓأَبَتِ ٱفۡعَلۡ مَا تُؤۡمَرُۖ سَتَجِدُنِيٓ إِن شَآءَ ٱللَّهُ مِنَ ٱلصَّٰبِرِينَ
Ndipo (adabadwa ndi kuyamba kukula.) Pamene adakwana nsinkhu woyenda pamodzi ndi tate wake pochitachita za m’dziko (Ibrahim adayesedwa mayeso kupyolera m’maloto omwe adalota). Adati: “E mwana wanga! Ine kutulo ndikuona maloto (owona ochokera kwa Allah omwe akundilamula) kuti ndikuzinge (monga nsembe yopereka kwa Allah). Nanga ukuti bwanji?” (Mwana wabwino) adanena: “Bambo wanga! Kwaniritsani chimene mukulamulidwa. Ngati Allah afuna, mundipeza ndili mmodzi mwa opirira.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَلَمَّآ أَسۡلَمَا وَتَلَّهُۥ لِلۡجَبِينِ
Pamene adagonjera onse awiri (chofuna cha Allah), ndipo (Ibrahim) adam’goneka chakumphumi (ndipo adatsimikiza kumupha).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَنَٰدَيۡنَٰهُ أَن يَٰٓإِبۡرَٰهِيمُ
Ndipo tidamuitana: “E iwe Ibrahim!”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
قَدۡ صَدَّقۡتَ ٱلرُّءۡيَآۚ إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
“Ndithu wavomereza maloto! (Choncho usamuphe mwana wakoyo).” Umo ndi momwe timawalipirira ochita zabwino.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّ هَٰذَا لَهُوَ ٱلۡبَلَٰٓؤُاْ ٱلۡمُبِينُ
Ndithu amenewa ndimayeso oonekera.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَفَدَيۡنَٰهُ بِذِبۡحٍ عَظِيمٖ
Ndipo tidampulumutsa pompatsa nyama yayikulu (yoti apereke nsembe).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَتَرَكۡنَا عَلَيۡهِ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndipo tidamsiira (mbiri yabwino) kwa anthu ena (amene adadza pambuyo pake).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
سَلَٰمٌ عَلَىٰٓ إِبۡرَٰهِيمَ
Mtendere ukhale pa Ibrahim!
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
M’menemo ndi mornwe timawalipirira ochita zabwino.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّهُۥ مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithu iye adali mmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَبَشَّرۡنَٰهُ بِإِسۡحَٰقَ نَبِيّٗا مِّنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
Ndiponso tidamuuza nkhani yabwino (yoti akhala ndi mwana wotchedwa) Isihaqa; mneneri; wam’gulu la olungama.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَبَٰرَكۡنَا عَلَيۡهِ وَعَلَىٰٓ إِسۡحَٰقَۚ وَمِن ذُرِّيَّتِهِمَا مُحۡسِنٞ وَظَالِمٞ لِّنَفۡسِهِۦ مُبِينٞ
Ndipo tidamdalitsa iye ndi (mwana wake) Isihaqa; ndipo m’mbumba ya awiriwa mudapezeka abwino ndi odzichitira zoipa owonekera.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَلَقَدۡ مَنَنَّا عَلَىٰ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
Ndipo ndithu tidawachitira zabwino Mûsa ndi Haruna, (powapatsa uneneri ndi madalitso ambiri).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَنَجَّيۡنَٰهُمَا وَقَوۡمَهُمَا مِنَ ٱلۡكَرۡبِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo tidawapulumutsa (awiriwa) ndi anthu awo ku vuto lalikulu.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَنَصَرۡنَٰهُمۡ فَكَانُواْ هُمُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
Ndipo tidawathangata (powagonjetsera adani awo), ndipo iwo adali opambana.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَءَاتَيۡنَٰهُمَا ٱلۡكِتَٰبَ ٱلۡمُسۡتَبِينَ
Ndipo tidawapatsa (Mûsa ndi Haruna) buku losonyeza poyera (malamulo).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَهَدَيۡنَٰهُمَا ٱلصِّرَٰطَ ٱلۡمُسۡتَقِيمَ
Ndipo tidawaongolera ku njira yolunjika.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَتَرَكۡنَا عَلَيۡهِمَا فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndiponso tidawasiira (mbiri yabwino) kwa anthu ena (amene adadza pambuyo pawo).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
سَلَٰمٌ عَلَىٰ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
Mtendere ukhale pa Mûsa ndi Haruna!
