Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə * - Tərcumənin mündəricatı


Mənaların tərcüməsi Surə: əl-Vaqiə   Ayə:

əl-Vaqiə

إِذَا وَقَعَتِ ٱلۡوَاقِعَةُ
Chikadzachitika chochitikacho (Qiyâma).
Ərəbcə təfsirlər:
لَيۡسَ لِوَقۡعَتِهَا كَاذِبَةٌ
Palibe wotsutsa za kuchitika kwake.
Ərəbcə təfsirlər:
خَافِضَةٞ رَّافِعَةٌ
Chidzatsitsa (oipa) ndi kutukula (abwino).
Ərəbcə təfsirlər:
إِذَا رُجَّتِ ٱلۡأَرۡضُ رَجّٗا
Nthaka ikadzagwedezeka kwamphamvu.
Ərəbcə təfsirlər:
وَبُسَّتِ ٱلۡجِبَالُ بَسّٗا
Ndipo mapiri akadzaperedwaperedwa.
Ərəbcə təfsirlər:
فَكَانَتۡ هَبَآءٗ مُّنۢبَثّٗا
Nkukhala fumbi longouluka.
Ərəbcə təfsirlər:
وَكُنتُمۡ أَزۡوَٰجٗا ثَلَٰثَةٗ
Choncho, inu mudzakhala m’magulu atatu (kulingana ndi zochita zanu).
Ərəbcə təfsirlər:
فَأَصۡحَٰبُ ٱلۡمَيۡمَنَةِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَيۡمَنَةِ
Anthu akumanja (abwino;) taonani kukula kwa ulemelero wa anthu akumanja!
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَصۡحَٰبُ ٱلۡمَشۡـَٔمَةِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَشۡـَٔمَةِ
Ndi anthu akumanzere (oipa;) taonani kuipa khalidwe la anthu akumanzere!
Ərəbcə təfsirlər:
وَٱلسَّٰبِقُونَ ٱلسَّٰبِقُونَ
Ndipo otsogola (pochita zabwino pa dziko) adzakhalanso otsogola (polandira ulemu tsiku lachimaliziro).
Ərəbcə təfsirlər:
أُوْلَٰٓئِكَ ٱلۡمُقَرَّبُونَ
Iwowo ndioyandikitsidwa (kwa Allah).
Ərəbcə təfsirlər:
فِي جَنَّٰتِ ٱلنَّعِيمِ
M’minda yamtendere.
Ərəbcə təfsirlər:
ثُلَّةٞ مِّنَ ٱلۡأَوَّلِينَ
(Iwowo oyandikitsidwawo), gulu lalikulu lochokera kumibadwo yakale.
Ərəbcə təfsirlər:
وَقَلِيلٞ مِّنَ ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndipo ochepa ochokera ku mbadwo wotsirizira.
Ərəbcə təfsirlər:
عَلَىٰ سُرُرٖ مَّوۡضُونَةٖ
Uku ali m’makama (m’mabedi) olukidwa ndi zingwe zagolide,
Ərəbcə təfsirlər:
مُّتَّكِـِٔينَ عَلَيۡهَا مُتَقَٰبِلِينَ
Atatsamira m’makamawo uku akuyang’anizana (mwachikondi).
Ərəbcə təfsirlər:
يَطُوفُ عَلَيۡهِمۡ وِلۡدَٰنٞ مُّخَلَّدُونَ
Anyamata osasintha adzakhala akuwazungulira iwo (ndi kuwatumikira).
Ərəbcə təfsirlər:
بِأَكۡوَابٖ وَأَبَارِيقَ وَكَأۡسٖ مِّن مَّعِينٖ
Uku atatenga matambula ndi maketulo (odzaza ndi zakumwa za ku Jannah), ndi zipanda zodzaza ndi zakumwa zochokera mu akasupe oyenda;
Ərəbcə təfsirlər:
لَّا يُصَدَّعُونَ عَنۡهَا وَلَا يُنزِفُونَ
(Zakumwa zake) zosapweteketsa mutu ndiponso zosaledzeretsa;
Ərəbcə təfsirlər:
وَفَٰكِهَةٖ مِّمَّا يَتَخَيَّرُونَ
Ndi zipatso (zamitundumitundu) zimene azikazisankha;
Ərəbcə təfsirlər:
وَلَحۡمِ طَيۡرٖ مِّمَّا يَشۡتَهُونَ
Ndi nyama yambalame imene mitima yawo izikafuna;
Ərəbcə təfsirlər:
وَحُورٌ عِينٞ
Ndi akazi ophanuka maso mokongola,
Ərəbcə təfsirlər:
كَأَمۡثَٰلِ ٱللُّؤۡلُوِٕ ٱلۡمَكۡنُونِ
(Kukongola kwawo) ndiye ngati ngale zosungidwa bwino mzigoba zake.
