للإطلاع على الموقع بحلته الجديدة

ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - خالد إبراهيم بتيالا * - فهرس التراجم


ترجمة معاني سورة: الواقعة   آية:
يَطُوفُ عَلَيۡهِمۡ وِلۡدَٰنٞ مُّخَلَّدُونَ
Anyamata osasintha adzakhala akuwazungulira iwo (ndi kuwatumikira).
التفاسير العربية:
بِأَكۡوَابٖ وَأَبَارِيقَ وَكَأۡسٖ مِّن مَّعِينٖ
Uku atatenga matambula ndi maketulo (odzaza ndi zakumwa za ku Jannah), ndi zipanda zodzaza ndi zakumwa zochokera mu akasupe oyenda;
التفاسير العربية:
لَّا يُصَدَّعُونَ عَنۡهَا وَلَا يُنزِفُونَ
(Zakumwa zake) zosapweteketsa mutu ndiponso zosaledzeretsa;
التفاسير العربية:
وَفَٰكِهَةٖ مِّمَّا يَتَخَيَّرُونَ
Ndi zipatso (zamitundumitundu) zimene azikazisankha;
التفاسير العربية:
وَلَحۡمِ طَيۡرٖ مِّمَّا يَشۡتَهُونَ
Ndi nyama yambalame imene mitima yawo izikafuna;
التفاسير العربية:
وَحُورٌ عِينٞ
Ndi akazi ophanuka maso mokongola,
التفاسير العربية:
كَأَمۡثَٰلِ ٱللُّؤۡلُوِٕ ٱلۡمَكۡنُونِ
(Kukongola kwawo) ndiye ngati ngale zosungidwa bwino mzigoba zake.
التفاسير العربية:
جَزَآءَۢ بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Kukhala mphoto chifukwa cha zimene amachita (zabwino padziko lapansi).
التفاسير العربية:
لَا يَسۡمَعُونَ فِيهَا لَغۡوٗا وَلَا تَأۡثِيمًا
M’menemo sakamva mawu achabe ngakhale (mawu a) machimo,
التفاسير العربية:
إِلَّا قِيلٗا سَلَٰمٗا سَلَٰمٗا
Koma mawu oti: “Mtendere! Mtendere!”
التفاسير العربية:
وَأَصۡحَٰبُ ٱلۡيَمِينِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلۡيَمِينِ
Anthu akudzanja lamanja. Taonani kukula malipiro a anthu akudzanja lamanja!
التفاسير العربية:
فِي سِدۡرٖ مَّخۡضُودٖ
(Adzakhala m’mithunzi ya) mitengo ya masawu yopanda minga.
التفاسير العربية:
وَطَلۡحٖ مَّنضُودٖ
Ndi mitengo ya nthochi yobereka kwambiri.
التفاسير العربية:
وَظِلّٖ مَّمۡدُودٖ
Ndi m’mithunzi yotambasuka kwambiri, yosachoka,
التفاسير العربية:
وَمَآءٖ مَّسۡكُوبٖ
Ndi madzi oyenda mosalekeza,
التفاسير العربية:
وَفَٰكِهَةٖ كَثِيرَةٖ
Ndi zipatso zambiri,
التفاسير العربية:
لَّا مَقۡطُوعَةٖ وَلَا مَمۡنُوعَةٖ
Zopezeka mnyengo zonse, ndiponso zosaletsedwa (kwa amene akuzifuna).
التفاسير العربية:
وَفُرُشٖ مَّرۡفُوعَةٍ
Ndi zoyala zapamwamba (zawofuwofu).
التفاسير العربية:
إِنَّآ أَنشَأۡنَٰهُنَّ إِنشَآءٗ
Ndithu tidzawalenga (akazi okhulupirira) m’kalengedwe kapamwamba.
التفاسير العربية:
فَجَعَلۡنَٰهُنَّ أَبۡكَارًا
Tidzawapanga kukhala anamwali.
التفاسير العربية:
عُرُبًا أَتۡرَابٗا
Okondedwa ndi amuna awo; ofanana misinkhu,
التفاسير العربية:
لِّأَصۡحَٰبِ ٱلۡيَمِينِ
A anthu akudzanja la manja.
التفاسير العربية:
ثُلَّةٞ مِّنَ ٱلۡأَوَّلِينَ
Gulu lalikulu lochokera ku m’badwo woyamba.
التفاسير العربية:
وَثُلَّةٞ مِّنَ ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndiponso gulu lalikulu lochokera ku mibadwo yotsiriza.
التفاسير العربية:
وَأَصۡحَٰبُ ٱلشِّمَالِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلشِّمَالِ
Anthu akudzanja lakumanzere. Taonani chilango choopsa kwa anthu akudzanja lakumanzere!
التفاسير العربية:
فِي سَمُومٖ وَحَمِيمٖ
Adzakhala mu mvuchi wamoto ndi m’madzi owira.
التفاسير العربية:
وَظِلّٖ مِّن يَحۡمُومٖ
Ndi mumthunzi wa utsi wakuda.
التفاسير العربية:
لَّا بَارِدٖ وَلَا كَرِيمٍ
Siwoziziritsa ndiponso siwosangalatsa.
التفاسير العربية:
إِنَّهُمۡ كَانُواْ قَبۡلَ ذَٰلِكَ مُتۡرَفِينَ
Ndithu iwo amakhala kalelo mosangalala (samalabadira kumvera Allah),
التفاسير العربية:
وَكَانُواْ يُصِرُّونَ عَلَى ٱلۡحِنثِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo amapitiriza kuchita machimo aakulu (polinga kuti palibe kuuka ku imfa).
التفاسير العربية:
وَكَانُواْ يَقُولُونَ أَئِذَا مِتۡنَا وَكُنَّا تُرَابٗا وَعِظَٰمًا أَءِنَّا لَمَبۡعُوثُونَ
Ndipo amanena (motsutsa); “Kodi tikadzafa nkusanduka fumbi ndi mafupa ofumbwa, tidzaukitsidwanso?”
التفاسير العربية:
أَوَءَابَآؤُنَا ٱلۡأَوَّلُونَ
“Kodi ndi makolo athu akale (adzaukitsidwanso!)”
التفاسير العربية:
قُلۡ إِنَّ ٱلۡأَوَّلِينَ وَٱلۡأٓخِرِينَ
Nena kwa iwo (poyankha kutsutsa kwawo). Ndithudi, amibadwo yoyamba ndi mibadwo yomaliza (omwe inu muli m’gulu lawo),
التفاسير العربية:
لَمَجۡمُوعُونَ إِلَىٰ مِيقَٰتِ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Adzasonkhanitsidwa m’nthawi ya tsiku lomwe lakhazikitsidwa.
التفاسير العربية:
 
ترجمة معاني سورة: الواقعة
فهرس السور رقم الصفحة
 
ترجمة معاني القرآن الكريم - الترجمة الشيشيوا - خالد إبراهيم بتيالا - فهرس التراجم

ترجمها خالد إبراهيم بيتالا.

إغلاق