আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চেৱা অনুবাদ * - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ


অৰ্থানুবাদ ছুৰা: ছুৰা আল-মুতাফ্ফিফীন   আয়াত:

ছুৰা আল-মুতাফ্ফিফীন

وَيۡلٞ لِّلۡمُطَفِّفِينَ
Kuonongeka koopsa kukawapeza opunguza miyeso ya malonda.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ٱلَّذِينَ إِذَا ٱكۡتَالُواْ عَلَى ٱلنَّاسِ يَسۡتَوۡفُونَ
Amene amati akamadziyezera zinthu kwa anthu amafuna kulandira miyeso yodzadza.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَإِذَا كَالُوهُمۡ أَو وَّزَنُوهُمۡ يُخۡسِرُونَ
Koma pamene iwo akamawayesera pa muyeso wa mbale kapena wa sikelo amapungula (choyenera kulandira ogulawo).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَلَا يَظُنُّ أُوْلَٰٓئِكَ أَنَّهُم مَّبۡعُوثُونَ
Kodi amenewa (akupungula miyeso pamalondawo) sakuganiza kuti adzaukitsidwa;
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
لِيَوۡمٍ عَظِيمٖ
Pa tsiku lalikulu (ndiponso loopsa)?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
يَوۡمَ يَقُومُ ٱلنَّاسُ لِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Tsiku limene adzaimilira anthu pamaso pa Mbuye wa zolengedwa.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
كَلَّآ إِنَّ كِتَٰبَ ٱلۡفُجَّارِ لَفِي سِجِّينٖ
Ayi! Ndithu (siyani chinyengo pamalonda ndi kusalabadira kuuka mmanda); zolembedwa za ntchito ya oipa zili mu Sijjin.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سِجِّينٞ
Nanga nchiyani chitakudziwitse za Sijjin?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
كِتَٰبٞ مَّرۡقُومٞ
Ameneyu ndi kaundula wamkulu yemwe walembedwa (mkati mwake ntchito za anthu oipa).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Chilango chaukali tsiku limenelo chili pa otsutsa,[401]
[401] Kutsutsa kulipo kwa mitundu itatu:
(a) Kutsutsa kwa mawu ndi zochita;
(b) Kutsutsa kwa zochita zokha, monga ukauzidwa kuti chinthu ichi nchoipa, munthu nkudziwa kuti zoona nchoipadi koma nkudzachichita chimenecho mosalabadira;
(c) Kutsutsa ndi zolankhula zokha. Kumeneko ndiko monga munthu akudziwa kuti chakutichakuti ncholetsedwa (haramu) koma m’malo mwake iye nkumati chimenecho nchovomerezeka (halali)
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ٱلَّذِينَ يُكَذِّبُونَ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Amene akutsutsa za tsiku la malipiro.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَمَا يُكَذِّبُ بِهِۦٓ إِلَّا كُلُّ مُعۡتَدٍ أَثِيمٍ
Ndipo palibe angalitsutse koma yekhayo wopyola malire (pochita zoipa), wa machimo ambiri;
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِ ءَايَٰتُنَا قَالَ أَسَٰطِيرُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Pamene ma Ayah Athu akuwerengedwa kwa iye (onena za tsiku la malipiro ndikuuka mmanda) amanena kuti: “Izi ndi nthano za anthu akale.”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
كَلَّاۖ بَلۡۜ رَانَ عَلَىٰ قُلُوبِهِم مَّا كَانُواْ يَكۡسِبُونَ
Iyayi, sichoncho! Koma yaphimbidwa mitima yawo ndi dzimbiri (la machimo) omwe akhala akukolola.[402]
[402] Munthu akachita choipa koyamba ndipo osalapa, limalowa dontho lakuda mu mtima mwake; nthawi iliyonse pamene akuonjezera machimo, dontho lija limakulirakulira mpaka kuuphimba mtima wonse. Dontho limeneli ndilo likutchedwa “Ran.” Tsono mtima ngati utaphimbidwa chotere sulabadira kuchita zoipa, ngakhale kuti auongole sungaongoke.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
كَلَّآ إِنَّهُمۡ عَن رَّبِّهِمۡ يَوۡمَئِذٖ لَّمَحۡجُوبُونَ
Ayi ndithu iwo (okanira) tsiku limenelo) adzatchingidwa kwa Mbuye wawo; (sadzamuona).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ثُمَّ إِنَّهُمۡ لَصَالُواْ ٱلۡجَحِيمِ
Pambuyo pake adzalowa ku Moto; (oyaka)
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ثُمَّ يُقَالُ هَٰذَا ٱلَّذِي كُنتُم بِهِۦ تُكَذِّبُونَ
Kenaka adzauzidwa (powaliritsa) “Ichi nchilango chomwe mudali kuchitsutsa (pa dziko lapansi).”
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
كَلَّآ إِنَّ كِتَٰبَ ٱلۡأَبۡرَارِ لَفِي عِلِّيِّينَ
Zoona, ndithu kaundula wa anthu abwino (ochita ntchito zabwino) ali mu Illiyyun.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا عِلِّيُّونَ