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndithu umu ndi momwe Ife timawalipirira ochita zabwino.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّهُمَا مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithu awiriwa adali m’gulu la akapoio Athu okhulupirira.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِنَّ إِلۡيَاسَ لَمِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndipo ndithu Iliyasa ndi mmodzi wa atumiki.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِذۡ قَالَ لِقَوۡمِهِۦٓ أَلَا تَتَّقُونَ
(Kumbuka) pamene adanena kwa anthu ake: “Bwanji simuopa (Allah)?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَتَدۡعُونَ بَعۡلٗا وَتَذَرُونَ أَحۡسَنَ ٱلۡخَٰلِقِينَ
“Mukupembedza (fano lotchedwa) Ba’la ndi kusiya (kupembedza) Wabwino zedi mwa olenga onse.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ٱللَّهَ رَبَّكُمۡ وَرَبَّ ءَابَآئِكُمُ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Allah, Mbuye wanu ndi Mbuye wa makolo anu akale?”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَكَذَّبُوهُ فَإِنَّهُمۡ لَمُحۡضَرُونَ
Koma adamtsutsa; ndithu iwo adzaonekera (ku Moto).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِلَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
Kupatula akapolo a Allah amene ayeretsedwa (ndi Allah).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَتَرَكۡنَا عَلَيۡهِ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndipo tidamsiira (mbiri yabwino) kwa anthu ena (amene adadza pambuyo pake).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
سَلَٰمٌ عَلَىٰٓ إِلۡ يَاسِينَ
Mtendere ukhale pa Iliyasiin!
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّا كَذَٰلِكَ نَجۡزِي ٱلۡمُحۡسِنِينَ
Ndithu umo ndi mmene Ife timawalipirira ochita zabwino.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّهُۥ مِنۡ عِبَادِنَا ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndithu iye ndimmodzi mwa akapolo Athu okhulupirira.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِنَّ لُوطٗا لَّمِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndithu Luti ndi mmodzi wa atumiki.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِذۡ نَجَّيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
(Kumbuka) pamene tidampulumutsa iye ndi anthu ake onse.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِلَّا عَجُوزٗا فِي ٱلۡغَٰبِرِينَ
Kupatula nkhalamba yachikazi; idali mwa otsalira.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ثُمَّ دَمَّرۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Kenako tidawaononga enawo (omwe adali oipa).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِنَّكُمۡ لَتَمُرُّونَ عَلَيۡهِم مُّصۡبِحِينَ
Ndithu inu (a mumzinda wa Makka) mumadutsa pa malo pawopo m’mawa,
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَبِٱلَّيۡلِۚ أَفَلَا تَعۡقِلُونَ
Ndi usiku. Kodi bwanji simuzindikira?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِنَّ يُونُسَ لَمِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndithu Yunusu ndi mmodzi wa atumiki.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِذۡ أَبَقَ إِلَى ٱلۡفُلۡكِ ٱلۡمَشۡحُونِ
(Kumbuka) pamene adathawira m’chombo chodzazidwa (ndi katundu).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَسَاهَمَ فَكَانَ مِنَ ٱلۡمُدۡحَضِينَ
