Check out the new design

அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: அல்வாகிஆ   வசனம்:
يَطُوفُ عَلَيۡهِمۡ وِلۡدَٰنٞ مُّخَلَّدُونَ
Anyamata osasintha adzakhala akuwazungulira iwo (ndi kuwatumikira).
அரபு விரிவுரைகள்:
بِأَكۡوَابٖ وَأَبَارِيقَ وَكَأۡسٖ مِّن مَّعِينٖ
Uku atatenga matambula ndi maketulo (odzaza ndi zakumwa za ku Jannah), ndi zipanda zodzaza ndi zakumwa zochokera mu akasupe oyenda;
அரபு விரிவுரைகள்:
لَّا يُصَدَّعُونَ عَنۡهَا وَلَا يُنزِفُونَ
(Zakumwa zake) zosapweteketsa mutu ndiponso zosaledzeretsa;
அரபு விரிவுரைகள்:
وَفَٰكِهَةٖ مِّمَّا يَتَخَيَّرُونَ
Ndi zipatso (zamitundumitundu) zimene azikazisankha;
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَحۡمِ طَيۡرٖ مِّمَّا يَشۡتَهُونَ
Ndi nyama yambalame imene mitima yawo izikafuna;
அரபு விரிவுரைகள்:
وَحُورٌ عِينٞ
Ndi akazi ophanuka maso mokongola,
அரபு விரிவுரைகள்:
كَأَمۡثَٰلِ ٱللُّؤۡلُوِٕ ٱلۡمَكۡنُونِ
(Kukongola kwawo) ndiye ngati ngale zosungidwa bwino mzigoba zake.
அரபு விரிவுரைகள்:
جَزَآءَۢ بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Kukhala mphoto chifukwa cha zimene amachita (zabwino padziko lapansi).
அரபு விரிவுரைகள்:
لَا يَسۡمَعُونَ فِيهَا لَغۡوٗا وَلَا تَأۡثِيمًا
M’menemo sakamva mawu achabe ngakhale (mawu a) machimo,
அரபு விரிவுரைகள்:
إِلَّا قِيلٗا سَلَٰمٗا سَلَٰمٗا
Koma mawu oti: “Mtendere! Mtendere!”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَأَصۡحَٰبُ ٱلۡيَمِينِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلۡيَمِينِ
Anthu akudzanja lamanja. Taonani kukula malipiro a anthu akudzanja lamanja!
அரபு விரிவுரைகள்:
فِي سِدۡرٖ مَّخۡضُودٖ
(Adzakhala m’mithunzi ya) mitengo ya masawu yopanda minga.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَطَلۡحٖ مَّنضُودٖ
Ndi mitengo ya nthochi yobereka kwambiri.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَظِلّٖ مَّمۡدُودٖ
Ndi m’mithunzi yotambasuka kwambiri, yosachoka,
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَآءٖ مَّسۡكُوبٖ
Ndi madzi oyenda mosalekeza,
அரபு விரிவுரைகள்:
وَفَٰكِهَةٖ كَثِيرَةٖ
Ndi zipatso zambiri,
அரபு விரிவுரைகள்:
لَّا مَقۡطُوعَةٖ وَلَا مَمۡنُوعَةٖ
Zopezeka mnyengo zonse, ndiponso zosaletsedwa (kwa amene akuzifuna).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَفُرُشٖ مَّرۡفُوعَةٍ
Ndi zoyala zapamwamba (zawofuwofu).
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّآ أَنشَأۡنَٰهُنَّ إِنشَآءٗ
Ndithu tidzawalenga (akazi okhulupirira) m’kalengedwe kapamwamba.
அரபு விரிவுரைகள்:
فَجَعَلۡنَٰهُنَّ أَبۡكَارًا
Tidzawapanga kukhala anamwali.
அரபு விரிவுரைகள்:
عُرُبًا أَتۡرَابٗا
Okondedwa ndi amuna awo; ofanana misinkhu,
அரபு விரிவுரைகள்:
لِّأَصۡحَٰبِ ٱلۡيَمِينِ
A anthu akudzanja la manja.
அரபு விரிவுரைகள்:
ثُلَّةٞ مِّنَ ٱلۡأَوَّلِينَ
Gulu lalikulu lochokera ku m’badwo woyamba.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَثُلَّةٞ مِّنَ ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndiponso gulu lalikulu lochokera ku mibadwo yotsiriza.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَأَصۡحَٰبُ ٱلشِّمَالِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلشِّمَالِ
Anthu akudzanja lakumanzere. Taonani chilango choopsa kwa anthu akudzanja lakumanzere!
அரபு விரிவுரைகள்:
فِي سَمُومٖ وَحَمِيمٖ
Adzakhala mu mvuchi wamoto ndi m’madzi owira.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَظِلّٖ مِّن يَحۡمُومٖ
Ndi mumthunzi wa utsi wakuda.
அரபு விரிவுரைகள்:
لَّا بَارِدٖ وَلَا كَرِيمٍ
Siwoziziritsa ndiponso siwosangalatsa.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِنَّهُمۡ كَانُواْ قَبۡلَ ذَٰلِكَ مُتۡرَفِينَ
Ndithu iwo amakhala kalelo mosangalala (samalabadira kumvera Allah),
அரபு விரிவுரைகள்:
وَكَانُواْ يُصِرُّونَ عَلَى ٱلۡحِنثِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo amapitiriza kuchita machimo aakulu (polinga kuti palibe kuuka ku imfa).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَكَانُواْ يَقُولُونَ أَئِذَا مِتۡنَا وَكُنَّا تُرَابٗا وَعِظَٰمًا أَءِنَّا لَمَبۡعُوثُونَ
Ndipo amanena (motsutsa); “Kodi tikadzafa nkusanduka fumbi ndi mafupa ofumbwa, tidzaukitsidwanso?”
அரபு விரிவுரைகள்:
أَوَءَابَآؤُنَا ٱلۡأَوَّلُونَ
“Kodi ndi makolo athu akale (adzaukitsidwanso!)”
அரபு விரிவுரைகள்:
قُلۡ إِنَّ ٱلۡأَوَّلِينَ وَٱلۡأٓخِرِينَ
Nena kwa iwo (poyankha kutsutsa kwawo). Ndithudi, amibadwo yoyamba ndi mibadwo yomaliza (omwe inu muli m’gulu lawo),
அரபு விரிவுரைகள்:
لَمَجۡمُوعُونَ إِلَىٰ مِيقَٰتِ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Adzasonkhanitsidwa m’nthawi ya tsiku lomwe lakhazikitsidwa.
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: அல்வாகிஆ
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

மொழிபெயர்த்தது காலித் இப்ராஹீம் பைதாலா.

மூடுக