Ərəbcə təfsirlər:
جَزَآءَۢ بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Kukhala mphoto chifukwa cha zimene amachita (zabwino padziko lapansi).
Ərəbcə təfsirlər:
لَا يَسۡمَعُونَ فِيهَا لَغۡوٗا وَلَا تَأۡثِيمًا
M’menemo sakamva mawu achabe ngakhale (mawu a) machimo,
Ərəbcə təfsirlər:
إِلَّا قِيلٗا سَلَٰمٗا سَلَٰمٗا
Koma mawu oti: “Mtendere! Mtendere!”
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَصۡحَٰبُ ٱلۡيَمِينِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلۡيَمِينِ
Anthu akudzanja lamanja. Taonani kukula malipiro a anthu akudzanja lamanja!
Ərəbcə təfsirlər:
فِي سِدۡرٖ مَّخۡضُودٖ
(Adzakhala m’mithunzi ya) mitengo ya masawu yopanda minga.
Ərəbcə təfsirlər:
وَطَلۡحٖ مَّنضُودٖ
Ndi mitengo ya nthochi yobereka kwambiri.
Ərəbcə təfsirlər:
وَظِلّٖ مَّمۡدُودٖ
Ndi m’mithunzi yotambasuka kwambiri, yosachoka,
Ərəbcə təfsirlər:
وَمَآءٖ مَّسۡكُوبٖ
Ndi madzi oyenda mosalekeza,
Ərəbcə təfsirlər:
وَفَٰكِهَةٖ كَثِيرَةٖ
Ndi zipatso zambiri,
Ərəbcə təfsirlər:
لَّا مَقۡطُوعَةٖ وَلَا مَمۡنُوعَةٖ
Zopezeka mnyengo zonse, ndiponso zosaletsedwa (kwa amene akuzifuna).
Ərəbcə təfsirlər:
وَفُرُشٖ مَّرۡفُوعَةٍ
Ndi zoyala zapamwamba (zawofuwofu).
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّآ أَنشَأۡنَٰهُنَّ إِنشَآءٗ
Ndithu tidzawalenga (akazi okhulupirira) m’kalengedwe kapamwamba.
Ərəbcə təfsirlər:
فَجَعَلۡنَٰهُنَّ أَبۡكَارًا
Tidzawapanga kukhala anamwali.
Ərəbcə təfsirlər:
عُرُبًا أَتۡرَابٗا
Okondedwa ndi amuna awo; ofanana misinkhu,
Ərəbcə təfsirlər:
لِّأَصۡحَٰبِ ٱلۡيَمِينِ
A anthu akudzanja la manja.
Ərəbcə təfsirlər:
ثُلَّةٞ مِّنَ ٱلۡأَوَّلِينَ
Gulu lalikulu lochokera ku m’badwo woyamba.
Ərəbcə təfsirlər:
وَثُلَّةٞ مِّنَ ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndiponso gulu lalikulu lochokera ku mibadwo yotsiriza.
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَصۡحَٰبُ ٱلشِّمَالِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلشِّمَالِ
Anthu akudzanja lakumanzere. Taonani chilango choopsa kwa anthu akudzanja lakumanzere!
Ərəbcə təfsirlər:
فِي سَمُومٖ وَحَمِيمٖ
Adzakhala mu mvuchi wamoto ndi m’madzi owira.
Ərəbcə təfsirlər:
وَظِلّٖ مِّن يَحۡمُومٖ
Ndi mumthunzi wa utsi wakuda.