Nanga nchiyani chitakudziwitse za Illiyyun?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
كِتَٰبٞ مَّرۡقُومٞ
Ameneyu ndi kaundula (wamkulu) yemwe walembedwa (mkati mwake ntchito za anthu abwino);
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
يَشۡهَدُهُ ٱلۡمُقَرَّبُونَ
Amamuyikira umboni (angelo) amene ayandikitsidwa (kwa Allah).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِنَّ ٱلۡأَبۡرَارَ لَفِي نَعِيمٍ
Ndithu ochita zabwino adzakhala mu mtendere,
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
عَلَى ٱلۡأَرَآئِكِ يَنظُرُونَ
Atakhala pa mipando ya ulemu uku akuyang’ana (zimene Allah wawapatsa monga mtendere ndi ulemelero).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
تَعۡرِفُ فِي وُجُوهِهِمۡ نَضۡرَةَ ٱلنَّعِيمِ
Udzaona kuwala kwa mtendere pa nkhope zawo;
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
يُسۡقَوۡنَ مِن رَّحِيقٖ مَّخۡتُومٍ
Adzamwetsedwa vinyo (woyeretsedwa) wotsekeredwa ndi zitsekerero zolimba;
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
خِتَٰمُهُۥ مِسۡكٞۚ وَفِي ذَٰلِكَ فَلۡيَتَنَافَسِ ٱلۡمُتَنَٰفِسُونَ
Komalizira kwake (kwa vinyoyo) kuzikatuluka fungo la misk; kuti akapeze zimenezi, apikisane opikisana.[403]
[403] Apa, akutilamula kupikisana pakuchita zabwino kuti tipeze madalitso amene awakonzera anthu abwino. Kumeneko ndikuti munthu aliyense alimbikire kuchita mapemphero ndi zina zabwino.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَمِزَاجُهُۥ مِن تَسۡنِيمٍ
Ndipo chosakanizira cha vinyoyo ndi madzi a Tasnim.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
عَيۡنٗا يَشۡرَبُ بِهَا ٱلۡمُقَرَّبُونَ
(Tasnim ameneyo) ndi kasupe amene azikamwa amene ayandikitsidwa (kwa Allah.)
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِنَّ ٱلَّذِينَ أَجۡرَمُواْ كَانُواْ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ يَضۡحَكُونَ
Ndithu amene adachita machimo adali kuwaseka (mwachipongwe) okhulupirira (pa dziko lapansi);
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَإِذَا مَرُّواْ بِهِمۡ يَتَغَامَزُونَ
(Okhulupirira) akadutsa pafupi ndi iwo ankakodolerana maso (mwachipongwe);
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَإِذَا ٱنقَلَبُوٓاْ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِمُ ٱنقَلَبُواْ فَكِهِينَ
Ndipo akabwerera kwa anzawo amabwerera akusangalala (ndi kunyozedwa kwa okhulupirira);
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَإِذَا رَأَوۡهُمۡ قَالُوٓاْ إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ لَضَآلُّونَ
Ndipo (nthawi zonse) akawaona Asilamu amanena: “Ndithu awa ndi osokera (chifukwa chomkhulupirira Mtumiki).” (s.a.w)
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَمَآ أُرۡسِلُواْ عَلَيۡهِمۡ حَٰفِظِينَ
Sanatumizidwe (Akafiri) kukhala ayang’aniri kwa okhulupirira (ndikuwaweruza zakulungama ndi kusokera).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَٱلۡيَوۡمَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مِنَ ٱلۡكُفَّارِ يَضۡحَكُونَ
Basi lero okhulupirira awaseka osakhulupirira (powabwezera chipongwe chawo chimene ankachita pa dziko lapansi),[404]
[404] (Ndime 34-36) Tanthauzo lake ndikuti okhulupilira, tsiku lachimaliziro adzakhala m’mipando ya ulemu uku akuwayang’ana ndi kuwaseka anthu osakhulupilira ali m’mavuto monga momwe iwo adali kuseka okhulupilira pa dziko lapansi.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
عَلَى ٱلۡأَرَآئِكِ يَنظُرُونَ
Atakhala pa mipando ya ulemu uku akuyang’ana (mtendere umene Allah wawapatsa).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
هَلۡ ثُوِّبَ ٱلۡكُفَّارُ مَا كَانُواْ يَفۡعَلُونَ
Kodi alipidwa osakhulupirira pa zomwe ankachita zija (pa dziko lapansi)?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
 
অৰ্থানুবাদ ছুৰা: ছুৰা আল-মুতাফ্ফিফীন
ছুৰাৰ তালিকা পৃষ্ঠা নং
 
আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চেৱা অনুবাদ - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ

চেৱা ভাষাত কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ- অনুবাদ কৰিছে খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা। ২০২০ চন।

বন্ধ