Choncho adachita mayere, ndipo adali m’gulu la omgwera (mayerewo).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱلۡتَقَمَهُ ٱلۡحُوتُ وَهُوَ مُلِيمٞ
Choncho nsomba idammeza uku ali wodzudzulidwa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَلَوۡلَآ أَنَّهُۥ كَانَ مِنَ ٱلۡمُسَبِّحِينَ
Kukadapanda kuti iye adali m’modzi mwa otamanda ndi kulemekeza Allah).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
لَلَبِثَ فِي بَطۡنِهِۦٓ إِلَىٰ يَوۡمِ يُبۡعَثُونَ
Akadakhala m’mimba mwake mpaka tsiku loukitsidwa (zolengedwa ku imfa).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
۞ فَنَبَذۡنَٰهُ بِٱلۡعَرَآءِ وَهُوَ سَقِيمٞ
Koma tidamponya pa gombe uku ali wodwala.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَأَنۢبَتۡنَا عَلَيۡهِ شَجَرَةٗ مِّن يَقۡطِينٖ
Ndipo tidammeretsera mmera wa mtundu wa nkhaka.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَأَرۡسَلۡنَٰهُ إِلَىٰ مِاْئَةِ أَلۡفٍ أَوۡ يَزِيدُونَ
Ndipo (atachira) tidamtuma ku anthu okwana zikwi zana limodzi (100,000) kapena kupambana apa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَـَٔامَنُواْ فَمَتَّعۡنَٰهُمۡ إِلَىٰ حِينٖ
Ndipo adakhulupirira (ndi kuvomereza ulaliki wake); choncho tidawapatsa chisangalalo kufikira nthawi (ya imfa yawo).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَٱسۡتَفۡتِهِمۡ أَلِرَبِّكَ ٱلۡبَنَاتُ وَلَهُمُ ٱلۡبَنُونَ
Choncho afunse: “Kodi Mbuye wako ndiye woyenera ana aakazi, ndipo iwo aamuna? (Pomwe iwo akabereka mwana wamkazi amanyansidwa naye)!”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَمۡ خَلَقۡنَا ٱلۡمَلَٰٓئِكَةَ إِنَٰثٗا وَهُمۡ شَٰهِدُونَ
Kapena kuti tidalenga angelo kukhala akazi, iwo akuona?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَلَآ إِنَّهُم مِّنۡ إِفۡكِهِمۡ لَيَقُولُونَ
Chenjera ndi bodza lawolo, ndithu iwo akunena:
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَلَدَ ٱللَّهُ وَإِنَّهُمۡ لَكَٰذِبُونَ
“Allah wabereka.” Ndithu iwo ndi abodza.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَصۡطَفَى ٱلۡبَنَاتِ عَلَى ٱلۡبَنِينَ
Kodi Iye adasankha ana aakazi kusiya aamuna?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
مَا لَكُمۡ كَيۡفَ تَحۡكُمُونَ
Kodi nchiyani chakupezani (kuti muweruze mopanda chilungamo); nanga mukuweruza bwanji (zimenezi)?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَفَلَا تَذَكَّرُونَ
Kodi bwanji simukumbukira, (mwaiwala zisonyezo Zake zodabwitsa ndi kupatukana kwake ndi zimenezo)?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَمۡ لَكُمۡ سُلۡطَٰنٞ مُّبِينٞ
Kapena inu muli ndi umboni woonekera (wochokera kumwamba)?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَأۡتُواْ بِكِتَٰبِكُمۡ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Tabweretsani buku lanulo (momwe mwalembedwa zimenezi) ngati mukunena zoona.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَجَعَلُواْ بَيۡنَهُۥ وَبَيۡنَ ٱلۡجِنَّةِ نَسَبٗاۚ وَلَقَدۡ عَلِمَتِ ٱلۡجِنَّةُ إِنَّهُمۡ لَمُحۡضَرُونَ
Ndipo adapeka chibale pakati pa Iye (Allah) ndi ziwanda; (pomwe ziwanda nzobisika kwa iwo). Ndithu ziwanda zimadziwa kuti iwo osakhulupirira akaonekera (kwa Allah kuti aweruzidwe)!
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
سُبۡحَٰنَ ٱللَّهِ عَمَّا يَصِفُونَ
Walemekezeka Allah! Ndi kupatukana ndi zimene akumnamizira!