Ərəbcə təfsirlər:
لَّا بَارِدٖ وَلَا كَرِيمٍ
Siwoziziritsa ndiponso siwosangalatsa.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّهُمۡ كَانُواْ قَبۡلَ ذَٰلِكَ مُتۡرَفِينَ
Ndithu iwo amakhala kalelo mosangalala (samalabadira kumvera Allah),
Ərəbcə təfsirlər:
وَكَانُواْ يُصِرُّونَ عَلَى ٱلۡحِنثِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo amapitiriza kuchita machimo aakulu (polinga kuti palibe kuuka ku imfa).
Ərəbcə təfsirlər:
وَكَانُواْ يَقُولُونَ أَئِذَا مِتۡنَا وَكُنَّا تُرَابٗا وَعِظَٰمًا أَءِنَّا لَمَبۡعُوثُونَ
Ndipo amanena (motsutsa); “Kodi tikadzafa nkusanduka fumbi ndi mafupa ofumbwa, tidzaukitsidwanso?”
Ərəbcə təfsirlər:
أَوَءَابَآؤُنَا ٱلۡأَوَّلُونَ
“Kodi ndi makolo athu akale (adzaukitsidwanso!)”
Ərəbcə təfsirlər:
قُلۡ إِنَّ ٱلۡأَوَّلِينَ وَٱلۡأٓخِرِينَ
Nena kwa iwo (poyankha kutsutsa kwawo). Ndithudi, amibadwo yoyamba ndi mibadwo yomaliza (omwe inu muli m’gulu lawo),
Ərəbcə təfsirlər:
لَمَجۡمُوعُونَ إِلَىٰ مِيقَٰتِ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Adzasonkhanitsidwa m’nthawi ya tsiku lomwe lakhazikitsidwa.
Ərəbcə təfsirlər:
ثُمَّ إِنَّكُمۡ أَيُّهَا ٱلضَّآلُّونَ ٱلۡمُكَذِّبُونَ
Kenako inu osokera (njira yachilungamo), otsutsa (za kuuka,)
Ərəbcə təfsirlər:
لَأٓكِلُونَ مِن شَجَرٖ مِّن زَقُّومٖ
Mudzadya (ku Jahannam) mtengo wa Zakkum, (mtengo wowawa wopezeka mu Jahannam).
Ərəbcə təfsirlər:
فَمَالِـُٔونَ مِنۡهَا ٱلۡبُطُونَ
Mudzakhutitsa mimba zanu ndi umenewu (chifukwa cha njala yadzaoneni).
Ərəbcə təfsirlər:
فَشَٰرِبُونَ عَلَيۡهِ مِنَ ٱلۡحَمِيمِ
(Mkhuto wa mtengowo) adzamwera madzi owira;
Ərəbcə təfsirlər:
فَشَٰرِبُونَ شُرۡبَ ٱلۡهِيمِ
Adzamwa monga mmene imamwera ngamira yodwala matenda aludzu!
Ərəbcə təfsirlər:
هَٰذَا نُزُلُهُمۡ يَوۡمَ ٱلدِّينِ
Ili ndi phwando lawo tsiku lamalipiro.
Ərəbcə təfsirlər:
نَحۡنُ خَلَقۡنَٰكُمۡ فَلَوۡلَا تُصَدِّقُونَ
Ife tidakulengani kodi nchifukwa ninji simukukhulupirira?
Ərəbcə təfsirlər:
أَفَرَءَيۡتُم مَّا تُمۡنُونَ
Tandiuzani za madzi (ambewu ya munthu) amene mumawathira m’chiberekero,
Ərəbcə təfsirlər:
ءَأَنتُمۡ تَخۡلُقُونَهُۥٓ أَمۡ نَحۡنُ ٱلۡخَٰلِقُونَ
Kodi inu ndiamene mumawalenga (madziwo ndi kumayang’anira mkusinthasintha kwake kuti akhale cholengedwa) kapena Ife ndiamene timawalenga?
Ərəbcə təfsirlər:
نَحۡنُ قَدَّرۡنَا بَيۡنَكُمُ ٱلۡمَوۡتَ وَمَا نَحۡنُ بِمَسۡبُوقِينَ
Ife tidalamula imfa pakati panu ndipo Ife sitili wolephera,
Ərəbcə təfsirlər:
عَلَىٰٓ أَن نُّبَدِّلَ أَمۡثَٰلَكُمۡ وَنُنشِئَكُمۡ فِي مَا لَا تَعۡلَمُونَ
Kubweretsa ena m’malo mwanu ndi kukulengani mwamaonekedwe ena omwe simumawadziwa.
