Check out the new design

قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا * - ترجمے کی لسٹ


معانی کا ترجمہ سورت: واقعہ   آیت:

Al-Wâqi’ah

إِذَا وَقَعَتِ ٱلۡوَاقِعَةُ
Chikadzachitika chochitikacho (Qiyâma).
عربی تفاسیر:
لَيۡسَ لِوَقۡعَتِهَا كَاذِبَةٌ
Palibe wotsutsa za kuchitika kwake.
عربی تفاسیر:
خَافِضَةٞ رَّافِعَةٌ
Chidzatsitsa (oipa) ndi kutukula (abwino).
عربی تفاسیر:
إِذَا رُجَّتِ ٱلۡأَرۡضُ رَجّٗا
Nthaka ikadzagwedezeka kwamphamvu.
عربی تفاسیر:
وَبُسَّتِ ٱلۡجِبَالُ بَسّٗا
Ndipo mapiri akadzaperedwaperedwa.
عربی تفاسیر:
فَكَانَتۡ هَبَآءٗ مُّنۢبَثّٗا
Nkukhala fumbi longouluka.
عربی تفاسیر:
وَكُنتُمۡ أَزۡوَٰجٗا ثَلَٰثَةٗ
Choncho, inu mudzakhala m’magulu atatu (kulingana ndi zochita zanu).
عربی تفاسیر:
فَأَصۡحَٰبُ ٱلۡمَيۡمَنَةِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَيۡمَنَةِ
Anthu akumanja (abwino;) taonani kukula kwa ulemelero wa anthu akumanja!
عربی تفاسیر:
وَأَصۡحَٰبُ ٱلۡمَشۡـَٔمَةِ مَآ أَصۡحَٰبُ ٱلۡمَشۡـَٔمَةِ
Ndi anthu akumanzere (oipa;) taonani kuipa khalidwe la anthu akumanzere!
عربی تفاسیر:
وَٱلسَّٰبِقُونَ ٱلسَّٰبِقُونَ
Ndipo otsogola (pochita zabwino pa dziko) adzakhalanso otsogola (polandira ulemu tsiku lachimaliziro).
عربی تفاسیر:
أُوْلَٰٓئِكَ ٱلۡمُقَرَّبُونَ
Iwowo ndioyandikitsidwa (kwa Allah).
عربی تفاسیر:
فِي جَنَّٰتِ ٱلنَّعِيمِ
M’minda yamtendere.
عربی تفاسیر:
ثُلَّةٞ مِّنَ ٱلۡأَوَّلِينَ
(Iwowo oyandikitsidwawo), gulu lalikulu lochokera kumibadwo yakale.
عربی تفاسیر:
وَقَلِيلٞ مِّنَ ٱلۡأٓخِرِينَ
Ndipo ochepa ochokera ku mbadwo wotsirizira.
عربی تفاسیر:
عَلَىٰ سُرُرٖ مَّوۡضُونَةٖ
Uku ali m’makama (m’mabedi) olukidwa ndi zingwe zagolide,
عربی تفاسیر:
مُّتَّكِـِٔينَ عَلَيۡهَا مُتَقَٰبِلِينَ
Atatsamira m’makamawo uku akuyang’anizana (mwachikondi).
عربی تفاسیر:
 
معانی کا ترجمہ سورت: واقعہ
سورتوں کی لسٹ صفحہ نمبر
 
قرآن کریم کے معانی کا ترجمہ - چیچیوا ترجمہ - خالد ابراہیم بتیالا - ترجمے کی لسٹ

خالد ابراہیم پیٹالا نے ترجمہ کیا۔

بند کریں