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِلَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
Koma akapolo a Allah oyeretsedwa (ali kutali ndi zimene akusimba osakhulupirirazi).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَإِنَّكُمۡ وَمَا تَعۡبُدُونَ
Ndithu inu (osakhulupirira) ndi zimene mukuzipembedza (kusiya Allah),
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
مَآ أَنتُمۡ عَلَيۡهِ بِفَٰتِنِينَ
Ndi zimenezo simungamsokeretse aliyense.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِلَّا مَنۡ هُوَ صَالِ ٱلۡجَحِيمِ
Kupatula yemwe (Allah adadziwa kuti) ngolowa ku Jahannam.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَمَا مِنَّآ إِلَّا لَهُۥ مَقَامٞ مَّعۡلُومٞ
Ndipo (angelo adanena): “Aliyense mwa ife ali ndi malo ake odziwika.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِنَّا لَنَحۡنُ ٱلصَّآفُّونَ
“Ndipo ndithu (ena mwa) ife ngondanda m’mizere (ya mapemphero nthawi zonse).”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِنَّا لَنَحۡنُ ٱلۡمُسَبِّحُونَ
“Ndipo (ena mwa) ife ngolemekeza (Allah nthawi zonse ndi kumtamanda ndi kumpatula ku zinthu zosayenerana ndi ulemelero wake).”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِن كَانُواْ لَيَقُولُونَ
Ndipo (osakhulupirira) ankati:
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
لَوۡ أَنَّ عِندَنَا ذِكۡرٗا مِّنَ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Tikadakhala ndi buku monga lomwe anthu akale adali nalo.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
لَكُنَّا عِبَادَ ٱللَّهِ ٱلۡمُخۡلَصِينَ
“Tikadakhala akapolo a Allah, oyeretsedwa.”
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَكَفَرُواْ بِهِۦۖ فَسَوۡفَ يَعۡلَمُونَ
Koma (pamene lidawadzera bukulo), adalikana; choncho posachedwa adziwa (zotsatira zake).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَلَقَدۡ سَبَقَتۡ كَلِمَتُنَا لِعِبَادِنَا ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndipo ndithu liwu lathu lidatsogola kwa akapolo athu otumidwa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّهُمۡ لَهُمُ ٱلۡمَنصُورُونَ
(Kuti) ndithu iwo ngopulumutsidwa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِنَّ جُندَنَا لَهُمُ ٱلۡغَٰلِبُونَ
Ndipo ndithu asilikali Athu ndi opambana.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَتَوَلَّ عَنۡهُمۡ حَتَّىٰ حِينٖ
Choncho, asiye kwa kanthawi kochepa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَأَبۡصِرۡهُمۡ فَسَوۡفَ يُبۡصِرُونَ
Ndipo ingowayang’ana basi; posachedwapa aona!
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
أَفَبِعَذَابِنَا يَسۡتَعۡجِلُونَ
Kodi chilango chathu akuchifulumizitsa?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فَإِذَا نَزَلَ بِسَاحَتِهِمۡ فَسَآءَ صَبَاحُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Choncho chikadzatsika pabwalo lawo, udzakhala mmawa woipa kwa ochenjezedwa!
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَتَوَلَّ عَنۡهُمۡ حَتَّىٰ حِينٖ
Ndipo asiye kwa kanthawi kochepa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَأَبۡصِرۡ فَسَوۡفَ يُبۡصِرُونَ
Ndipo ingowayang’ana basi; posachedwapa aona.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
سُبۡحَٰنَ رَبِّكَ رَبِّ ٱلۡعِزَّةِ عَمَّا يَصِفُونَ
Mbuye wako, Mwini ulemelero, wapatukana ndi zimene akumnamizira (osakhulupirira).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَسَلَٰمٌ عَلَى ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Ndipo mtendere ukhale pa atumiki onse.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo kuyamikidwa konse nkwa Allah, Mbuye wa zolengedwa zonse.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: ሱረቱ አስ ሷፋት
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም - የትርጉሞች ማዉጫ

የተከበረው ቁርአን ቸዋኛ መልዕክተ ትርጉም፤ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ የ 2020 ቅጅ

መዝጋት