Ərəbcə təfsirlər:
وَلَقَدۡ عَلِمۡتُمُ ٱلنَّشۡأَةَ ٱلۡأُولَىٰ فَلَوۡلَا تَذَكَّرُونَ
Ndipo ndithu mukdziwa kalengedwe koyamba; nanga bwanji simukukumbukira.
Ərəbcə təfsirlər:
أَفَرَءَيۡتُم مَّا تَحۡرُثُونَ
Tandiuzani za zimene mukubzala?
Ərəbcə təfsirlər:
ءَأَنتُمۡ تَزۡرَعُونَهُۥٓ أَمۡ نَحۡنُ ٱلزَّٰرِعُونَ
Kodi ndinu amene mukuzimeretsa kapena ndife Amene tikuzimeretsa?
Ərəbcə təfsirlər:
لَوۡ نَشَآءُ لَجَعَلۡنَٰهُ حُطَٰمٗا فَظَلۡتُمۡ تَفَكَّهُونَ
Tikadafuna tikadazitembenuza (mbewu zimenezo kukhala zouma isanakwane nthawi yake yozithyola) choncho mukadakhala mukudandaula.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّا لَمُغۡرَمُونَ
(Uku mukunena:) “Ndithu ife tangotaya chuma chathu (padera);”
Ərəbcə təfsirlər:
بَلۡ نَحۡنُ مَحۡرُومُونَ
“Koma ife tamanidwa (phindu la khama lathu).”
Ərəbcə təfsirlər:
أَفَرَءَيۡتُمُ ٱلۡمَآءَ ٱلَّذِي تَشۡرَبُونَ
Kodi mukuwaona madzi amene mukumwa!
Ərəbcə təfsirlər:
ءَأَنتُمۡ أَنزَلۡتُمُوهُ مِنَ ٱلۡمُزۡنِ أَمۡ نَحۡنُ ٱلۡمُنزِلُونَ
Kodi ndinu amene mudawatsitsa ku mitambo kapena ndife Amene timawatsitsa?
Ərəbcə təfsirlər:
لَوۡ نَشَآءُ جَعَلۡنَٰهُ أُجَاجٗا فَلَوۡلَا تَشۡكُرُونَ
Tikadafuna tikadawapanga kukhala amchere; nanga nchifukwa ninji simuthokoza?
Ərəbcə təfsirlər:
أَفَرَءَيۡتُمُ ٱلنَّارَ ٱلَّتِي تُورُونَ
Kodi mukuwuona moto umene mumaukoleza?
Ərəbcə təfsirlər:
ءَأَنتُمۡ أَنشَأۡتُمۡ شَجَرَتَهَآ أَمۡ نَحۡنُ ٱلۡمُنشِـُٔونَ
Kodi ndinu amene mudameretsa mitengo yake kapena Ndife tidaipanga?
Ərəbcə təfsirlər:
نَحۡنُ جَعَلۡنَٰهَا تَذۡكِرَةٗ وَمَتَٰعٗا لِّلۡمُقۡوِينَ
Ife taupanga kuti ukhale chikumbutso (cha Moto watsiku lachimaliziro akauona), ndikuti ukhale chothandiza kwa anthu apaulendo (amene akuyenda m’chipululu).
Ərəbcə təfsirlər:
فَسَبِّحۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلۡعَظِيمِ
Choncho, pitiriza kulemekeza dzina la Mbuye wako Wamkulu.
Ərəbcə təfsirlər:
۞ فَلَآ أُقۡسِمُ بِمَوَٰقِعِ ٱلنُّجُومِ
Ndikulumbilira motsimikiza, mmene mumatsikira nyenyezi (pomwe zikulowa).
Ərəbcə təfsirlər:
وَإِنَّهُۥ لَقَسَمٞ لَّوۡ تَعۡلَمُونَ عَظِيمٌ
Ndithu kulumbira uku, mukadakhala olingalira, nkwakukulu kwabasi (pazimene kukusonya).
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّهُۥ لَقُرۡءَانٞ كَرِيمٞ
Ndithu iyi ndi Qur’an yolemekezeka (ndipo mkati mwake muli zithandizo zambiri).
Ərəbcə təfsirlər:
فِي كِتَٰبٖ مَّكۡنُونٖ
Idachokera mu buku lotetezedwa.
