Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Ajet: (204) Sura: Sura el-Bekara
وَمِنَ ٱلنَّاسِ مَن يُعۡجِبُكَ قَوۡلُهُۥ فِي ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا وَيُشۡهِدُ ٱللَّهَ عَلَىٰ مَا فِي قَلۡبِهِۦ وَهُوَ أَلَدُّ ٱلۡخِصَامِ
Ndipo mwa anthu alipo amene zoyankhula zake zikukondweretsa (iwe) pano pa dziko la pansi, (koma tsiku lachimaliziro kuipa kwake kudzadziwika). Ndipo iye akutsimikizira Allah kuti akhale mboni pa zomwe zili mu mtima mwake pomwe iye ndi wa makani kwambiri.[25]
[25] Tanthauzo lake nkuti alipo ena mwa anthu omwe angakukometsere zoyankhula zawo ndi kuthwa kwa lirime lawo pomwe iwo chikhalirecho akungoyankhula kuti apeze zinthu za m’dziko.
Ndimeyi ikufotokoza za Al-Akhnas bun Sharik yemwe amati akakumana ndi Mtumiki (s.a.w), amatamanda ndi kusonyeza chikhulupiliro chabodza. Koma akachoka pamaso pa mtumiki (s.a.w) amayenda pa dziko ncholinga choononga.
Umo ndi momwe alili makhalidwe a anthu ena, amangokometsa mawu pomwe zochita zawo nzauve. Tero tichenjere ndi anthu otere.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Ajet: (204) Sura: Sura el-Bekara
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا - Sadržaj prijevodā

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Zatvaranje