Ərəbcə təfsirlər:
لَّا يَمَسُّهُۥٓ إِلَّا ٱلۡمُطَهَّرُونَ
Salikhudza kupatula okhawo oyeretsedwa (angelo).
Ərəbcə təfsirlər:
تَنزِيلٞ مِّن رَّبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Chivumbulutso chochokera kwa Mbuye wa zolengedwa zonse.
Ərəbcə təfsirlər:
أَفَبِهَٰذَا ٱلۡحَدِيثِ أَنتُم مُّدۡهِنُونَ
Kodi nkhani iyi (ya Qur’an) ndiyomwe inu mukuinyozera?
Ərəbcə təfsirlər:
وَتَجۡعَلُونَ رِزۡقَكُمۡ أَنَّكُمۡ تُكَذِّبُونَ
Kodi mwakuchita kukanira kukhala kuthokoza kwanu pa zimene wakupatsani?
Ərəbcə təfsirlər:
فَلَوۡلَآ إِذَا بَلَغَتِ ٱلۡحُلۡقُومَ
Mmaona bwanji (mzimu wa mmodzi wa inu) ukafika kummero (panthawi ya imfa).
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَنتُمۡ حِينَئِذٖ تَنظُرُونَ
Uku inu panthawi imeneyo mukuona zimenezo.
Ərəbcə təfsirlər:
وَنَحۡنُ أَقۡرَبُ إِلَيۡهِ مِنكُمۡ وَلَٰكِن لَّا تُبۡصِرُونَ
Pomwe Ife tili pafupi ndi iye kuposa inu, koma inu simuona,
Ərəbcə təfsirlər:
فَلَوۡلَآ إِن كُنتُمۡ غَيۡرَ مَدِينِينَ
Mukadakhala kuti simuzalipidwa (pa zomwe mukuchita),
Ərəbcə təfsirlər:
تَرۡجِعُونَهَآ إِن كُنتُمۡ صَٰدِقِينَ
Bwenzi mukuubweza (mzimuwo) ngati mukunena zoona.
Ərəbcə təfsirlər:
فَأَمَّآ إِن كَانَ مِنَ ٱلۡمُقَرَّبِينَ
Ngati (amene yamfikira imfayo) adali mmodzi wa woyandikitsidwa (kwa Allah;)
Ərəbcə təfsirlər:
فَرَوۡحٞ وَرَيۡحَانٞ وَجَنَّتُ نَعِيمٖ
Kobwerera kwake ndi kumpumulo ndi mtendere ndi kupatsidwa zonunkhira ndiponso Munda wamtendere.
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَمَّآ إِن كَانَ مِنۡ أَصۡحَٰبِ ٱلۡيَمِينِ
Ndipo ngati adali mmodzi wa anthu akudzanja lamanja,
Ərəbcə təfsirlər:
فَسَلَٰمٞ لَّكَ مِنۡ أَصۡحَٰبِ ٱلۡيَمِينِ
(Kudzanenedwa kwa iye:) “Mtendere ukhale pa iwe, amene udali m’gulu la anthu akudzanja lakumanja (anthu abwino).”
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَمَّآ إِن كَانَ مِنَ ٱلۡمُكَذِّبِينَ ٱلضَّآلِّينَ
Koma ngati adali mmodzi wa anthu otsutsa, osokera,
Ərəbcə təfsirlər:
فَنُزُلٞ مِّنۡ حَمِيمٖ
Phwando lamadzi owira (ndilake).
Ərəbcə təfsirlər:
وَتَصۡلِيَةُ جَحِيمٍ
Ndi kupsa m’moto wa Jahena.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّ هَٰذَا لَهُوَ حَقُّ ٱلۡيَقِينِ
Ndithu izi ndizoona, zotsimikizika.
Ərəbcə təfsirlər:
فَسَبِّحۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلۡعَظِيمِ
Choncho lemekeza dzina la Mbuye wako Wamkulu.
Ərəbcə təfsirlər:
 
Mənaların tərcüməsi Surə: əl-Vaqiə
Surələrin mündəricatı Səhifənin rəqəmi
 
Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Tərcumənin mündəricatı

Qurani Kərimin şişyo dilinə mənaca tərcüməsi. Tərcüməçi:

Bağlamaq